< Yeremiya 49 >

1 Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Mayelana labantwana bakoAmoni itsho njalo iNkosi: UIsrayeli kalamadodana yini? Kalayo indlalifa yini? Kungani uMilkomu esidla ilifa lakoGadi, labantu bakhe behlala emizini yayo?
2 Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
Ngakho khangela, insuku ziyeza, itsho iNkosi, lapho ngizakwenza ukuthi kuzwakale umkhosi wempi eRaba yabantwana bakoAmoni; njalo izakuba yinqumbi yencithakalo, lamadodakazi ayo atshiswe ngomlilo; loIsrayeli adle ilifa labadla ilifa lakhe, itsho iNkosi.
3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Qhinqa isililo, Heshiboni, ngoba iAyi ichithiwe; khalani, madodakazi eRaba, libhince amasaka, lilile, liye le lale ezintangweni; ngoba uMilkomu uzahamba ekuthunjweni, abapristi bakhe leziphathamandla zakhe ndawonye.
4 Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Uzincomelani ngezihotsha? Isihotsha sakho siyageleza, ndodakazi ehlehlela nyovane, ethemba amagugu ayo, usithi: Ngubani ozakuza kimi?
5 Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
Khangela, ngizakwehlisela phezu kwakho uvalo, itsho iNkosi, uJehova wamabandla, luvela kubo bonke abakuhanqileyo; njalo lizaxotshwa, ngulowo lalowo phambi kwakhe; njalo kakho ozabutha ozulayo.
6 “Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
Kodwa emva kwalokho ngizabuyisa ukuthunjwa kwabantwana bakoAmoni, itsho iNkosi.
7 Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Mayelana leEdoma, itsho njalo iNkosi yamabandla: Kakuselanhlakanipho yini eThemani? Icebo liphelile yini kwabaqedisisayo? Inhlakanipho yabo isinyamalele yini?
8 Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Balekani, buyelani emuva, hlalani endaweni ejulileyo, bahlali beDedani; ngoba ngizakwehlisela inhlupheko kaEsawu phezu kwakhe, isikhathi sokumhambela kwami.
9 Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Uba abavuni bamavini befika kuwe bebengayikutshiya yini umkhothozo? Uba amasela efika ebusuku, azaphanga aze anele?
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
Kodwa mina ngimhlubule uEsawu, ngizembule indawo zakhe zensitha, ukuze angabi lakho ukucatsha; inzalo yakhe ichithiwe, labafowabo, labomakhelwane bakhe, yena kasekho.
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
Tshiya izintandane zakho, mina ngizazilondoloza ziphila, labafelokazi bakho kabathembele kimi.
12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
Ngoba itsho njalo iNkosi: Khangela, labo okugwetshwa kwabo kwakungeyisikho ukunatha inkezo bazayinatha lokuyinatha, wena-ke nguwe yini ozayekelwa ungajeziswanga ngokupheleleyo? Kawuyikuyekelwa ungelacala, kodwa isibili uzanatha.
13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
Ngoba ngifungile ngami uqobo, itsho iNkosi, ukuthi iBhozira izakuba ngokwesabekayo, ibe lihlazo, ibe lunxiwa, ibe yisiqalekiso; lemizi yayo yonke izakuba ngamanxiwa aphakade.
14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
Ngizwile umbiko ovela eNkosini, lesithunywa sithunywe phakathi kwezizwe, sisithi: Buthanani, lize limelane layo, lisukumele impi.
15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
Ngoba khangela, ngizakwenza ube mncinyane phakathi kwezizwe, udeleleke phakathi kwabantu.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Ukwesabeka kwakho kukukhohlisile, ukuziqhenya kwenhliziyo yakho, wena ohlala ezingoxweni zamadwala, obamba izingqonga zoqaqa. Loba usenza isidleke sakho sibe phezulu njengokhozi, ngizakwehlisa usuka khona, itsho iNkosi.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
IEdoma layo izakuba yinto eyesabekayo; wonke odlula kuyo uzamangala kakhulu, ancife ngenxa yenhlupheko yonke yayo.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
Njengokuchithwa kweSodoma leGomora, labomakhelwane bayo, itsho iNkosi; kakulamuntu ozahlala khona, kakulandodana yomuntu ezahlala khona njengowezizwe.
19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
Khangela, njengesilwane esivela ekukhukhumaleni kweJordani uzakwenyuka emelene lendawo yokuhlala okungapheliyo, kodwa ngizahle ngimgijimise asuke kuyo; njalo ngubani okhethiweyo engingammisa emelene layo? Ngoba ngubani onjengami? Ngubani-ke ozangibizela ukulandisa? Njalo nguwuphi lowomelusi ongema phambi kwami?
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Ngakho, zwanini icebo leNkosi elicebe imelene leEdoma, lemicabango yayo eyicabange emelene labahlali beThemani: Isibili abancinyane bomhlambi bazabadonsa; isibili izachitha indawo yabo yokuhlala phezu kwabo.
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
Ngomsindo wokuwa kwabo umhlaba uyazamazama; ukukhala, umsindo wakho wezwakala eLwandle oluBomvu.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Khangela, uzakwenyuka andize ngesiqubu njengokhozi, elulele impiko zakhe phezu kweBhozira; lenhliziyo yamaqhawe eEdoma ngalolosuku izakuba njengenhliziyo yowesifazana ohelelwayo.
23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
Mayelana leDamaseko. IHamathi leArpadi kuyangekile, ngoba bazwile umbiko omubi; bancibilika, kulokunqineka elwandle, kungeke kube lokuthula.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
IDamaseko isibuthakathaka, itshibilike ukuze ibaleke, lokwethuka kuyibambile, ukucindezelwa losizi kuyibambile njengobelethayo.
25 Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
Kawutshiywanga njani umuzi wodumo, umuzi wentokozo yami!
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Ngakho amajaha awo azawela ezitaladeni zawo, lawo wonke amadoda empi azabhujiswa ngalolosuku, itsho iNkosi yamabandla.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
Ngizaphemba-ke umlilo emdulini weDamaseko, ozaqothula izigodlo zikaBenihadadi.
28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
Mayelana leKedari njalo mayelana lemibuso yeHazori owayitshayayo uNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni: Itsho njalo iNkosi: Sukumani, lenyukele eKedari, lichithe amadodana empumalanga.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
Bazathatha amathente abo lemihlambi yabo, amakhetheni abo lempahla yabo yonke lamakamela abo bazazithwalela khona; bamemeze kibo bathi: Uvalo enhlangothini zonke.
30 “Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
Balekani, lizulazule kakhulu, lihlale ngokujula, lina bahlali beHazori, itsho iNkosi; ngoba uNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni waceba icebo emelene lani, wacabanga umcabango emelene lani.
31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
Sukumani, lenyuke limelene lesizwe esonwabileyo, esihlala ekuvikelekeni, itsho iNkosi, esingelamasango, esingelamigoqo, esizihlalele sodwa.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
Lamakamela abo azakuba yimpango, lemihlambi yezifuyo zabo izakuba yimpango; njalo ngizabachithachitha kuyo yonke imimoya, abaphoselwe engonsini, ngilethe inkathazo yabo evela inhlangothi zonke zaso, itsho iNkosi.
33 “Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
LeHazori izakuba yindawo yokuhlala yamakhanka, unxiwa kuze kube nininini; kakuyikuhlala muntu khona, lendodana yomuntu kayiyikuhlala kuyo njengowezizwe.
34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
Ilizwi leNkosi elafika kuJeremiya umprofethi limelene leElamu ekuqaleni kokubusa kukaZedekhiya, inkosi yakoJuda, lisithi:
35 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Khangela, ngizakwephula idandili leElamu, induna yamandla abo.
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
Ngilethele iElamu imimoya emine evela emikhawulweni emine yamazulu, ngibahlakazele kuyo yonke leyomimoya; njalo kakuyikuba khona isizwe lapho abaxotshiweyo beElamu abangayikufika khona.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
Ngoba ngizakwenza abeElamu besabe phambi kwezitha zabo laphambi kwalabo abadinga impilo yabo, ngibehlisele okubi, ukuvutha kolaka lwami, itsho iNkosi, ngithume inkemba emva kwabo, ngize ngibaqede.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
Ngizamisa-ke isihlalo sami sobukhosi eElamu, ngichithe kuyo inkosi leziphathamandla, itsho iNkosi.
39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.
Kodwa kuzakuthi ekucineni kwezinsuku ngibuyise ukuthunjwa kukaElamu, itsho iNkosi.

< Yeremiya 49 >