< Yeremiya 48 >

1 Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
Ebikwata ku Mowaabu: Bw’ati bw’ayogera Mukama ow’Eggye, Katonda wa Isirayiri nti, “Zikisanze Nebo, kubanga kijja kuzikirizibwa, Kiriyasayimu kiswale kiwambibwe, ekigo eky’amaanyi kijja kuswala kimenyebwe.
2 Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
Mowaabu taddeyo kutenderezebwa; mu Kesuboni abantu balitegeka okugwa kwe, nga boogera nti, ‘Mujje, tumalewo ensi eyo.’ Nammwe, mmwe Madumeni mulisirisibwa, n’ekitala kirikugoberera.
3 Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
Muwulirize emiranga egiva e Kolonayimu, okwonoonekerwa n’okuzikirizibwa okunene.
4 Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
Mowaabu alimenyebwa; abawere ne bakaaba.
5 Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
Bakwata ekkubo erigenda e Lukisi, nga bwe bakungubaga ku luguudo olugenda e Kolonayimu, emiranga egy’okuzikirizibwa giwulirwa.
6 Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
Mudduke! Muwonye obulamu bwammwe; mubeere ng’ebisaka mu ddungu.
7 Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
Kubanga mwesiga ebikolwa byammwe n’obugagga bwammwe, nammwe mulitwalibwa ng’abaddu, ne Kemosi alitwalibwa mu buwaŋŋanguse awamu ne bakabona be n’abakungu be.
8 Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
Omuzikiriza alirumba buli kibuga, era tewali kibuga kiriwona. Ekiwonvu kiryonoonebwa n’olusenyu luzikirizibwe kubanga Mukama ayogedde.
9 Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
Muwe Mowaabu ebiwaawaatiro abuuke agende kubanga alifuuka matongo, ebibuga bye birizikirizibwa, nga tewali abibeeramu.
10 “Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
“Akolimirwe oyo agayaalira omulimu gwa Mukama Katonda. Akolimirwe oyo aziyiza ekitala kye okuyiwa omusaayi.
11 “Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
“Mowaabu abadde mirembe okuva mu buvubuka bwe, nga wayini gwe batasengezze, gwe bataggye mu kibya ekimu okumuyiwa mu kirala, tagenzeko mu buwaŋŋanguse. Kale awooma ng’edda, n’akawoowo ke tekakyukanga.
12 Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
Naye ennaku zijja,” bw’ayogera Mukama Katonda, “lwe ndituma basajja bange abaggya wayini mu bibya, era balimuyiwa ebweru; balittulula ensuwa ze baase n’ebibya bye.
13 Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
Awo Mowaabu alikwatibwa ensonyi olwa Kemosi, ng’ennyumba ya Isirayiri bwe yaswala bwe yeesiga Beseri.
14 “Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
“Oyinza otya okugamba nti, ‘Tuli balwanyi, abasajja abazira mu ntalo?’
15 Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Mowaabu alizindibwa n’ebibuga bye ne bizikirizibwa; abavubuka be abato bagende battibwe,” bw’ayogera Kabaka, erinnya lye ye Mukama Katonda ow’Eggye.
16 Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
“Okugwa kwa Mowaabu kusembedde; akabi katuuse.
17 Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
Mumubeesebeese mwenna abamwetoolodde, mwenna abamanyi ettutumu lye; mugambe nti, ‘Ng’Omuggo ogw’amaanyi ogw’obwakabaka gumenyese, ng’oluga olw’ekitiibwa lumenyese!’
18 “Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
“Mukke muve mu kitiibwa kyammwe mutuule ku ttaka, mmwe abatuuze b’Omuwala w’e Diboni, kubanga oyo azikiriza Mowaabu alibajjira azikirize ebibuga byammwe ebya bbugwe.
19 Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
Muyimirire ku luguudo mulabe, mmwe ababeera mu Aloweri. Mubuuze omusajja adduka, n’omukazi atoloka, mubabuuze nti, ‘Kiki ekiguddewo?’
20 Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
Mowaabu aswadde kubanga amenyesemenyese. Mukaabe muleekaane! Mulangiririre mu Alunoni nti Mowaabu kizikiridde.
21 Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
Okusala omusango kutuuse mu nsi ey’ensenyi ku Koloni ne ku Yaza ne ku Mefaasi,
22 Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
ne ku Diboni, ne ku Nebo ne ku Besudibulasayimu,
23 Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
ne ku Kiriyasayimu ne ku Besugamuli ne ku Besumyoni;
24 Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
ne ku Keriyoosi ne ku Bozula ne ku bibuga byonna eby’omu nsi ya Mowaabu ebiri ewala n’ebiri okumpi.
25 Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
Ejjembe lya Mowaabu lisaliddwako, n’omukono gwe gumenyese,” bw’ayogera Mukama Katonda.
26 “Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
“Mumutamiize; kubanga ajeemedde Mukama. Ka Mowaabu yekulukuunyize mu bisesemye bye, era asekererwe.
27 Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
Isirayiri tewagisekereranga? Baali bamukutte mu bubbi, olyoke onyeenye omutwe gwo ng’omusekerera buli lw’omwogerako?
28 Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
Muve mu bibuga byammwe mubeere mu njazi, mmwe ababeera mu Mowaabu. Mubeere ng’ejjiba erikola ekisu kyalyo ku mumwa gw’empuku.
29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
“Tuwulidde amalala ga Mowaabu amalala ge agayitiridde n’okwemanya, okwewulira kwe era n’okweyisa kwe era n’okwegulumiza kwe okw’omutima.
30 Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
Mmanyi obusungu bwe obutaliimu,” bw’ayogera Mukama Katonda, “okwenyumiriza kwe okutaliiko kye kugasa.
31 Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
Noolwekyo nkaabirira Mowaabu, olwa Mowaabu yenna nkaaba, nkungubagira abasajja ab’e Kirukeresi.
32 Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
Nkukaabira ggwe amaziga, nga Yazeri bw’akaaba, ggwe omuzabbibu gw’e Sibuna. Amatabi gammwe geegolola okutuuka ku nnyanja; gatuuka ku nnyanja y’e Yazeri. Omuzikiriza agudde ku bibala byo ebyengedde era n’emizabbibu.
33 Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
Essanyu n’okujaguza biggiddwa ku nnimiro ne ku bibanja bya Mowaabu. Nziyizza okukulukuta kwa wayini mu masogolero; tewali asogola ng’aleekaana olw’essanyu. Newaakubadde nga waliyo okuleekaana, okuleekaana okwo si kwa ssanyu.
34 “A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
“Amaloboozi g’okukaaba kwabwe galinnye okuva e Kesuboni okutuuka ku Ereyale, n’okutuuka ku Yakazi. Okuva e Zowaali okutuuka e Kolanayimu n’e Egulasuserisiya, kubanga n’amazzi g’e Nimulimu gakalidde.
35 Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
Ndiggyawo abo abawaayo ebiweebwayo mu bifo ebigulumivu e Mowaabu, ne bootereza n’obubaane eri bakatonda baabwe,” bw’ayogera Mukama Katonda.
36 “Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
“Noolwekyo omutima gwange gukaabira Mowaabu ng’endere; gukaaba ng’endere olw’abasajja b’e Kirukesi. Obugagga bwe baafuna buweddewo.
37 Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
Buli mutwe mumwe na buli kirevu kisaliddwako; buli mukono gutemeddwako na buli kiwato kisibiddwamu ebibukutu.
38 Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
Ku buli kasolya ka nnyumba e Mowaabu ne mu bifo awakuŋŋaanirwa, tewaliwo kintu kirala wabula okukungubaga, kubanga njasizzayasizza Mowaabu ng’ekibya ekitaliiko akyagala,” bw’ayogera Mukama Katonda.
39 “Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
“Ng’amenyeddwamenyeddwa! Nga bakaaba! Mowaabu ng’akyusa omugongo gwe olw’obuswavu! Mowaabu afuuse kyakusekererwa, ekyekango eri bonna abamwetoolodde.”
40 Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
Bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda nti: “Laba! Empungu ekka, ng’eyanjuluza ebiwaawaatiro byayo ku Mowaabu.
41 Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Ebibuga birikwatibwa n’ebigo biwambibwe. Ku lunaku olwo emitima gy’abalwanyi ba Mowaabu giribeera ng’omutima gw’omukazi alumwa okuzaala.
42 Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
Mowaabu alizikirizibwa, kubanga yajeemera Mukama.
43 Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
Entiisa n’obunnya n’omutego bibalindiridde, mmwe abantu ba Mowaabu,” bw’ayogera Mukama Katonda.
44 “Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
“Buli alidduka entiisa aligwa mu bunnya, n’oyo aliba avudde mu bunnya alikwatibwa omutego; kubanga ndireeta ku Mowaabu omwaka gw’okubonaabona kwe,” bw’ayogera Mukama Katonda.
45 “Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
“Mu kisiikirize kya Kesuboni, abadduka mwe bayimirira nga tebalina maanyi, kubanga omuliro guvudde mu Kesuboni, ennimi z’omuliro wakati mu Sikoni, era gw’okezza ebyenyi bya Mowaabu, n’obuwanga bw’abo abaleekaana nga beewaanawaana.
46 Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
Zikusanze ggwe, Mowaabu. Abantu b’e Kemosi bazikiridde, batabani bo batwaliddwa mu buwaŋŋanguse ne bawala bammwe mu busibe.
47 “Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.
“Ndikomyawo nate obugagga bwa Mowaabu mu nnaku ezijja,” bw’ayogera Mukama Katonda. Omusango Mowaabu gw’asaliddwa gukoma wano.

< Yeremiya 48 >