< Yeremiya 49 >
1 Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Et tous les chefs de l'armée, Joanan, Azarias, fils de Maasie, et tout le peuple, du petit au grand, allèrent trouver Jérémie le prophète, et ils lui dirent:
2 Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
Que notre appel à la compassion soit devant ta face. Prie le Seigneur ton Dieu pour les restes de notre peuple; car de beaucoup que nous étions, nous sommes restés fort peu, comme tu le vois de tes yeux.
3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Et que le Seigneur ton Dieu nous fasse connaître la voie où nous devons marcher, et la parole qu'il nous faut accomplir.
4 Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Et Jérémie leur dit: J'ai entendu, voilà que je prierai pour vous le Seigneur mon Dieu, selon vos paroles; et la parole que me répondra le Seigneur Dieu, je vous la ferai connaître, et je ne vous en cacherai aucune chose.
5 Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
Et ils dirent: Que le Seigneur soit entre nous un témoin juste et vrai, si nous n'agissons selon toute parole que le Seigneur nous enverra.
6 “Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
Qu'elle nous annonce du bien ou du mal, la voix du Seigneur, vers qui nous t'envoyons, nous l'écouterons, afin qu'il en aille mieux pour nous, parce que nous aurons écouté la voix du Seigneur notre Dieu.
7 Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Et dix jours après la parole du Seigneur vint à Jérémie.
8 Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Et il appela Joanan, et les chefs de l'armée, et tout le peuple, du petit au grand;
9 Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Et il leur dit: Voici ce que dit le Seigneur:
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
Si vous demeurez en cette terre, je vous réédifierai, et ne vous abattrai pas; je vous planterai et ne vous arracherai pas, parce que je mets un terme aux maux que je vous ai faits.
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
N'ayez plus peur du roi de Babylone, que vous craignez, n'ayez plus peur de lui, dit le Seigneur; car je suis avec vous pour vous délivrer et vous sauver de leurs mains.
12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
Et je vous ferai miséricorde, et j'aurai compassion de vous, et je vous ramènerai en votre terre.
13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
Et si vous dites: Nous ne demeurerons pas en cette terre pour ne plus entendre la voix du Seigneur.
14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
Nous irons en Égypte, et nous ne verrons pas la guerre, et nous n'entendrons pas le son des trompettes, et nous ne manquerons pas de pain, et nous demeurerons en cette terre.
15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
Si vous dites cela, écoutez la parole du Seigneur: Voici ce que dit le Seigneur: Si vous tournez votre face vers l'Égypte, si vous y entrez pour y demeurer,
16 Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Ceci adviendra: le glaive que vous craignez vous trouvera en Égypte, et la famine, dont l'aspect vous donne tant d'inquiétude, marchera derrière vous et vous atteindra en Égypte, et vous y mourrez.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
Et tous les Hébreux et tous les prosélytes qui auront tourné leur face vers l'Égypte pour y demeurer périront par le glaive ou par la famine, et aucun d'eux n'échappera aux maux que j'amènerai sur eux.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
Car voici ce que dit le Seigneur: De même que ma colère est tombée sur les habitants de Jérusalem, ainsi ma colère tombera goutte à goutte si vous entrez en Égypte; et vous serez en abomination, vous serez assujettis, maudits, outragés, et vous ne verrez plus cette terre.
19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
Voici ce que vous dit le Seigneur, ô restes de Juda: N'entrez pas en Égypte, et maintenant sachez
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Que vous avez agi avec malice en vos âmes, quand vous m'avez envoyé, disant: Prie pour nous le Seigneur, et nous nous conduirons selon tout ce que le Seigneur te dira.
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
Et vous avez entendu la parole du Seigneur qu'il m'a envoyée pour vous.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Et vous périrez par le glaive et la famine dans le lieu où vous voulez aller pour vous y établir.
23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 “Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 “Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.