< Yeremiya 49 >

1 Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Concerning the sons of Ammon: “Thus said YHWH: Has Israel no sons? Has he no heir? Why has Malcam possessed Gad, And his people have dwelt in its cities?
2 Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
Therefore, behold, days are coming, A declaration of YHWH, And I have sounded a shout of battle in Rabbah of the sons of Ammon, And it has been for a heap—a desolation, And her daughters are burned with fire, And Israel has succeeded its heirs, said YHWH.
3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Howl, Heshbon, for Ai is spoiled, Cry, daughters of Rabbah, gird on sackcloth, Lament, and go to and fro by the hedges, For Malcam goes into captivity, His priests and his princes together.
4 Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Why do you boast yourself in valleys? Your valley is flowing, O backsliding daughter, Who is trusting in her treasures: Who comes to me?
5 Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
Behold, I am bringing fear in on you, A declaration of Lord YHWH of Hosts, From all around you, And you have each been driven out before it, And there is no gatherer of the wandering.
6 “Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
And after this I return the captivity of the sons of Ammon, A declaration of YHWH.”
7 Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Concerning Edom: “Thus said YHWH of Hosts: Is wisdom no longer in Teman? Has counsel perished from the intelligent? Has their wisdom vanished?
8 Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Flee, turn, go deep to dwell, you inhabitants of Dedan, For I brought the calamity of Esau on him, The time I inspected him.
9 Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
If gatherers have come to you, They do not leave gleanings, If thieves in the night, They have destroyed their sufficiency!
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
For I have made Esau bare, I have uncovered his secret places, And he is not able to be hidden, Spoiled [is] his seed, and his brothers, And his neighbors, and he is not.
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
Leave your orphans—I keep alive, And your widows—trust on Me,
12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
For thus said YHWH: They whose judgment is not to drink of the cup, Do certainly drink, And you [are] he that is entirely acquitted! You are not acquitted, for you certainly drink.
13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
For I have sworn by Myself, A declaration of YHWH, That for a desolation, for a reproach, For a dry place, and for a reviling—is Bozrah, And all her cities are for continuous ruins.
14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
I have heard a report from YHWH, And an ambassador is sent among nations, Gather yourselves and come in against her, And rise for battle.
15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
For behold, I have made you little among nations, Despised among men.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Your terribleness has lifted you up, The pride of your heart, O dweller in clefts of the rock, Holding the high place of the height, For you make your nest high as an eagle, From there I bring you down, A declaration of YHWH.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
And Edom has been for a desolation, Everyone passing by her is astonished, And hisses because of all her plagues.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
As the overthrow of Sodom and Gomorrah, And its neighbors, said YHWH, No one dwells there, Nor does a son of man sojourn in her.
19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
Behold, he comes up as a lion, Because of the rising of the Jordan, To the enduring habitation, But I cause to rest, I cause him to run from off her, And who is chosen? I lay a charge concerning her, For who is like Me? And who convenes Me? And who [is] this shepherd who stands before Me?
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Therefore, hear the counsel of YHWH, That He has counseled concerning Edom, And His plans that He has devised Concerning the inhabitants of Teman: Do little ones of the flock not drag them out, Does He not make their habitation desolate?
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
The earth has shaken from the noise of their fall, The cry—its voice is heard at the Sea of Suph.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Behold, He comes up as an eagle, and flies, And He spreads His wings over Bozrah, And the heart of the mighty of Edom has been in that day, As the heart of a travailing woman.”
23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
Concerning Damascus: “Hamath and Arpad have been ashamed, For they have heard an evil report, They have been melted, sorrow [is] in the sea, It is not able to be quiet.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
Damascus has been feeble, She turned to flee, and fear strengthened her, Distress and pangs have seized her, as a travailing woman.
25 Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
How it is not left—the city of praise, The city of My joy!
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Therefore her young men fall in her broad places, And all the men of war are cut off in that day, A declaration of YHWH of Hosts.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
And I have kindled a fire against the wall of Damascus, And it consumed palaces of Ben-Hadad!”
28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
Concerning Kedar, and concerning the kingdoms of Hazor that Nebuchadnezzar king of Babylon has struck: “Thus said YHWH: Arise, go up to Kedar, And spoil the sons of the east.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
They take their tents and their flock, Their curtains, and all their vessels, And they carry away their camels for themselves, And they called concerning them, Fear [is] all around.
30 “Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
Flee, bemoan mightily, go deep to dwell, You inhabitants of Hazor—a declaration of YHWH, For Nebuchadnezzar king of Babylon has given counsel against you, Indeed, he devises a scheme against them.
31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
Rise, go up to a nation at rest, Dwelling confidently, a declaration of YHWH, It has no double gates nor bar, They dwell alone.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
And their camels have been for a prey, And the multitude of their livestock for a spoil, And I have scattered them to every wind, Who cut off the corner [of the beard], And from all its passages I bring in their calamity, A declaration of YHWH.
33 “Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
And Hazor has been for a habitation of dragons, A desolation for all time, No one dwells there, nor does a son of man sojourn in it!”
34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
That which has been the word of YHWH to Jeremiah the prophet concerning Elam, in the beginning of the reign of Zedekiah king of Judah, saying,
35 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
“Thus said YHWH of Hosts: Behold, I am breaking the bow of Elam, The beginning of their might.
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
And I have brought four winds to Elam, From the four ends of the heavens, And have scattered them to all these winds, And there is no nation to where outcasts of Elam do not come in.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
And I have frightened Elam before their enemies, And before those seeking their life, And I have brought calamity on them, The heat of My anger, A declaration of YHWH, And I have sent the sword after them, Until I have consumed them;
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
And I have set My throne in Elam, And I have destroyed king and princes from there, A declaration of YHWH.
39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.
And it has come to pass, in the latter end of the days, I return the captivity of Elam, A declaration of YHWH!”

< Yeremiya 49 >