< Yeremiya 49 >

1 Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Ebikwata ku baana ba Amoni bye bino. Bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda nti, “Isirayiri terina baana balenzi? Terina basika? Lwaki Malukamu atutte Gaadi? Lwaki abantu be batutte ebibuga by’e Gaadi?
2 Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
Naye ennaku zijja,” bw’ayogera Mukama Katonda, “lwe ndiraya eŋŋoma ezirangirira olutalo ku Labba eky’abawala ba Amoni. Kirifuuka ntuumu ya mafunfugu, n’ebyalo ebiriraanyeewo byokebwe omuliro. Isirayiri eryoke egobere ebweru abo abagigoba,” bw’ayogera Mukama Katonda.
3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
“Kaaba, ggwe Kesuboni, kubanga Ayi kizikiridde! Mukaabe mmwe abatuuze b’omu Labba! Mwesibe ebibukutu mukungubage. Mudduke mudde eno n’eri mu bisenge by’ekibuga, kubanga Malukamu alitwalibwa mu busibe, awamu ne bakabona n’abakungu.
4 Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Lwaki mwenyumiriza olw’ebiwonvu byammwe, ne mwenyumiriza olw’ebiwonvu ebigimu? Ggwe omuwala atali mwesigwa, weesiga obugagga bwo n’ogamba nti, ‘Ani alinnumba?’
5 Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
Ndikuleetako entiisa, okuva mu abo bonna abakwetoolodde,” bw’ayogera Mukama, Mukama Katonda ow’Eggye. “Buli omu ku mmwe aligobebwa, era tewali n’omu alikuŋŋaanya abadduka.
6 “Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
“Naye oluvannyuma ndikomyawo nate omukisa gy’abaana ba Amoni,” bw’ayogera Mukama Katonda.
7 Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda ow’Eggye nti, “Tewakyali magezi mu Temani? Abeegendereza babuliddwa okutegeera? Amagezi gaabwe gaweddemu ensa?
8 Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Mukyuke mudduke mwekweke mu mpuku eziri ewala mmwe abatuuze b’e Dedani, kubanga ndireeta ekikangabwa ku Esawu, mu kiseera bwe ndimubonerereza.
9 Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Abanozi b’emizabbibu singa bazze gy’oli, tebandikuleseeko mizabbibu mibale bubazi? Singa ababbi bazze ekiro, tebandibbye byonna bye beetaaga?
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
Naye ndyambula Esawu mwerule; ndizuula ebifo bye mwe yeekweka, aleme kwekweka. Abaana be, n’ab’eŋŋanda ze n’ab’omuliraano baakuzikirira, era wa kuggwaawo.
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
Bamulekwa mu mmwe mubaleke, ndibalabirira. Ne bannamwandu mu mmwe banneesige.”
12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
Bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda nti, “Obanga abo abatandinywedde ku kikompe bawaliriziddwa okukinywako, lwaki mmwe temubonerezebwa? Temuuleme kubonerezebwa, mulina okukinywa.
13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
Neerayirira,” bw’ayogera Mukama Katonda nti, “Bozula alifuuka matongo era ekibuga ekijjudde entiisa, ekinyoomebwa era ekikolimire, era ebibuga bye byonna biriba matongo emirembe gyonna.”
14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
Mpulidde obubaka okuva eri Mukama Katonda. Omubaka yatumibwa eri amawanga okugamba nti, “Mwekuŋŋaanye mukirumbe! Mugolokoke mukole olutalo!”
15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
“Kaakano ndibafuula aba wansi ennyo mu mawanga, abanyoomebwa mu bantu.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Entiisa gy’oleeta n’amalala g’omutima gwo bikulimbye, mmwe ababeera mu bunnya bw’amayinja, mmwe ababeera waggulu mu nsozi. Wadde nga muzimba ebisu byammwe okubeera waggulu nga eby’empungu, ndibawanulayo ne mbasuula wansi,” bw’ayogera Mukama Katonda.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
“Edomu kirifuuka kyerolerwa, abo bonna abayitawo balyewuunya batye olw’ebiwundu bye byonna.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
Nga Sodomu ne Ggomola bwe byayonoonebwa, wamu n’ebibuga ebirala ebiriraanyeewo,” bw’ayogera Mukama Katonda, “tewaliba n’omu abibeeramu; tewali musajja alikituulamu.
19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
“Ng’empologoma eva mu bisaka by’omu Yoludaani okugenda mu muddo omugimu, ndigoba Edomu mu nsi ye amangu n’embiro. Ani oyo omulonde gwe nnaateekawo akole kino? Ani ali nga nze era ani ayinza okunsomooza? Era musumba wa ndiga ki ayinza okunjolekera?”
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Noolwekyo, muwulire Mukama Katonda kyategese okuleeta ku Edomu, kyategekedde abo abatuula mu Temani. Endiga ento mu bisibo za kuwalulwa, alyonoonera ddala ebisibo byazo ku lwabwe.
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
Bwe baligwa ensi erikankana, emiranga gyabwe giriwulirwa mu Nnyanja Emyufu.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Laba, alibuuka mu bire ng’empungu n’atumbiira, n’alyoka akka ng’ayanjululiza ebiwaawaatiro bye ku Bozula. Ku lunaku olwo emitima gy’abalwanyi ba Edomu giribeewanika ng’ogw’omukazi alumwa okuzaala.
23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
Ebikwata ku Damasiko: “Kamasi ne Alupaadi biweddemu amaanyi, kubanga biwulidde amawulire amabi. Bakeŋŋentereddwa, batabuddwa ng’ennyanja esiikuuse, tebasobola kutereera.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
Ddamasiko ayongobedde, akyuse adduke era okutya kumukutte; obubalagaze n’obuyinike bimunyweezezza, obulumi nga obw’omukazi alumwa okuzaala.
25 Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
Lwaki ekibuga ekimanyiddwa tebakidduse, ekibuga mwe nsanyukira?
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Ddala abavubuka baakyo baligwa mu nguudo, n’abalwanyi baakyo bonna ku olwo baakusirisibwa,” bw’ayogera Mukama Katonda ow’Eggye.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
“Ndiyokya bbugwe wa Ddamasiko omuliro; gwakumalawo n’embiri za Benukadaadi.”
28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
Bino bye bikwata ku Kedali n’obwakabaka bwa Kazoli, obwalumbibwa Nebukadduneeza kabaka w’e Babulooni. Bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda nti, “Golokoka, olumbe Kedali ozikirize abantu be bugwanjuba.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
Weema zaabwe n’ebisibo byabwe bya kutwalibwa; enju zaabwe ziryetikkibwa n’ebintu byabwe byonna n’eŋŋamira zaabwe. Abasajja balibakanga nga bawowoggana nti, ‘Akabi kavudde ku buli ludda!’
30 “Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
“Mudduke mwekukume mangu! Mubeere mu mpuku empanvu, mmwe abatuuze b’omu Kazoli,” bw’ayogera Mukama Katonda. “Nebukadduneeza kabaka w’e Babulooni abasalidde olukwe; ategese okubalumba.
31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
“Golokoka olumbe eggwanga eriri mu ggandaalo, eriri mu kweyagala,” bw’ayogera Mukama Katonda, “eggwanga eritalina miryango gisibwa wadde ebyuma; abantu baalyo babeera awo bokka.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
Eŋŋamira zaabwe zaakunyagibwa, n’amagana gaabwe amanene gatwalibwe. Ndibasaasaanya eri empewo, abo abali mu bifo eby’ewala, mbaleeteko akabi okuva ku buli ludda,” bw’ayogera Mukama Katonda.
33 “Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
“Kazoli alifuuka kifo kya bibe, ekifo eky’amatongo eky’emirembe n’emirembe. Tewali alikibeeramu; tewali muntu alikituulamu.”
34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
Kino kye kigambo kya Mukama Katonda ekyajjira nnabbi Yeremiya ekikwata ku Eramu, nga Zeddekiya kabaka wa Yuda kyajje alye obwakabaka.
35 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
Bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda ow’Eggye nti, “Laba, ndimenya omutego gwa Eramu, amaanyi gaabwe mwe gasinga okwesigibwa.
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
Era ndireeta ku Eramu empewo ennya, okuva mu bitundu ebina eby’eggulu; ndibasaasaanyiza eri empewo ezo ennya, era tewaliba nsi n’emu abawaŋŋanguse ba Eramu gye bataliddukiramu.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
Ndimenyeramenyera Eramu mu maaso g’abalabe be, mu maaso gaabo abamunoonya okumutta; ndibatuusaako ekikangabwa, n’obusungu bwange obungi ennyo,” bw’ayogera Mukama Katonda. “Ndibawondera n’ekitala okutuusa lwe ndibamalirawo ddala.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
Nditeeka entebe yange ey’obwakabaka mu Eramu era nzikirize kabaka we n’abakungu be,” bw’ayogera Mukama Katonda.
39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.
“Wabula ekiseera kijja, lwe ndiddiramu Eramu,” bw’ayogera Mukama Katonda.

< Yeremiya 49 >