< Yeremiya 49 >
1 Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Emot Ammons barn säger Herren alltså: Hafver nu Israel inga barn, eller hafver han inga arfvingar? Hvi besitter då Malcham Gads land, och hans folk bor i hans städer?
2 Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
Derföre, si; den tiden kommer, säger Herren, att jag skall låta, höra ett krigsskri öfver Rabbath, Ammons barnas, att det skall öde ligga uti en hop, och dess döttrar med eld uppbrända varda; men Israel skall besitta dem, af hvilkom de hafva besuttne varit, säger Herren.
3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Jämra dig, o Hesbon, ty Aj är förstörd; roper, I Rabba döttrar, och drager säcker uppå, gråter och löper omkring på murarna; ty Malcham varder fången bortförd, samt med sina Prester och Förstar.
4 Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Hvad trotsar du uppå dina dalar? Dine dalar äro fördränkte, du ohörsamma dotter, som förlåter dig uppå dina rikedomar, och säger i ditt hjerta: Ho tör komma till mig?
5 Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
Si detta säger Herren Herren Zebaoth: Jag skall låta komma en fruktan öfver dig, af allom dem som kring dig bo, så att hvar och en skall på sin väg bortdrifven varda, ifrå den andra, och ingen skall vara den som de flyktiga församlar.
6 “Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
Men derefter skall jag omvända Ammons barnas fängelse, säger Herren.
7 Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Emot Edom. Detta säger Herren Zebaoth: Är nu ingen vishet mer i Theman? Är nu intet råd mer när barnen? Är deras vishet ute?
8 Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Flyr, vänder eder om, och gömmer eder djupt neder, I borgare i Dedan; ty jag låter en ofärd komma öfver Esau, hans hemsöknings tid.
9 Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Vinhemtare skola komma öfver dig, de der intet skola lefva dig efter sig, och tjufvar om nattena skola komma öfver dig, de skola stjäla sig nog.
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
Ty jag hafver blottat Esau, och uppenbarat hans hemlig rum, så att han kan icke undstinga sig; hans säd, hans bröder, och hans grannar äro förstörde, att ingen af dem mer för handene är.
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
Dock hvad der qvart blifver af dina faderlösa, dem vill jag lifvet unna, och dina enkor skola hoppas uppå mig.
12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
Ty så säger Herren: Si, de som intet förskyllt hafva att dricka kalken, de måste drickan, och du skulle ostraffad blifva? Du skall intet ostraffad blifva; utan du måste ock drickan.
13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
Ty jag hafver svorit vid mig sjelf, säger Herren, att Bozra skall vara till ett vidunder, försmädelse, förödning och bannor, och alle hans städer till ett evigt öde.
14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
Jag hafver hört af Herranom, att ett bådskap är sändt till Hedningarna: Församler eder, och kommer hit emot honom, och strider.
15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
Ty si, jag hafver förnedrat dig ibland Hedningarna, och förakteligan gjort ibland menniskorna.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Din öfverdådighet och dins hjertans högmod hafver bedragit dig, efter du bor i bergklyftor, ock hafver hög berg inne; om du ditt näste så högt gjorde som en örn, så skall jag ändå likväl störta dig der neder, säger Herren.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
Alltså skall Edom öde varda, att allo de der framom gå, skola förundra sig, och hvissla öfver alla hans plågor;
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
Likasom Sodoma och Gomorra, samt med sina grannar, omstört är, säger Herren, så att ingen bor der, eller någor menniska derinne blifva kan.
19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
Ty si, han kommer upp lika som ett lejon ifrå den stolta Jordan, emot de fasta hyddor; ty jag vill låta honom snarliga löpa dit; och ho vet, hvilken den ynglingen är, den jag emot dem rusta skall? Ty ho är mig lik, ho vill lära mig? Och hvilken är den herden, som mig emotstå kan?
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Så hörer nu Herrans rådslag, som han öfver Edom hafver, och hans tankar, som han öfver Themans inbyggare hafver: Hvad gäller, att vallebarnen skola bortsläpa dem, och förstöra deras boning;
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
Så att jorden skall bäfva i deras fall, och deras rop skall man höra på röda hafvet.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Si, han flyger upp såsom en örn, och skall uträcka sina vingar öfver Bozra; på den tiden skall de hjeltars hjerta i Edom vara lika som ene qvinnos hjerta i barnsnöd.
23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
Emot Damascon. Hamath och Arpad stå jämmerliga, de äro förtviflade; ty de höra ond tidende: De som vid hafvet bo äro förskräckte, så att de kunna ingen ro hafva.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
Damascus är förtviflad, och gifver flyktena; han darrar, och är i ångest och värk, likasom en qvinna i barnsnöd.
25 Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
Huru? Är han nu icke öfvergifven, den beprisade och säkre staden?
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Derföre skola hans unge män ligga på hans gator, och alle hans krigsmän falla på den tiden, säger Herren Zebaoth.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
Och jag skall sticka eld på murarna i Damascon, att han Benhadads palats upptära skall.
28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
Emot Kedar och Hazors riken, hvilka NebucadNezar, Konungen i Babel, slog. Detta säger Herren: Upp, drager upp till Kedar, och förstörer de barn österut.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
Man skall taga dem deras hyddor och hjordar bort, deras tjäll och all deras tyg; och cameler skola de bortföra, och man skall förskräckeliga ropa öfver dem allt omkring.
30 “Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
Flyr, låter lida eder dädan, gömmer eder djupt neder, I inbyggare i Hazor, säger Herren; ty NebucadNezar, Konungen i Babel, hafver rådslagit om eder, och hafver något i sinnet emot eder.
31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
Nu upp, drager upp emot ett folk, som nog hafver, och bor säkert, säger Herren; de hafva hvarken portar eller bommar, och de bo allena för sig,
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
Deras cameler skola bortröfvade varda, och deras myckna boskap borttagen; och jag skall förströ dem i alla väder, de der i vråar bo; och på alla sidor skall jag låta deras olycka komma öfver dem, säger Herren.
33 “Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
Och Hazor skall varda till en drakaboning, och till ett evigt öde, så att der ingen bo skall, och ingen menniska deruti vistas.
34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
Detta är Herrans ord, som skedde till Jeremia Propheten, emot Elam, uti Zedekia, Juda Konungs rikes begynnelse, och sade:
35 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
Så säger Herren Zebaoth: Si, jag skall sönderbryta Elams båga, deras yppersta magt;
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
Och skall låta komma öfver dem de fyra väder, utaf fyra himmelens ändar, och skall förströ dem uti all de vädren, att intet folk vara skall, dit icke ju någre fördrefne af Elam komma skola.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
Och jag skall göra Elam förtviflad för deras fiendar, och för dem som stå efter deras lif, och låta olycko komma öfver dem med mine grymma vrede, säger Herren; och skall sända svärdet efter dem, tilldess jag gör en ända uppå dem.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
Min stol skall jag sätta i Elam, och skall förgöra der både Konung och Förstar, säger Herren.
39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.
Men i tillkommande tid skall jag vända Elams fängelse om igen, säger Herren.