< Yeremiya 50 >
1 Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:
The word which Yahweh spake Against Babylon Against the land of the Chaldeans, through Jeremiah the prophet:
2 “Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina, kweza mbendera ndipo ulengeze; usabise kanthu, koma uwawuze kuti, ‘Babuloni wagwa; mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi, nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha. Milungu yake yagwidwa ndi mantha ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
Tell ye among the nations And let it be heard And lift ye up a standard, Let it be heard do not conceal: Say ye—Captured is Babylon, Confounded is Bel, Broken in pieces is Merodach, Confounded are her images, Broken down her manufactured gods;
3 Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni ndi kusandutsa bwinja dziko lake. Kumeneko sikudzakhalanso munthu kapena nyama.
For there hath come up against her—a nation out of the North The same, shall make her land an astonishment, And there shall be none to dwell therein, —Both man and beast, have removed—have gone.
4 “Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
In those days, and at that time, Declareth Yahweh, Shall the sons of Israel come in, They and the sons of Judah together: Weeping as they travel, so shall they journey on, And Yahweh their God, shall they seek;
5 Adzafunsa njira ya ku Ziyoni ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko. Iwo adzadzipereka kwa Yehova pochita naye pangano lamuyaya limene silidzayiwalika.
To Zion, shall they ask the way, Hitherward, their faces, Come and let us join ourselves unto Yahweh, In a covenant age-abiding, which shall not be forgotten.
6 “Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika; abusa awo anawasocheretsa mʼmapiri. Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda mpaka kuyiwala kwawo.
Wandering sheep, have my people, been, Their own shepherds led them astray, On the mountains, they seduced them, From mountain to hill, have they gone, They have forgotten their couching-place.
7 Aliyense amene anawapeza anawawononga; adani awo anati, ‘Ife si olakwa, chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’
All who found them, devoured them, And, their adversaries, said—We shall not be, guilty, —Because they have sinned, Against, Yahweh the pasturage of righteousness, Yea the hope of their fathers—Yahweh.
8 “Thawaniko ku Babuloni; chokani mʼdziko la Ababuloni. Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
Remove ye out of the midst of Babylon, And out of the land of the Chaldeans, come ye forth, —And become ye like he-goats before the flock;
9 Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto kudzamenyana ndi Babuloni. Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni. Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso, yosapita padera.
For lo! I am rousing and bringing up against Babylon a gathered host of great nations, out of the land of the North, And they shall array themselves against her, From thence, shall she be captured, —His arrows, are as of a hero making childless, None shall return empty.
10 Motero Ababuloni adzafunkhidwa; ndipo onse omufunkha adzakhuta,” akutero Yehova.
So shall the Chaldeans become a spoil, —All her spoilers, shall be satisfied, Declareth Yahweh;
11 “Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika. Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala. Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
Because they used to be glad Because they used to be uproarious When plundering mine inheritance, —Because they used to caper about as a heifer at grass, And bellow like bulls.
12 Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri. Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa. Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse. Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
Your mother, hath turned very pale, She that bare you, hath turned red, —Lo! the last of nations, is—A desert, A parched land, and A waste plain,
13 Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu ndipo adzakhala chipululu chokhachokha. Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.
Because of the vexation of Yahweh, she shall not be inhabited, But Shall become a complete desolation, —Every one passing by Babylon, shall be astonished and hiss, over all her plagues.
14 “Inu okoka uta, konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse. Muponyereni mivi yanu yonse chifukwa anachimwira Yehova.
Set yourselves in array against Babylon round about All ye who tread the bow, Shoot at her, do not spare so much as an arrow, —For against Yahweh, hath she sinned.
15 Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja. Nsanja zake zagwa. Malinga ake agwetsedwa. Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova. Mulipsireni, mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
Raise a shout against her round about She hath stretched forth her hand, Fallen are her buttresses, Torn down are her walls, —Because, the avenging of Yahweh it is, Take ye vengeance upon her, As she hath done, do ye, unto her.
16 Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense, ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola. Poona lupanga la ozunza anzawo, aliyense adzabwerera kwa anthu ake; adzathawira ku dziko la kwawo.
Cut ye off the sower from Babylon, And him that graspeth the sickle in the time of harvest, From the face of the sword of the oppressor, Each, to his own people will they turn, and Each, to his own land will they flee.
17 “Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika pothamangitsidwa ndi mikango. Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo. Wotsiriza anali Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”
A sheep all alone, is Israel Lions, have driven him away, —At the first, the king of Assyria devoured him, And here, at the last, Nebuchadrezzar king of Babylon hath broken his bones!
18 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
Therefore, Thus, saith Yahweh of hosts, God of Israel, Behold me! bringing punishment against the king of Babylon, and against his land, —Just as I brought punishment against the king of Assyria.
19 Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani; adzadya nakhuta ku mapiri a ku Efereimu ndi Giliyadi.
So will I bring back Israel unto his own pasture, And he shall feed upon Carmel and Bashan; And in the hill country of Ephraim and Gilead, shall, his soul, be satisfied.
20 Masiku amenewo, nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe, ndipo adzafufuza machimo a Yuda, koma sadzapeza ndi limodzi lomwe, chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.
In those days and in that time, Declareth Yahweh, The iniquity of Israel, shall be sought, and there shall be none, And the sins of Judah, and they shall not be found; For I will grant pardon to them whom I suffer to remain.
21 “Lithireni nkhondo dziko la Merataimu ndi anthu okhala ku Pekodi. Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,” akutero Yehova. “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
Against the land of Merathaim, go thou up against her, And against the inhabitants of Pekod, —Lay waste and devote to destruction after them Declareth Yahweh, And do according to all which I have commanded thee.
22 Mʼdziko muli phokoso la nkhondo, phokoso la chiwonongeko chachikulu!
The sound of battle is in the earth, —And a great destruction.
23 Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi. Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ina!
How is cut and broken the hammer of all the earth! How hath Babylon become an astonishment among the nations!
24 Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.
I laid a snare for thee yea and thou wast captured O Babylon, when, thou wast not aware, —Thou wast found out yea and taken, For with Yahweh, hadst thou contended.
25 Yehova watsekula nyumba ya zida zake ndipo watulutsa zida za ukali wake, pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire mʼdziko la Ababuloni.
Yahweh opened his armoury, and brought out his weapons of indignation, —For, a work, it is pertaining to My Lord, Yahweh of hosts, in the land of the Chaldeans,
26 Mumenyane naye Babuloni mbali zonse. Anthu ake muwawunjike ngati milu ya tirigu. Muwawononge kotheratu ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
Come ye against her from farthest parts, Throw open her granaries, Cast her up as heaps, and devote her to destruction, —Do not let her have a remnant.
27 Iphani ankhondo ake onse. Onse aphedwe ndithu. Tsoka lawagwera pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
Cut up all her bullocks, Let them go down to the slaughter, —Alas for them! For their day, hath come, Their time for punishment.
28 Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni akulengeza mu Yerusalemu za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu. Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.
The voice Of them who are in flight and Of such as are escaping, out of the land of Babylon, —To tell in Zion The avenging of Yahweh our God, The avenging of his temple.
29 “Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni. Muyitanenso onse amene amakoka mauta. Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira; musalole munthu aliyense kuthawa. Muchiteni monga momwe iye anachitira anthu ena. Iyeyu ananyoza Yehova, Woyera wa Israeli.
Publish against Babylon ye chiefs of all who tread the bow—Encamp against her round about Let there be none to escape, Recompense to her according to her work, According to all which she did, do ye to her, —For Against Yahweh, hath she acted presumptuously, Against the Holy One of Israel.
30 Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake; ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova.
Therefore, shall her young men fall in her broadways, —And, all her men of war, be silenced in that day, Declareth Yahweh.
31 “Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, “chifukwa tsiku lako lafika, nthawi yoti ndikulange yakwana.
Behold me! against thee most insolent one, Declareth My Lord Yahweh of hosts; For thy day, hath come, Thy time for punishment;
32 Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa ndipo palibe amene adzakudzutse; ndidzayatsa moto mʼmizinda yake umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”
So shall the most insolent one stumble and fall, And he shall have none to lift him up, —And I will kindle a fire in his cities which shall devour all who are round about him.
33 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a ku Israeli akuzunzidwa, pamodzi ndi anthu a ku Yuda, ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa, akukana kuwamasula.
Thus, saith Yahweh of hosts—Oppressed were the sons of Israel and the sons of Judah, together, —And, all who took them captive, Held them fast Refused to let them go: —
34 Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo, koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”
Their Redeemer, can hold fast, Yahweh of hosts, is his name, He will, thoroughly plead, their plea, —That he may quiet the earth, And disquiet the inhabitants of Babylon.
35 Yehova akuti, “Imfa yalunjika pa Ababuloni, pa akuluakulu ake ndi pa anthu ake a nzeru!
A sword, is over the Chaldeans, Declareth Yahweh, —And against the inhabitants of Babylon, And against her princes, And against her wise men:
36 Imfa yalunjika pa aneneri abodza kuti asanduke zitsiru. Imfa yalunjika pa ankhondo ake kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
A sword, is against the praters, And they shall be shewn to be foolish, A sword, is against her heroes And they shall be dismayed:
37 Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake. Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo kuti asanduke ngati akazi. Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake kuti chidzafunkhidwe.
A sword, is against his horses and against his chariots and, against all the rabble that are in her midst And they shall become women, —A sword, is against her treasures And they shall be made a prey:
38 Chilala chilunjike pa madzi ake kuti aphwe. Babuloni ndi dziko la mafano, ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.
A drought, is against her waters, And they shall be dried up, —For a land of images, it is, And with their shocking things, they act as men who are mad:
39 “Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko ndipo kudzakhalanso akadzidzi. Kumeneko sikudzapezekako anthu, ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
Therefore shall the criers dwell with, the howlers, Yea ostriches, shall dwell therein, —So shall it be dwelt in no more for ever, Neither shall it be inhabited unto generation after generation.
40 Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,” akutero Yehova, “momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko; anthu sadzayendanso mʼmenemo.
Like the divine overthrow of Sodom and Gomorrah and her neighbours, Declareth Yahweh, —There shall not dwell there—a man, Nor sojourn therein—a son of the earth-born.
41 “Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri, wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Lo! a people coming in from the North, —Yea, a great nation and many kings, shall be roused up out of the remote parts of the earth:
42 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo. Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo, ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo iwe Babuloni.
Bow and javelin, shall they grasp, Cruel, are they and will not have compassion, Their voice, like the sea, will roar, And, on horses, will they ride, —Set in array, as one man for battle, Against thee, O daughter of Babylon!
43 Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo, ndipo yalobodokeratu. Ikuda nkhawa, ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
The king of Babylon hath heard the report of them, And unnerved are his hands, —Anguish, hath seized him, Writhing pain, as a woman in child-birth.
44 Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani kupita ku msipu wobiriwira, momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi. Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine. Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane? Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
Lo! as a lion, shall he come up from the majesty of the Jordan, Unto the pasture perennial, But I will wink—I will make them run away therefrom, Who then shall be the Chosen One whom against it, I may set in charge? For who shall be like unto, me? And who shall appoint me, a time? And who is the Shepherd that shall stand before me?
45 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Therefore hear ye, The counsel of Yahweh, which he hath counselled against Babylon, And his devices which he hath devised against the land of the Chaldeans, —Surely the little ones of the flock, shall drag them away, Surely he will cause the pasture to be astounded over them.
46 Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera, ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.
At the noise of the taking of Babylon, the earth trembled, —And, the outcry, among the nations, was heard.