< Yeremiya 5 >
1 “Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu, mudzionere nokha, funafunani mʼmabwalo ake. Ngati mungapeze munthu mmodzi amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi, ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.
Run ye about in the streets of Jerusalem, and see, and know, and seek in her broad places, if ye can find [one], if there is any one that does judgment, and seeks faithfulness; and I will pardon them, saith the Lord.
2 Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ komabe akungolumbira mwachinyengo.”
The Lord lives, they say; do they not therefore swear falsely?
3 Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona? Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka; munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro. Anawumitsa mitima yawo ngati mwala ndipo anakaniratu kulapa.
O Lord, thine eyes are upon faithfulness: thou hast scourged them, but they have not grieved; thou hast consumed them; but they would not receive correction: they have made their faces harder than a rock; and they would not return.
4 Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe; anthu ochita zopusa. Sadziwa njira ya Yehova, sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.
Then I said, It may be they are poor; for they are weak, for they know not the way of the Lord, or the judgment of God.
5 Tsono ndidzapita kwa atsogoleri ndi kukayankhula nawo; ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova, amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.” Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova ndipo anadula msinga zawo.
I will go to the rich men, and will speak to them; for they have known the way of the Lord, and the judgment of God: but, behold, with one consent they have broken the yoke, they have burst the bonds.
6 Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha, mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga, kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.
Therefore has a lion out of the forest smitten them, and a wolf has destroyed them even to [their] houses, and a leopard has watched against their cities: all that go forth from them shall be hunted: for they have multiplied their ungodliness, they have strengthened themselves in their revoltings.
7 Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita? Ana anu andisiya Ine ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse. Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa, komabe iwo anachita chigololo namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.
In what [way] shall I forgive thee for these things? Thy sons have forsaken me, and sworn by them that are no gods: and I fed them to the full, and they committed adultery, and lodged in harlots' houses.
8 Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa, aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.
They became as wanton horses: they neighed each one after his neighbour's wife.
9 Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi nʼkuleka kuwulipsira mtundu woterewu?
Shall I not visit for these things? saith the Lord: and shall not my soul be avenged on such a nation as this.
10 “Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga, koma musakayiwononge kotheratu. Sadzani nthambi zake pakuti anthu amenewa si a Yehova.
Go up upon her battlements, and break [them] down; but make not a full end: leave her buttresses: for they are the Lord's.
11 Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”
For the house of Israel have indeed dealt treacherously against me, saith the Lord: the house of Juda also
12 Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti, “Yehova sangachite zimenezi! Choyipa sichidzatigwera; sitidzaona nkhondo kapena njala.
have lied to their Lord, and they have said, These things are not so; no evils shall come upon us; and we shall not see sword or famine.
13 Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo; ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova. Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”
Our prophets became wind, and the word of the Lord was not in them.
14 Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti, “Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa, tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.
Therefore thus saith the Lord Almighty, Because ye have spoken this word, behold, I have made my words in thy mouth fire, and this people wood, and it shall devour them.
15 Inu Aisraeli,” Yehova akuti, “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali, ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo, mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa, zimene akunena inu simungazimvetse.
Behold, I [will] bring upon you a nation from far, O house of Israel, saith the Lord; a nation the sound of whose language one shall not understand.
16 Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri; onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.
[They are] all mighty men:
17 Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu, adzapha ana anu aamuna ndi aakazi; adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu, adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu. Ndi malupanga awo adzagwetsa mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.
and they shall devour your harvest, and your bread; and shall devour your sons, and your daughters; and they shall devour your sheep, and your calves, and devour your vineyards, and your fig-plantations, and your olive yards: and they shall utterly destroy your strong cities, wherein ye trusted, with the sword.
18 “Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova.
And it shall come to pass in those days, saith the Lord thy God, that I will not utterly destroy you.
19 Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”
And it shall come to pass, when ye shall say, Wherefore has the Lord our God done all these things to us? that thou shalt say to them, Because ye served strange gods in your land, so shall ye serve strangers in a land that is not yours.
20 “Lengeza izi kwa ana a Yakobo ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,
Proclaim these things to the house of Jacob, and let them be heard in the house of Juda.
21 Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru, inu amene maso muli nawo koma simupenya, amene makutu muli nawo koma simumva.
Hear ye now these things, O foolish and senseless people; who have eyes, and see not; and have ears, and hear not:
22 Kodi simuyenera kuchita nane mantha?” Akutero Yehova. “Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga? Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja, malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo. Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo; mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.
will ye not be afraid of me? saith the Lord; and will ye not fear before me, who have set the sand for a bound to the sea, [as] a perpetual ordinance, and it shall not pass it: yea, it shall rage, but not prevail; and its waves shall roar, but not pass over it.
23 Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.
But this people has a disobedient and rebellious heart; and they have turned aside and gone back:
24 Sananenepo mʼmitima mwawo kuti, ‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu. Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika. Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’
and they have not said in their heart, Let us fear now the Lord our God, who gives us the early and latter rain, according to the season of the fulfillment of the ordinance of harvest, and has preserved [it] for us.
25 Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi; ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.
Your transgressions have turned away these things, and your sins have removed good things from you.
26 “Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.
For among my people were found ungodly men; and they have set snares to destroy men, and have caught [them].
27 Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo ngati zikwere zodzaza ndi mbalame. Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.
As a snare which has been set is full of birds, so are their houses full of deceit: therefore have they grown great, and become rich:
28 Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala. Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire; saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino, sateteza ufulu wa anthu osauka.
and they have transgressed [the rule of] judgment; they have not judged the cause of the orphan, nor have they judged the cause of the widow.
29 Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi? Kodi ndisawulipsire mtundu woterewu? Akutero Yehova.
Shall I not visit for these things? saith the Lord: and shall not my soul be avenged on such a nation as this?
30 “Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri chachitika mʼdzikomo:
Shocking and horrible deeds have been done on the land;
31 Aneneri akunenera zabodza, ndipo ansembe akuvomerezana nawo, ndipo anthu anga akukonda zimenezi. Koma mudzatani potsiriza?
the prophets utter unrighteous prophecies, and the priests have clapped their hands: and my people has loved [to have it] thus: and what will ye do for the future.