< Yeremiya 5 >

1 “Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu, mudzionere nokha, funafunani mʼmabwalo ake. Ngati mungapeze munthu mmodzi amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi, ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.
Parcourez les rues de Jérusalem et regardez, informez-vous; cherchez sur ses places publiques si vous y trouvez un homme, s’il en est un qui pratique la justice, et qui recherche la fidélité, et je ferai grâce à la ville.
2 Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ komabe akungolumbira mwachinyengo.”
Même quand ils disent: « Yahweh est vivant! » c’est pour le mensonge qu’ils jurent.
3 Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona? Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka; munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro. Anawumitsa mitima yawo ngati mwala ndipo anakaniratu kulapa.
Yahweh, vos yeux ne cherchent-ils pas la fidélité? Vous les avez frappés, et ils n’ont pas eu de douleur; vous les avez exterminés, et ils n’ont pas voulu recevoir l’instruction; ils ont endurci leur face plus que le roc; ils ont refusé de revenir.
4 Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe; anthu ochita zopusa. Sadziwa njira ya Yehova, sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.
Et moi, je disais: Ce ne sont que les petits. Ils agissent en insensés, car ils ne savent pas la voie de Yahweh, la loi de leur Dieu.
5 Tsono ndidzapita kwa atsogoleri ndi kukayankhula nawo; ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova, amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.” Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova ndipo anadula msinga zawo.
J’irai donc vers les grands et je leur parlerai; car eux, ils savent la voie de Yahweh, La loi de leur Dieu... Mais eux aussi, ils ont tous ensemble brisé le joug, Rompu les liens!
6 Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha, mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga, kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.
C’est pourquoi le lion de la forêt les a frappés, le loup du désert les ravage; la panthère est aux aguets devant leurs villes, tout homme qui en sort est déchiré; car leurs transgressions sont nombreuses, et leurs révoltes se sont accrues.
7 Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita? Ana anu andisiya Ine ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse. Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa, komabe iwo anachita chigololo namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.
Pour quelle raison te ferais-je grâce! Tes fils m’ont abandonné, et ils jurent par ce qui n’est pas Dieu. Je les ai rassasiés, et ils ont été adultères; ils vont par troupes dans la maison de la prostituée.
8 Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa, aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.
Etalons bien repus, vagabonds, chacun d’eux hennit à la femme de son prochain.
9 Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi nʼkuleka kuwulipsira mtundu woterewu?
Et je ne les punirais pas pour ces crimes! — oracle de Yahweh; et d’une nation telle que celle-là je ne me vengerais pas!
10 “Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga, koma musakayiwononge kotheratu. Sadzani nthambi zake pakuti anthu amenewa si a Yehova.
Escaladez ses murs et détruisez, mais non pas entièrement; enlevez ses sarments, car ils ne sont pas à Yahweh!
11 Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”
Car elles m’ont été tout à fait infidèles, la maison d’Israël et la maison de Juda, — oracle de Yahweh.
12 Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti, “Yehova sangachite zimenezi! Choyipa sichidzatigwera; sitidzaona nkhondo kapena njala.
Ils ont renié Yahweh et dit: « Il n’est pas, et le malheur ne viendra pas sur nous; nous ne verrons ni l’épée, ni la famine.
13 Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo; ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova. Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”
Les prophètes ne sont que du vent, et personne ne parle en eux: qu’il leur soit fait ainsi à eux-mêmes! »
14 Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti, “Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa, tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.
C’est pourquoi ainsi parle Yahweh, le Dieu des armées: Parce que vous dites cette parole-là, voici que je mets ma parole dans ta bouche comme un feu, et ce peuple sera comme du bois et ce feu les dévorera.
15 Inu Aisraeli,” Yehova akuti, “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali, ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo, mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa, zimene akunena inu simungazimvetse.
Me voici qui amène sur vous une nation qui vient de loin, maison d’Israël, — oracle de Yahweh; c’est une nation forte, c’est une nation antique, une nation dont tu ne connais pas la langue, et tu n’entends pas ce qu’elle dit.
16 Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri; onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.
Son carquois est un sépulcre ouvert; ils sont tous des héros.
17 Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu, adzapha ana anu aamuna ndi aakazi; adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu, adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu. Ndi malupanga awo adzagwetsa mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.
Elle dévorera ta moisson et ton pain; elle dévorera tes fils et tes filles; elle dévorera tes brebis et tes bœufs; elle dévorera ta vigne et ton figuier; elle détruira par l’épée tes villes fortes dans lesquelles tu te confies.
18 “Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova.
Mais même en ces jours-là, — oracle du Yahweh, je ne vous détruirai pas entièrement.
19 Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”
Et quand vous direz: « Pour quelle raison Yahweh, notre Dieu, nous a-t-il fait toutes ces choses? » Tu leur diras: « Comme vous m’avez abandonné pour servir dans votre pays un dieu étranger, ainsi vous servirez des étrangers dans un pays qui n’est pas à vous.”
20 “Lengeza izi kwa ana a Yakobo ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,
Annoncez ceci dans la maison de Jacob; et publiez-le dans Juda, en ces termes:
21 Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru, inu amene maso muli nawo koma simupenya, amene makutu muli nawo koma simumva.
Ecoutez donc ceci, peuple insensé et sans cœur! Ils ont des yeux et ne voient point, des oreilles et ils n’entendent point!
22 Kodi simuyenera kuchita nane mantha?” Akutero Yehova. “Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga? Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja, malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo. Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo; mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.
Ne me craindrez-vous pas, — oracle de Yahweh; ne tremblerez-vous pas devant moi, moi qui ai mis le sable pour limite à la mer, borne éternelle, qu’elle ne franchira pas? Ses flots s’agitent, et ils sont impuissants; ils mugissent, et ils ne la dépassent pas.
23 Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.
Mais ce peuple a un cœur indocile et rebelle; ils se retirent et s’en vont.
24 Sananenepo mʼmitima mwawo kuti, ‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu. Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika. Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’
Ils ne disent pas dans leur cœur: « Craignons Yahweh notre Dieu lui qui donne la pluie, celle de la première saison, et celle de l’arrière-saison en son temps, et qui nous garde les semaines destinées à la moisson. »
25 Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi; ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.
Vos iniquités ont dérangé cet ordre; vos péchés vous privent de ces biens.
26 “Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.
Car il se trouve des pervers dans mon peuple; ils épient comme l’oiseleur qui se baisse, ils dressent des pièges et prennent des hommes.
27 Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo ngati zikwere zodzaza ndi mbalame. Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.
Comme une cage est pleine d’oiseaux, ainsi leurs maisons sont pleines de fraude; aussi deviennent-ils puissants et riches;
28 Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala. Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire; saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino, sateteza ufulu wa anthu osauka.
Ils s’engraissent, ils reluisent. Ils dépassent même la mesure du mal; ils ne font pas justice, justice à l’orphelin... et ils prospèrent!... Ils ne font pas droit aux malheureux.
29 Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi? Kodi ndisawulipsire mtundu woterewu? Akutero Yehova.
Et je ne punirais pas ces crimes! — oracle de Yahweh; et d’une nation telle que celle-là je ne me vengerais pas!...
30 “Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri chachitika mʼdzikomo:
Des choses abominables, horribles, se font dans le pays.
31 Aneneri akunenera zabodza, ndipo ansembe akuvomerezana nawo, ndipo anthu anga akukonda zimenezi. Koma mudzatani potsiriza?
Les prophètes prophétisent en mentant, les prêtres gouvernent d’accord avec eux! Et mon peuple l’aime ainsi! Et que ferez-vous au terme de tout cela?

< Yeremiya 5 >