< Yeremiya 49 >

1 Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
За синове Амонове: Овако вели Господ: Зар Израиљ нема синове? Зар нема наследнике? Зашто Малхом наследи земљу Гадову? И зашто се народ његов насели у његовим градовима?
2 Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
Зато ево иду дани, говори Господ, кад ћу учинити да се чује вика убојна у Рави синова Амонових, и она да буде гомила развалина, и села њена попаљена огњем; и Израиљ ће овладати онима који беху њим овладали, говори Господ.
3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Ридај Есевоне, јер је Гај опустошен, вичите села равска, припашите око себе кострет, наричите и трчите око плотова; јер ће Малхом отићи у ропство, свештеници његови и кнезови његови скупа.
4 Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Што се хвалиш долинама? Растопила се долина твоја, кћери одметницо! Која се уздаш у благо своје: Ко би ударио на ме?
5 Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
Ево ја ћу пустити на те страх од свуда унаоколо, говори Господ Господ над војскама, и распршаћете се сви, и неће бити никога да скупи бежан.
6 “Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
Али ћу после повратити робље синова Амонових, говори Господ.
7 Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
За Едома, овако вели Господ над војскама: Зар нема више мудрости у Теману? Неста ли савета разумнима? Ишчиле ли мудрост њихова?
8 Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Бежите, обратите плећи, заврите се дубоко, становници дедански, јер ћу пустити на Исава погибао његову у време кад ћу га походити.
9 Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Да ти дођу берачи, не би ли ти оставили пабирака? Да дођу лупежи ноћу, не би ли однели колико им је доста?
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
Али ја оголузних Исава, открих потаје његове да се не може сакрити; пропаде семе његово, браћа његова и суседи његови, нико не оста.
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
Остави сироте своје, ја ћу им живот сачувати, и удовице твоје нека се уздају у ме.
12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
Јер овако вели Господ: Ево, који не би требало да пију из чаше, доиста ће пити; а ти ли ћеш остати без кара? Нећеш остати без кара, него ћеш зацело пити.
13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
Јер собом се заклињем, говори Господ, да ће Восора бити пустош, руг, чудо и проклетство, и сви ће градови њени бити пустиња вечна.
14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
Чух глас од Господа, и гласник би послан к народима да рече: Скупите се и идите на њу, и дигните се у бој.
15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
Јер гле, учинићу те да будеш мали међу народима и презрен међу људима.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Обест твоја и поноситост срца твог превари тебе, који живиш у раселинама каменим и држиш се високих хумова; да начиниш себи гнездо високо као орао, и оданде ћу те свалити, говори Господ.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
И земља ће едомска бити пустиња, ко прође мимо њу, свак ће се чудити и звиждати ради свих рана њених.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
Као кад се затре Содом и Гомор и суседство њихово, вели Господ, неће се населити онде нико нити ће се бавити онде син човечји.
19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
Гле, као лав изаћи ће подижући се више него Јордан на стан Силнога; али ћу га брзо отерати из те земље, и поставићу над њом оног ко је изабран; јер ко је као ја? И ко ће се прети са мном? И који ће ми пастир одолети?
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Зато чујте намеру Господњу што је наумио за Едомце и мисли његове што је смислио за становнике теманске: заиста најмањи из стада развлачиће их, заиста ће опустети стан с њима.
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
Од праске падања њиховог земља ће се трести, и вика ће се њихова чути на црвеном мору.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Гле, доћи ће и долетеће као орао и рашириће крила своја над Восором, и биће срце у јунака едомских као срце у жене која се порађа.
23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
За Дамаск. Посрами се Емат и Арфад, јер чу зле гласе; растопише се, страх је на мору, не може се умирити.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
Дамаск клону, обрати се да бежи, дрхат га подузе, туга и болови освојише га као породиљу.
25 Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
Како се не остави славни град? Град радости моје?
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Зато ће попадати младићи његови на улицама његовим, и сви ће војници његови изгинути у онај дан, говори Господ над војскама.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
И распалићу огањ у зидовима дамаштанским, и прождреће дворе Вен-Ададове.
28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
За Кидар и за царства асорска, која разби Навуходоносор цар вавилонски, овако вели Господ: Устаните, идите на Кидар, и затрите синове источне.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
Узеће им шаторе и стада, завесе њихове и судове њихове и камиле њихове отеће, и викаће на њих страшно одсвуда.
30 “Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
Бежите, селите се далеко, сакријте се дубоко, становници асорски, говори Господ, јер је Навуходоносор цар вавилонски намерио намеру против вас, и смислио мисао против вас.
31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
Устаните, идите к народу мирном, који живи без страха, говори Господ, који нема врата ни преворница, живе сами.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
И камиле ће њихове бити плен, и мноштво стоке њихове грабеж, и расејаћу их у све ветрове, оне што се с краја стрижу, и довешћу погибао на њих са свих страна, говори Господ.
33 “Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
И Асор ће бити стан змајевски, пустиња до века: нико се неће онде населити, нити ће се бавити у њему син човечји.
34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
Реч Господња која дође Јеремији пророку за Елам, у почетку царовања Седекије цара Јудиног, говорећи:
35 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
Овако вели Господ над војскама: Ево, ја ћу сломити лук Еламу, главну силу његову;
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
И довешћу на Елам четири ветра с четири краја небеса, и у све те ветрове расејаћу их, тако да неће бити народа куда неће отићи прогнаници еламски.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
И уплашићу Еламце пред непријатељима њиховим, и пред онима који траже душу њихову; и пустићу зло на њих, жестину гнева свог, говори Господ, и пустићу за њима мач докле их не затрем.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
И наместићу престо свој у Еламу, и истребићу оданде цара и кнезове, говори Господ.
39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.
Али у последње време повратићу робље еламско, говори Господ.

< Yeremiya 49 >