< Yeremiya 5 >

1 “Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu, mudzionere nokha, funafunani mʼmabwalo ake. Ngati mungapeze munthu mmodzi amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi, ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.
Obchodźcie ulice Jeruzalemskie, a upatrujcie teraz, i obaczcie, a szukajcie po ulicach jego, jeźli znajdziecie męża, jeźli kto jest coby czynił sąd i szukał prawdy, a przepuszczę mu.
2 Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ komabe akungolumbira mwachinyengo.”
Ale choć mówią: Jako żyje Pan, tedy przecię krzywo przysięgają.
3 Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona? Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka; munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro. Anawumitsa mitima yawo ngati mwala ndipo anakaniratu kulapa.
O Panie! izali oczy twoje nie patrzą na prawdę? Bijesz ich, ale ich nie boli; wniwecz ich obracasz, ale nie chcą przyjąć karania; zatwardzili oblicza swe nad opokę, nie chcą się nawrócić.
4 Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe; anthu ochita zopusa. Sadziwa njira ya Yehova, sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.
Tedym Ja rzekł: Podobno ci nędzni są, głupio sobie poczynają; bo nie są powiadomi drogi Pańskiej, i sądu Boga swego.
5 Tsono ndidzapita kwa atsogoleri ndi kukayankhula nawo; ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova, amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.” Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova ndipo anadula msinga zawo.
Pójdę do celniejszych, i będę mówił do nich; bo oni są powiadomi drogi Pańskiej, i sądu Boga swego; ale i ci wespół połamali jarzmo, potargali związki.
6 Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha, mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga, kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.
Przetoż ich pobije lew z lasu, wilk wieczorny wygubi ich, lampart czyhać będzie u miast ich. Ktokolwiek wyjdzie z nich, rozszarpany będzie; bo się rozmnożyły przestępstwa ich, i zmogły się odwrócenia ich.
7 Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita? Ana anu andisiya Ine ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse. Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa, komabe iwo anachita chigololo namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.
Jestże co, dlaczegobym ci miał przepuścić? Synowie twoi opuścili mię, a przysięgają przez onych, którzy nie są bogami. Jakom ich jedno nakarmił, zaraz cudzołożą, a do domu wszetecznicy hurmem się walą.
8 Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa, aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.
Rano wstawając są jako konie wytuczone, każdy z nich rży do żony bliźniego swego.
9 Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi nʼkuleka kuwulipsira mtundu woterewu?
Izali dlatego nawiedzić ich nie mam? mówi Pan; izali się nad takim narodem nie ma mścić dusza moja?
10 “Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga, koma musakayiwononge kotheratu. Sadzani nthambi zake pakuti anthu amenewa si a Yehova.
Wstąpcie na mury jego, a rozwalcie je, wszakże ich do gruntu nie znoście; znieście filarzyki murów jego, gdyż nie są Pańskie.
11 Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”
Wielce zaiste wystąpił przeciwko mnie dom Izraelski i dom Judzki, mówi Pan.
12 Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti, “Yehova sangachite zimenezi! Choyipa sichidzatigwera; sitidzaona nkhondo kapena njala.
Zadali kłamstwo Panu, i rzekli: Nie tak, nie przyjdzieć na nas nic złego, a miecza i głodu nie doznamy.
13 Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo; ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova. Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”
A ci prorocy pominą z wiatrem, a żadnego słowa Bożego niemasz u nich; i owszem tak się im samym stanie.
14 Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti, “Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa, tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.
Przetoż tak mówi Pan, Bóg zastępów: Ponieważeście to mówili, oto Ja kładę słowa moje w usta twoje za ogień, a lud ten za drwa, i pożre ich.
15 Inu Aisraeli,” Yehova akuti, “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali, ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo, mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa, zimene akunena inu simungazimvetse.
Oto Ja przywiodę na was naród z daleka, o domie Izraelski! mówi Pan, naród mocny, naród starodawny, naród, którego języka umieć nie będziesz, ani zrozumiesz, co mówi.
16 Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri; onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.
Którego sajdak jako grób otwarty, wszyscy są mężni.
17 Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu, adzapha ana anu aamuna ndi aakazi; adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu, adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu. Ndi malupanga awo adzagwetsa mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.
I zjedzą urodzaj twój, i chleb twój: pożrą synów twoich i córki twoje; poje trzody twoje i woły twoje; poje winną macicę twoję, i figi twoje, a miasta twoje obronne, w których ty ufasz, mieczem znędzi.
18 “Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova.
A wszakże i w one dni, mówi Pan, końca z wami nie uczynię.
19 Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”
Albowiem gdy rzeczecie: Przeczże nam Pan, Bóg nasz, to wszystko czyni? Tedy im odpowiesz: Jakoście mię opuścili, a służyli bogom cudzym w ziemi waszej, tak służyć będziecie cudzoziemcom w ziemi nie waszej.
20 “Lengeza izi kwa ana a Yakobo ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,
Oznajmijcie to domowi Jakóbowemu, a rozgłoście w Judzie, mówiąc:
21 Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru, inu amene maso muli nawo koma simupenya, amene makutu muli nawo koma simumva.
Słuchajcież teraz tego, ludu głupi! który niemasz serca, który oczy mając, a nie widzisz, który uszy mając, a nie słyszysz.
22 Kodi simuyenera kuchita nane mantha?” Akutero Yehova. “Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga? Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja, malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo. Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo; mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.
I nie będziecież się mnie bali? mówi Pan; a przed obliczem mojem nie będziecież się lękali? którym położył morzu piasek za granicę ustawą wieczną, a nie przestąpi jej. Choć się wzruszą, wszakże nie przemogą; choć się wzburzą wały jego, wszakże nie przeskoczą go.
23 Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.
Ale ten lud ma serce ociążałe i odporne; odstąpili odemnie i odeszli;
24 Sananenepo mʼmitima mwawo kuti, ‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu. Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika. Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’
Ani rzekli w sercu swem: Bójmy się już Pana, Boga naszego, który daje deszcz i w jesieni i na wiosnę czasu swego, który tygodni pewnych i żniwa naszego przestrzega.
25 Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi; ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.
Ale nieprawości wasze odwróciły to, a grzechy wasze zahamowały to dobro od was.
26 “Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.
Bo się znajdują w ludu moim niezbożnicy, którzy czyhają jako łowcy, rozciągają sieci, zastawiają sidła, a łapią ludzi.
27 Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo ngati zikwere zodzaza ndi mbalame. Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.
Jako klatka pełna ptaków, tak domy ich pełne są zdrady; przetoż się wzmogli i zbogacili.
28 Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala. Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire; saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino, sateteza ufulu wa anthu osauka.
Roztyli, lśnią się, i innych w złościach przewyższają; sprawy nie sądzą, ani sprawy sierotki; wszakże się im szczęści, chociaż sprawy ubogiego nie rozsądzili.
29 Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi? Kodi ndisawulipsire mtundu woterewu? Akutero Yehova.
Izali dlatego nie nawiedzę ich? mówi Pan; izali się nad narodem takowym nie będzie mścić dusza moja?
30 “Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri chachitika mʼdzikomo:
Rzecz dziwna i sroga dzieje się w tej ziemi:
31 Aneneri akunenera zabodza, ndipo ansembe akuvomerezana nawo, ndipo anthu anga akukonda zimenezi. Koma mudzatani potsiriza?
Prorocy kłamliwie prorokują, a kapłani panują przez ręce ich, a lud mój kocha się w tem; czegożbyście na ostatek nie uczynili?

< Yeremiya 5 >