< Yeremiya 50 >

1 Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
Asɛm a Awurade nam odiyifo Yeremia so ka faa Babilonia ne Babiloniafo asase ho ni:
2 “Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina, kweza mbendera ndipo ulengeze; usabise kanthu, koma uwawuze kuti, ‘Babuloni wagwa; mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi, nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha. Milungu yake yagwidwa ndi mantha ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
“Mommɔ no dawuru na mompae mu nka wɔ amanaman mu. Momma frankaa so na mompae mu nka; na momma wɔnte sɛ, ‘Wɔbɛfa Babilonia; wobegu Bel anim ase, na ehu bɛhyɛ Merodak ma. Wobegu ne nsɛsode anim ase na ehu bɛhyɛ nʼahoni ma.’
3 Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni ndi kusandutsa bwinja dziko lake. Kumeneko sikudzakhalanso munthu kapena nyama.
Ɔman bi fi atifi fam bɛtow ahyɛ ne so na wɔbɛyɛ nʼasase amamfo. Obiara rentena so; nnipa ne mmoa beguan afi so.
4 “Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
“Nna no mu ne saa bere no,” Awurade na ose, “Israelfo ne Yudafo bɛka abɔ mu de nusu akɔhwehwɛ wɔn Awurade, wɔn Nyankopɔn.
5 Adzafunsa njira ya ku Ziyoni ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko. Iwo adzadzipereka kwa Yehova pochita naye pangano lamuyaya limene silidzayiwalika.
Wobebisa ɔkwan a ɛkɔ Sion na wɔde wɔn ani akyerɛ hɔ. Wɔbɛba de wɔn ho abɛbɔ Awurade wɔ daa apam a werɛ remfi mu.
6 “Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika; abusa awo anawasocheretsa mʼmapiri. Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda mpaka kuyiwala kwawo.
“Me nkurɔfo ayɛ nguan a wɔayera; wɔn nguanhwɛfo ama wɔafom ɔkwan ma wokyinkyin mmepɔw so. Wokyinkyin bepɔw ne koko so na wɔn werɛ fii wɔn ankasa homebea.
7 Aliyense amene anawapeza anawawononga; adani awo anati, ‘Ife si olakwa, chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
Obiara a ohuu wɔn no tetew wɔn mu: wɔn atamfo kae se, ‘Yenni fɔ, efisɛ wɔyɛɛ bɔne tiaa Awurade, wɔn nokware didibea no, Awurade wɔn agyanom anidaso no.’
8 “Thawaniko ku Babuloni; chokani mʼdziko la Ababuloni. Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
“Munguan mfi Babilonia; mumfi Babiloniafo asase so, na monyɛ sɛ mpapo a wodi nguankuw anim.
9 Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto kudzamenyana ndi Babuloni. Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni. Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso, yosapita padera.
Mɛkanyan amanaman akɛse nkabom afi atifi fam asase so de wɔn abɛko atia Babilonia. Wobegyinagyina wɔn afa atia no, wobefi atifi fam ako afa no. Wɔn agyan bɛyɛ sɛ dɔmmarima a wɔakwadaw akodi mu, wɔn a wɔmmfa nsapan nsan wɔn akyi.
10 Motero Ababuloni adzafunkhidwa; ndipo onse omufunkha adzakhuta,” akutero Yehova.
Enti wɔbɛfow Babilonia; wɔn a wɔfow no nyinaa benya asade bebree,” Awurade na ose.
11 “Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika. Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala. Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
“Esiane sɛ mo ani gye na mudi ahurusi, mo a mofow mʼagyapade, sɛ muhuruhuruw anigye so te sɛ nantwiforo a ɔwɔ sare frɔmfrɔm mu na musu te sɛ apɔnkɔnini nti,
12 Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri. Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa. Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse. Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
wo na ani bewu pa ara; nea ɔwoo wo anim begu ase. Ɔbɛyɛ akumaa wɔ amanaman no mu, sare, asase wosee ne nweatam.
13 Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu ndipo adzakhala chipululu chokhachokha. Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
Awurade abufuw nti, obiara rentena hɔ na ɛbɛda mpan korakora. Wɔn a wotwa mu wɔ Babilonia nyinaa ho bedwiriw wɔn na wɔadi ne ho fɛw esiane nʼapirakuru nyinaa nti.
14 “Inu okoka uta, konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse. Muponyereni mivi yanu yonse chifukwa anachimwira Yehova.
“Munnyinagyina mo afa ntwa Babilonia ho nhyia, mo a motow agyan nyinaa. Montow no! Munnyaw bɛmma biara, efisɛ wayɛ bɔne atia Awurade.
15 Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja. Nsanja zake zagwa. Malinga ake agwetsedwa. Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova. Mulipsireni, mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
Monteɛ mu ntia no wɔ afanan nyinaa! Ɔma ne nsa so, nʼabandennen bubu, wodwiriw nʼafasu gu fam. Esiane sɛ eyi yɛ Awurade aweretɔ no nti, montɔ ne so were; monyɛ no sɛnea wayɛ afoforo no.
16 Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense, ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola. Poona lupanga la ozunza anzawo, aliyense adzabwerera kwa anthu ake; adzathawira ku dziko la kwawo.
Munyi ogufo mfi Babilonia, ɔne otwafo a okura ne kantankrankyi wɔ otwabere mu no. Esiane nhyɛsofo no afoa nti obiara nsan nkɔ ne nkurɔfo mu, obiara nguan nkɔ nʼankasa asase so.
17 “Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika pothamangitsidwa ndi mikango. Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo. Wotsiriza anali Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
“Israel yɛ nguankuw a wɔahwete a gyata apam wɔn. Nea odii kan tetew ne mu yɛ Asiriahene; na nea ɔdwerɛwee ne nnompe akyiri no yɛ Babiloniahene Nebukadnessar.”
18 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
Ɛno nti, sɛɛ na Asafo Awurade, Israel Nyankopɔn se: “Mɛtwe Babiloniahene ne nʼasase aso sɛnea metwee Asiriahene aso no.
19 Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani; adzadya nakhuta ku mapiri a ku Efereimu ndi Giliyadi.
Na mede Israel bɛsan aba nʼankasa didibea, na obedidi wɔ Karmel ne Basan; ɔbɛmee wɔ Efraim ne Gilead nkoko so.
20 Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe, ndipo adzafufuza machimo a Yuda, koma sadzapeza ndi limodzi lomwe, chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
Saa nna no ne saa bere no,” Awurade na ose, “Wɔbɛhwehwɛ Israel afɔbu mu, nanso wɔrennya bi, wɔbɛhwehwɛ Yuda nnebɔne mu, nanso wɔrenhu bi, efisɛ, mede nkae a migyaa wɔn no bɔne bɛkyɛ wɔn.
21 “Lithireni nkhondo dziko la Merataimu ndi anthu okhala ku Pekodi. Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,” akutero Yehova. “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
“Montow nhyɛ Merataim asase so ne nnipa a wɔte Pekod. Montaa wɔn, munkunkum wɔn na monsɛe wɔn korakora,” Awurade na ose. “Monyɛ biribiara a mahyɛ mo no.
22 Mʼdziko muli phokoso la nkhondo, phokoso la chiwonongeko chachikulu!
Ɔko mu gyegyeegye wɔ asase no so, ɔsɛe kɛse nnyigyei!
23 Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi. Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ina!
Hwɛ sɛnea wɔabubu na wɔabobɔ asase nyinaa so asae! Hwɛ sɛnea Babilonia ada mpan wɔ amanaman no mu!
24 Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.
Misum wo afiri, Babilonia, na eyii wo ansa na worehu; wohuu wo kyeree wo efisɛ woko tiaa Awurade.
25 Yehova watsekula nyumba ya zida zake ndipo watulutsa zida za ukali wake, pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire mʼdziko la Ababuloni.
Otumfo Awurade abue nʼakode adekoradan na wayi nʼabufuwhyew akode de apue, efisɛ Asafo Awurade wɔ adwuma yɛ wɔ Babiloniafo asase so.
26 Mumenyane naye Babuloni mbali zonse. Anthu ake muwawunjike ngati milu ya tirigu. Muwawononge kotheratu ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
Mumfi akyirikyiri mmra ne so. Mummubu nʼasan no ani; monhɔre no siw sɛ awi akuwakuw. Monsɛe no korakora na munnyaw nkae biara mma no.
27 Iphani ankhondo ake onse. Onse aphedwe ndithu. Tsoka lawagwera pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
Munkunkum nʼanatwinini nyinaa; momfa wɔn nkɔ mma wonkokum wɔn! Mmusu nka wɔn! Efisɛ wɔn da no adu, bere a wɔde bɛtwe wɔn aso no.
28 Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni akulengeza mu Yerusalemu za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu. Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
Muntie akobɔfo ne aguanfo a wofi Babilonia no sɛ wɔreka wɔ Sion sɛnea Awurade, yɛn Nyankopɔn atɔ were, nʼasɔrefi ho aweretɔ.
29 “Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni. Muyitanenso onse amene amakoka mauta. Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira; musalole munthu aliyense kuthawa. Muchiteni monga momwe iye anachitira anthu ena. Iyeyu ananyoza Yehova, Woyera wa Israeli.
“Momfrɛ agyantowfo nkɔtoa Babilonia, wɔn a wɔtow agyan nyinaa. Muntwa ne ho nhyia; mommma obiara nguan. Muntua ne nneyɛe so ka; monyɛ no sɛnea wayɛ. Efisɛ wabu Awurade animtiaa, Israel kronkronni no.
30 Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake; ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova.
Enti ne mmerante bɛtotɔ wɔ mmɔnten so; wɔbɛtɔre nʼasraafo nyinaa ase saa da no,” Awurade na ose.
31 “Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, “chifukwa tsiku lako lafika, nthawi yoti ndikulange yakwana.
“Hwɛ, mikyi wo; ɔhantanni.” Awurade, Asafo Awurade na ose, “efisɛ wo da no adu bere a wɔde bɛtwe wʼaso no.
32 Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa ndipo palibe amene adzakudzutse; ndidzayatsa moto mʼmizinda yake umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
Ɔhantanni no behintiw na wahwe ase, obiara remmoa no mma ɔnnsɔre; mɛto ne nkurow mu gya na ahyew wɔn a atwa ne ho ahyia nyinaa.”
33 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a ku Israeli akuzunzidwa, pamodzi ndi anthu a ku Yuda, ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa, akukana kuwamasula.
Sɛɛ na Asafo Awurade se: “Wɔhyɛ Israelfo so, na Yudafo nso saa ara. Wɔn nnommumfafo no kura wɔn dennen a wɔmpɛ sɛ wogyaa wɔn ma wɔkɔ.
34 Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo, koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
Nanso wɔn Gyefo yɛ ɔhoɔdenfo; ne din ne Asafo Awurade. Obedi wɔn asɛm ama wɔn anibere so, sɛnea ɔde ahotɔ bɛba wɔn asase no so, na wɔn a wɔte Babilonia no nea wahyɛ wɔn ahometew.
35 Yehova akuti, “Imfa yalunjika pa Ababuloni, pa akuluakulu ake ndi pa anthu ake a nzeru!
“Afoa a etia Babiloniafo!” Awurade na ose, “etia wɔn a wɔte Babilonia na etia nʼadwumayɛfo ne nʼanyansafo!
36 Imfa yalunjika pa aneneri abodza kuti asanduke zitsiru. Imfa yalunjika pa ankhondo ake kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
Afoa a etia nʼatoro adiyifo! Wɔbɛdan nkwaseafo. Afoa a etia nʼakofo! Ehu bɛhyɛ wɔn ma.
37 Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake. Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo kuti asanduke ngati akazi. Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake kuti chidzafunkhidwe.
Afoa a etia nʼapɔnkɔ ne ne nteaseɛnam ne ananafo a wɔwɔ wɔn mu nyinaa! Wɔbɛdan mmea. Afoa a etia nʼademude! Wɔbɛfom.
38 Chilala chilunjike pa madzi ake kuti aphwe. Babuloni ndi dziko la mafano, ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
Ɔyow wɔ nʼasu ahorow so! Ɛbɛyoyow. Efisɛ ɛyɛ ahoni asase, ahoni a ehu bɛma wɔabobɔ adam.
39 “Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko ndipo kudzakhalanso akadzidzi. Kumeneko sikudzapezekako anthu, ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
“Enti sare so mmoa ne mpataku bɛtena hɔ, na ɛhɔ na patu bɛtena. Obiara rentena so bio efi awo ntoatoaso kosi awo ntoatoaso.
40 Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,” akutero Yehova, “momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko; anthu sadzayendanso mʼmenemo.
Sɛnea Onyankopɔn tuu Sodom ne Gomora ne wɔn nkurow gui no,” Awurade na ose, “saa ara na obiara rentena hɔ; onipa biara rentena mu.
41 “Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri, wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
“Monhwɛ! Asraafo bi fi atifi fam reba; ɔman kɛse ne ahemfo bebree, wɔrehwanyan wɔn afi nsase ano.
42 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo. Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo, ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo iwe Babuloni.
Wokurakura bɛmma ne mpeaw; wɔn tirim yɛ den, na wonni ahummɔbɔ. Wɔn nnyigyei te sɛ po a ɛworo so. Sɛ wɔtete wɔn apɔnkɔ so a, wɔba sɛ mmarima a wɔrekɔ sa abɛtow ahyɛ wo so, Ɔbabea Babilonia.
43 Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo, ndipo yalobodokeratu. Ikuda nkhawa, ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
Babiloniahene ate wɔn ho nsɛm, ne nsa sesa ne ho kwa. Ahohiahia akyekyere no ɔyaw a ɛte sɛ ɔbea a ɔrekyem wɔ awo so.
44 Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani kupita ku msipu wobiriwira, momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi. Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine. Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane? Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
Sɛnea gyata a ofi Yordan nkyɛkyerɛ mu rekɔ adidibea frɔmfrɔm no, saa ara na mɛtaa Babilonia fi nʼasase so wɔ bere tiaa bi mu. Hena ne nea mayi no sɛ ɔnyɛ eyi? Hena na ɔte sɛ me, na hena na obetumi ne me adi asi? Na oguanhwɛfo bɛn na obetumi asɔre atia me?”
45 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Enti tie nea Awurade ahyehyɛ atia Babilonia, nea wabɔ ne tirim sɛ ɔbɛyɛ de atia Babiloniafo asase ni: Nguankuw no mu nkumaa no wɔbɛtwe wɔn akɔ; wɔn nti ɔbɛsɛe adidibea no koraa.
46 Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera, ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Babilonia nnommumfa nnyigyei bɛma asase awosow; ne nteɛteɛmu gyegyeegye wɔ amanaman no mu.

< Yeremiya 50 >