< Yeremiya 49 >
1 Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
BOEIPA loh Ammon ca rhoek ham he ni a thui. Israel te a ca om pawt tih anih aka pang khaw a om moenih a? Balae tih Gad Milkom loh a huul tih a khopuei kah a pilnam kho a sak.
2 Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
Te dongah BOEIPA kah olphong khohnin ha pawk tangloeng coeng he. Ammon koca Rabbah ah caemtloek tamlung ka yaak coeng tih khopong imrhong la poeh ni. A tanu te hmai neh a hlup uh ni. Amah aka huul rhoek te Israel loh koep a huul ni. He tah BOEIPA long ni a thui.
3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Ai te a rhoelrhak dongah Heshbon nang rhung laeh. Rabbah nu rhoek pang uh lamtah tlamhni vah laeh. Rhaengsae lamtah tanglung khuiah tinghil laeh. Milkom neh a khosoih rhoek, a mangpa khaw vangsawn la rhenten cet ni.
4 Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Hnukmael nu aw, balae tih tuikol te na yan? na tuikol khaw long coeng te. A thakvoh dongah pangtung ni, “Unim kai taengla aka pawk eh?” a ti.
5 Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
Na kaepvai boeih lamkah birhihnah te kai loh nang soah ka thoeng sak ni. He tah ka Boeipa caempuei Yahovah kah olphong ni. Hlang loh a mikhmuh ah a heh tih aka yong te khaw coi mahpawh.
6 “Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
Tedae he phoeiah ni Ammon ca rhoek khuikah thongtla te ka mael puei eh. He tah BOEIPA kah olphong ni.
7 Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Edom kawng he caempuei BOEIPA loh a thui. Teman ah cueihnah om voel pawt nim? Aka yakming lamkah cilsuep he bing tih amih kah cueihnah khaw awk aih.
8 Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Dedan khosa rhoek te thuh ham rhaelrham lamtah muelh hoihaeng uh laeh. Anih ka cawh tue ah tah Esau kah rhainah te anih soah ka thoeng sak ni.
9 Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Misur ka bit loh na taengla ha pawk koinih a yoep koi khaw paih mahpawh. Hlanghuen long khaw khoyin ah a ngaih te ni a phae eh.
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
Tedae Esau te ka baeh vetih a huephael te ka hliphen pah ni. Te vaengah thuh thai pawt vetih a tiingan neh, a manuca neh a imben khaw a rhoelrhak vetih amah khaw om mahpawh.
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
Na cadah rhoek te hnoo lamtah ka hing sak bitni. Te phoeiah na nuhmai ni kai dongah aka pangtung thai.
12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
BOEIPA loh he ni a thui. Amih kah tiktamnah mueh a mam ham aih ke. Boengloeng dongah a mam la a mam uh mai. Te dongah nang te m'hmil khaw m'hmil venim? M'hmil pawt vetih na mam rhoe na mam ni.
13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
BOEIPA kah olphong neh kamah loh ka toemngam coeng. Bozrah te imsuep la, kokhahnah la, kholing la, rhunkhuennah la om ni. A khopuei boeih te kumhal due imrhong la om ni.
14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
Olthang te BOEIPA taeng lamloh ka yaak coeng. Laipai khaw namtom taengah ka tueih coeng. Coi uh thae lamtah anih te paan uh laeh. Te phoeiah caemtloek la thoo uh laeh.
15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
Nang te namtom taengah tanoe neh hlang taengkah a hnaep la kang khueh ni ne.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Na mueipuelnah loh nang n'rhaithi coeng. Na lungbuei althanah neh thaelrhaep thaelpang ah aka om. Hmuensang som te na loh tihatha bangla na bu na sang sak cakhaw te lamloh nang te kan suntlak sak ni. He tah BOEIPA kah olphong ni.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
Edom te imsuep la om vetih aka pah boeih khaw a taengah pong uh ni. Te vaengah a hmasoe cungkuem neh hlip ni.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
Sodom, Gomorrah neh a imben te imrhong- la om coeng. BOEIPA loh, “A khuiah hlang loh khosa pawt vetih hlang capa khaw bakuep mahpawh,” a ti.
19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
Sathueng bangla Jordan mingthennah lamloh tolkhoeng puei la cet coeng ke. Anih so lamloh ka hoep uh vetih ka cungpoeh ni. Anih te coelh ham unim ka khueh eh? Kamah bang he unim, unim kai aka tuentah? Ka mikhmuh ah pai tih boiva aka dawn te unim?
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Te dongah BOEIPA loh Edom ham a uen cilsuep neh Teman khosa taengah a moeh a kopoek te hnatun uh. Boiva ca a koeng pah pawt atah a tolkhoeng khaw amih kongah pong mahpawt nim?
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
Amih kah cungku ol ah diklai he hinghuen vetih pangngawlnah ol te carhaek tuipuei duela a yaak uh ni.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Thahum bangla luei vetih tih ding ni ne. Te vaengah Bozrah te a phae a khuk thil ni. Te khohnin ah tah Edom hlangrhalh kah lungbuei te puencak nu kah lungbuei bangla om ni.
23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
Damasku ham olthang thae a yaak dongah Khamath neh Arpad yak coeng. Tuipuei mawnnah dongah paci tih mong thai pawh.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
Damasku te tahah tih rhaelrham ham a mael hatah lueihlaknah loh a cuuk thil. Citcai dongah ca-om nu bangla tharhui loh a doek.
25 Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
Ka omthennah khorha koehnah aih he, balae tih khopuei koehnah he a toeng pawh.
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Te dongah a toltung ah a tongpang rhoek cungku uh vetih caemtloek hlang boeih khaw te khohnin ah kuemsuem uh ni. Hetah caempuei BOEIPA kah olphong ni.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
Damasku vongtung te hmai ka hlup vetih Benhadad impuei khaw a hlawp ni.
28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
Nebukhanezar, Babylon manghai Nebukhanezar loh a ngawn Kedar neh Hazor ram kawng khaw BOEIPA loh a thui. Thoo lamtah Kedar te paan laeh, khothoeng ca rhoek ke rhoelrhak laeh.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
A dap neh a boiva te a rhawt pa uh ni. A himbaiyan neh a hnopai boeih khaw, amamih ham a kalauk neh a phueih uh vetih amih te a kaepvai ah rhihnah neh a doek uh ni.
30 “Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
Hazor khosak rhoek loh khosak ham rhaelrham lamtah muelh rhaehba khing mai laeh. He tah BOEIPA kah olphong ni. Babylon manghai Nebukhanezar te nang soah a cilsuep a uen tih a kopoek neh nang soah amih te a moeh.
31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
Thoo uh lamtah thayoeituipan neh ngaikhuek la aka om namtom te paan uh laeh. Amah bueng te kho a sak uh dongah thohkhaih om pawt tih thohkalh khaw om pawh. He tah BOEIPA kah olphong ni.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
A kalauk te maeh la, a boiva boeih te kutbuem la poeh ni. Baengki aka kuet khaw khohli cungkuem taengah ka thaek ni. Amih kah rhainah te kaepvai rhalvangan boeih lamloh ka thoeng sak ni. He tah BOEIPA kah olphong ni.
33 “Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
Hazor khaw kumhal kah khopong pongui kah khuirhung la poeh ni. Teah te hlang loh khosa pawt vetih a khuiah hlang capa khaw bakuep mahpawh.
34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
Judah manghai Zedekiah a ram a tongcuek vaengah Elam ham BOEIPA ol te tonghma Jeremiah taengla ha pawk.
35 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
“Caempuei BOEIPA loh he ni a thui. Elam kah a thayung thamal vueilue lii te ka khaem coeng he.
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
Vaan khobawt pali lamkah khohli pali te Elam taengla ka khuen ni. Te khohli cungkuem taengla amih te ka thaek vetih namtom hmuen khaw om mahpawh. Te kah te Elam khuiah Elam kah a heh long pataeng a pha moenih.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
Elam te a thunkha rhoek kah mikhmuh neh a hinglu aka toem rhoek mikhmuh ah ka rhihyawp sak ni. Ka thintoek thinsa te amih soah yoethae la ka thoeng sak ni. He tah BOEIPA kah olphong ni. Amih ka khah duela amih hnukah cunghang neh ka tueih ni.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
Elam ah ka ngolkhoel ka hol vetih te lamkah manghai neh mangpa rhoek te ka milh sak ni. He tah BOEIPA kah olphong ni.
39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.
Tedae hmailong kah khohnin a pha vaengah Elam kah thongtla, thongtla te ka mael rhoe ka mael sak ni. He tah BOEIPA kah olphong ni,” a ti.