< Yeremiya 50 >

1 Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
کلامی که خداوند درباره بابل و زمین کلدانیان به واسطه ارمیا نبی گفت:۱
2 “Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina, kweza mbendera ndipo ulengeze; usabise kanthu, koma uwawuze kuti, ‘Babuloni wagwa; mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi, nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha. Milungu yake yagwidwa ndi mantha ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
«درمیان امت‌ها اخبار و اعلام نمایید، علمی برافراشته، اعلام نمایید و مخفی مدارید. بگوییدکه بابل گرفتار شده، و بیل خجل گردیده است. مرودک خرد شده و اصنام او رسوا و بتهایش شکسته گردیده است۲
3 Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni ndi kusandutsa bwinja dziko lake. Kumeneko sikudzakhalanso munthu kapena nyama.
زیرا که امتی از طرف شمال بر او می‌آید و زمینش را ویران خواهدساخت به حدی که کسی در آن ساکن نخواهد شدو هم انسان و هم بهایم فرار کرده، خواهند رفت.۳
4 “Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
خداوند می‌گوید که در آن ایام و در آن زمان بنی‌اسرائیل و بنی یهودا با هم خواهند آمد. ایشان گریه‌کنان خواهند آمد و یهوه خدای خود راخواهند طلبید.۴
5 Adzafunsa njira ya ku Ziyoni ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko. Iwo adzadzipereka kwa Yehova pochita naye pangano lamuyaya limene silidzayiwalika.
و رویهای خود را بسوی صهیون نهاده، راه آن را خواهند پرسید و خواهندگفت بیایید و به عهد ابدی که فراموش نشود به خداوند ملصق شویم.۵
6 “Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika; abusa awo anawasocheretsa mʼmapiri. Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda mpaka kuyiwala kwawo.
«قوم من گوسفندان گم شده بودند و شبانان ایشان ایشان را گمراه کرده، بر کوهها آواره ساختند. از کوه به تل رفته، آرامگاه خود رافراموش کردند.۶
7 Aliyense amene anawapeza anawawononga; adani awo anati, ‘Ife si olakwa, chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
هر‌که ایشان را می‌یافت ایشان را می‌خورد و دشمنان ایشان می‌گفتند که گناه نداریم زیرا که به یهوه که مسکن عدالت است و به یهوه که امید پدران ایشان بود، گناه ورزیدند.۷
8 “Thawaniko ku Babuloni; chokani mʼdziko la Ababuloni. Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
ازمیان بابل فرار کنید و از زمین کلدانیان بیرون آیید. و مانند بزهای نر پیش روی گله راه روید.۸
9 Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto kudzamenyana ndi Babuloni. Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni. Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso, yosapita padera.
زیرااینک من جمعیت امت های عظیم را از زمین شمال برمی انگیزانم و ایشان را بر بابل می‌آورم وایشان در برابر آن صف آرایی خواهند نمود و درآنوقت گرفتار خواهد شد. تیرهای ایشان مثل تیرهای جبار هلاک کننده که یکی از آنها خالی برنگردد خواهد بود.۹
10 Motero Ababuloni adzafunkhidwa; ndipo onse omufunkha adzakhuta,” akutero Yehova.
خداوند می‌گوید که کلدانیان تاراج خواهند شد و هر‌که ایشان را غارت نماید سیر خواهد گشت.۱۰
11 “Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika. Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala. Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
زیرا شما‌ای غارت کنندگان میراث من شادی و وجد کردید ومانند گوساله‌ای که خرمن را پایمال کند، جست وخیز نمودید و مانند اسبان زورآور شیهه زدید.۱۱
12 Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri. Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa. Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse. Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
مادر شما بسیار خجل خواهد شد و والده شمارسوا خواهد گردید. هان او موخر امت‌ها و بیابان و زمین خشک و عربه خواهد شد.۱۲
13 Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu ndipo adzakhala chipululu chokhachokha. Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
به‌سبب خشم خداوند مسکون نخواهد شد بلکه بالکل ویران خواهد گشت. و هر‌که از بابل عبور نمایدمتحیر شده، به جهت تمام بلایایش صفیر خواهدزد.۱۳
14 “Inu okoka uta, konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse. Muponyereni mivi yanu yonse chifukwa anachimwira Yehova.
‌ای جمیع کمان داران در برابر بابل از هرطرف صف آرایی نمایید. تیرها بر او بیندازید ودریغ منمایید زیرا به خداوند گناه ورزیده است.۱۴
15 Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja. Nsanja zake zagwa. Malinga ake agwetsedwa. Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova. Mulipsireni, mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
از هر طرف بر او نعره زنید چونکه خویشتن راتسلیم نموده است. حصارهایش افتاده ودیوارهایش منهدم شده است زیرا که این انتقام خداوند است. پس از او انتقام بگیرید و بطوری که او عمل نموده است همچنان با او عمل نمایید.۱۵
16 Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense, ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola. Poona lupanga la ozunza anzawo, aliyense adzabwerera kwa anthu ake; adzathawira ku dziko la kwawo.
و از بابل، برزگران و آنانی را که داس را در زمان درو بکار می‌برند منقطع سازید. و از ترس شمشیر برنده هرکس بسوی قوم خود توجه نماید و هر کس به زمین خویش بگریزد.۱۶
17 “Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika pothamangitsidwa ndi mikango. Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo. Wotsiriza anali Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
«اسرائیل مثل گوسفند، پراکنده گردید. شیران او را تعاقب کردند. اول پادشاه آشور او راخورد و آخر این نبوکدرصر پادشاه بابل استخوانهای او را خرد کرد.»۱۷
18 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
بنابراین یهوه صبایوت خدای اسرائیل چنین می‌گوید: «اینک من بر پادشاه بابل و بر زمین او عقوبت خواهم رسانید چنانکه بر پادشاه آشور عقوبت رسانیدم.۱۸
19 Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani; adzadya nakhuta ku mapiri a ku Efereimu ndi Giliyadi.
و اسرائیل را به مرتع خودش باز خواهم آورد و در کرمل و باشان خواهد چرید و بر کوهستان افرایم و جلعاد جان او سیر خواهد شد.۱۹
20 Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe, ndipo adzafufuza machimo a Yuda, koma sadzapeza ndi limodzi lomwe, chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
خداوند می‌گوید که در آن ایام و در آن زمان عصیان اسرائیل را خواهند جست و نخواهد بودو گناه یهودا را اما پیدا نخواهد شد، زیرا آنانی راکه باقی می‌گذارم خواهم آمرزید.۲۰
21 “Lithireni nkhondo dziko la Merataimu ndi anthu okhala ku Pekodi. Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,” akutero Yehova. “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
«بر زمین مراتایم برآی یعنی بر آن و برساکنان فقود. خداوند می‌گوید: بکش و ایشان راتعاقب نموده، بالکل هلاک کن و موافق هر‌آنچه من تو را امر فرمایم عمل نما.۲۱
22 Mʼdziko muli phokoso la nkhondo, phokoso la chiwonongeko chachikulu!
آواز جنگ وشکست عظیم در زمین است.۲۲
23 Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi. Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ina!
کوپال تمام جهان چگونه بریده و شکسته شده و بابل در میان امت‌ها چگونه ویران گردیده است.۲۳
24 Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.
‌ای بابل ازبرای تو دام گستردم و تو نیز گرفتار شده، اطلاع نداری. یافت شده، تسخیر گشته‌ای چونکه باخداوند مخاصمه نمودی.۲۴
25 Yehova watsekula nyumba ya zida zake ndipo watulutsa zida za ukali wake, pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire mʼdziko la Ababuloni.
خداونداسلحه خانه خود را گشوده، اسلحه خشم خویش را بیرون آورده است. زیرا خداوند یهوه صبایوت با زمین کلدانیان کاری دارد.۲۵
26 Mumenyane naye Babuloni mbali zonse. Anthu ake muwawunjike ngati milu ya tirigu. Muwawononge kotheratu ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
بر او از همه اطراف بیایید و انبارهای او را بگشایید، او را مثل توده های انباشته بالکل هلاک سازید و چیزی ازاو باقی نماند.۲۶
27 Iphani ankhondo ake onse. Onse aphedwe ndithu. Tsoka lawagwera pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
همه گاوانش را به سلاخ خانه فرود آورده، بکشید. وای بر ایشان! زیرا که یوم ایشان و زمان عقوبت ایشان رسیده است.۲۷
28 Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni akulengeza mu Yerusalemu za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu. Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
آوازفراریان و نجات‌یافتگان از زمین بابل مسموع می‌شود که از انتقام یهوه خدای ما و انتقام هیکل او در صهیون اخبار می‌نمایند.۲۸
29 “Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni. Muyitanenso onse amene amakoka mauta. Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira; musalole munthu aliyense kuthawa. Muchiteni monga momwe iye anachitira anthu ena. Iyeyu ananyoza Yehova, Woyera wa Israeli.
تیراندازان را به ضد بابل جمع کنید. ای همگانی که کمان را زه می‌کنید، در برابر او از هر طرف اردو زنید تااحدی رهایی نیابد و بر وفق اعمالش او را جزا دهید و مطابق هر‌آنچه کرده است به او عمل نمایید. زیرا که به ضد خداوند و به ضد قدوس اسرائیل تکبر نموده است.۲۹
30 Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake; ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova.
لهذا خداوندمی گوید که جوانانش در کوچه هایش خواهندافتاد و جمیع مردان جنگیش در آن روز هلاک خواهند شد.۳۰
31 “Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, “chifukwa tsiku lako lafika, nthawi yoti ndikulange yakwana.
«اینک خداوند یهوه صبایوت می‌گوید: ای متکبر من بر‌ضد تو هستم. زیرا که یوم تو و زمانی که به تو عقوبت برسانم رسیده است.۳۱
32 Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa ndipo palibe amene adzakudzutse; ndidzayatsa moto mʼmizinda yake umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
و آن متکبر لغزش خورده، خواهد افتاد و کسی او رانخواهد برخیزانید و آتش در شهرهایش خواهم افروخت که تمامی حوالی آنها را خواهدسوزانید.۳۲
33 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a ku Israeli akuzunzidwa, pamodzi ndi anthu a ku Yuda, ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa, akukana kuwamasula.
یهوه صبایوت چنین می‌گوید: بنی‌اسرائیل و بنی یهودا با هم مظلوم شدند و همه آنانی که ایشان را اسیر کردند ایشان را محکم نگاه می‌دارند و از رها کردن ایشان ابا می‌نمایند.۳۳
34 Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo, koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
اماولی ایشان که اسم او یهوه صبایوت می‌باشدزورآور است و دعوی ایشان را البته انجام خواهدداد و زمین را آرامی خواهد بخشید و ساکنان بابل را بی‌آرام خواهد ساخت.۳۴
35 Yehova akuti, “Imfa yalunjika pa Ababuloni, pa akuluakulu ake ndi pa anthu ake a nzeru!
خداوند می‌گوید: شمشیری بر کلدانیان است و بر ساکنان بابل وسرورانش و حکیمانش.۳۵
36 Imfa yalunjika pa aneneri abodza kuti asanduke zitsiru. Imfa yalunjika pa ankhondo ake kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
شمشیری بر کاذبان است و احمق خواهند گردید. شمشیری برجباران است و مشوش خواهند شد.۳۶
37 Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake. Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo kuti asanduke ngati akazi. Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake kuti chidzafunkhidwe.
شمشیری بر اسبانش و بر ارابه هایش می‌باشدو بر تمامی مخلوق مختلف که در میانش هستند ومثل زنان خواهند شد. شمشیری بر خزانه هایش است و غارت خواهد شد.۳۷
38 Chilala chilunjike pa madzi ake kuti aphwe. Babuloni ndi dziko la mafano, ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
خشکسالی برآبهایش می‌باشد و خشک خواهد شد زیرا که آن زمین بتها است و بر اصنام دیوانه شده‌اند.۳۸
39 “Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko ndipo kudzakhalanso akadzidzi. Kumeneko sikudzapezekako anthu, ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
بنابراین وحوش صحرا با گرگان ساکن خواهندشد و شترمرغ در آن سکونت خواهد داشت و بعداز آن تا به ابد مسکون نخواهد شد و نسلا بعدنسل معمور نخواهد گردید.»۳۹
40 Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,” akutero Yehova, “momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko; anthu sadzayendanso mʼmenemo.
خداوندمی گوید: «چنانکه خدا سدوم و عموره وشهرهای مجاور آنها را واژگون ساخت، همچنان کسی آنجا ساکن نخواهد شد و احدی از بنی آدم در آن ماوا نخواهد گزید.۴۰
41 “Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri, wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
اینک قومی از طرف شمال می‌آیند و امتی عظیم و پادشاهان بسیار ازکرانه های جهان برانگیخته خواهند شد.۴۱
42 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo. Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo, ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo iwe Babuloni.
ایشان کمان و نیزه خواهند گرفت. ایشان ستم پیشه هستند و ترحم نخواهند نمود. آواز ایشان مثل شورش دریا است و بر اسبان سوار شده، در برابرتو‌ای دختر بابل مثل مردان جنگی صف آرایی خواهند نمود.۴۲
43 Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo, ndipo yalobodokeratu. Ikuda nkhawa, ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
پادشاه بابل آوازه ایشان راشنید و دستهایش سست گردید. و الم و درد او رامثل زنی که می‌زاید در‌گرفته است.۴۳
44 Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani kupita ku msipu wobiriwira, momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi. Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine. Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane? Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
اینک اومثل شیر از طغیان اردن به آن مسکن منیع برخواهد آمد زیرا که من ایشان را در لحظه‌ای ازآنجا خواهم راند. و کیست آن برگزیده‌ای که او رابر آن بگمارم؟ زیرا کیست که مثل من باشد وکیست که مرا به محاکمه بیاورد و کیست آن شبانی که به حضور من تواند ایستاد؟»۴۴
45 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
بنابراین مشورت خداوند را که درباره بابل نموده است وتقدیرهای او را که درباره زمین کلدانیان فرموده است بشنوید. البته ایشان صغیران گله را خواهندربود و هر آینه مسکن ایشان را برای ایشان خراب خواهد ساخت.۴۵
46 Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera, ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.
از صدای تسخیر بابل زمین متزلزل شد و آواز آن در میان امت‌ها مسموع گردید.۴۶

< Yeremiya 50 >