< Yeremiya 48 >

1 Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
Pa inge ma LEUM GOD Kulana El fahk ke acn Moab: “Pakomuta mwet Nebo, Siti selos uh kunausyukla! Sruoh tari siti Kiriathaim, Pot kulana we ikruiyuki, Ac mwet we akmwekinyeyuk;
2 Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
Oasku lun Moab wanginla. Mwet lokoalok elos sruokya acn Heshbon Ac akoo in sukela mutunfacl Moab nufon. Ac fah wanginla pusra lohngyuk in siti Madmen; Un mwet mweun ac fah mukuiyak in mweuni.
3 Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
Mwet in acn Horonaim wowoyak ac fahk, “Yoklana mwe lokoalok! Yoklana mwe ongoiya!”
4 Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
“Sikiyukla acn Moab. Lohng ke tulik uh tung.
5 Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
Lohng pusren mwemelil lalos Ke elos ututyak innek nu Luhith, Ac tung in ongoiya lalos Ke elos tufokla ke innek nu Horonaim.
6 Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
Elos fahk, ‘Sulaklak, kaing! Suk moul lowos! Kasrusr oana soko donkey lemnak yen mwesis!’
7 Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
“Moab, kom filiya lulalfongi lom in ku lom ac mwe kasrup lom, Tusruktu, kom ac fah kutangyukla. Chemosh, god lom, fah utukla nu in sruoh, Wi fisrak ac mwet tol lal.
8 Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
Siti nukewa ac fah kunausyukla; Infahlfal uh ac acn tupasrpasr ac fah sikiyukla pac. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.
9 Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
Tulokunak sie eot in kulyuk lun acn Moab. Ac tia paht el musalla. Siti we ac fah filfilla in kulawi, Ac wangin mwet fah sifilpa muta we.” (
10 “Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
Selngawiyuk mwet se su tia oru orekma lun LEUM GOD ke insial nufon! Selngawiyuk mwet se su sruokya cutlass natul in tia aksororye srah!)
11 “Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
LEUM GOD El fahk, “Oemeet me acn Moab oanna okak — soenna utukla nu in sruoh. Moab el oana wain ma filiyuki in oan sraholu — tia mokleyuk ku okwok liki sufa nu ke sufa, pwanang emah uh, ac fohlo, tia ekla; oanna wo.
12 Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
“Tusruktu pacl se ac tuku ke nga fah supwala mwet in okoala acn Moab oana wain. Elos fah okoala nwe ke lisr, ac elos fah fukulya sufa uh nu ke ip sririk.
13 Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
Na mwet Moab ac fah tia sifil lulalfongel Chemosh, god lalos, oana ke mwet Israel tuh fuhleak lulalfongi lalos kacl Bethel, sie god elos tuh lulalfongi meet.
14 “Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
“Mukul Moab, efu kowos ku fahk mu kowos mwet mweun watwen, Mwet pulaik ac fokoko ke mweun?
15 Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Moab ac siti we kunausyukla; Mukul fusr pisrla we anwuki. Nga pa tokosra, LEUM GOD Kulana, Ac nga pa fahk ma inge.
16 Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
Mwe ongoiya lulap apkunme in sun acn Moab; Mwe keok lal uh ac sa na sikyak.
17 Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
“Tungi mutunfacl sac, kowos su muta apkuran, Kowos nukewa su etu pungal. Fahk mu, ‘Ku lun tokosrai lal musalla; Wolana ac ku lal wanginla.’
18 “Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
Kowos su muta Dibon, Tufokme liki acn fulat suwos Ac muta fin fohk uh in kutkut uh. Mwet se ma ac kunausla Moab oasr inge, El kunausla tari pot ku we.
19 Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
Kowos su muta Aroer, Tu sisken inkanek uh ac soano. Siyuk selos su kaing Lah mea sikyak.
20 Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
Na elos ac topuk, ‘Acn Moab ikori. Kowos in tungi, mweyen Moab el arulana tonongla. Sulkakinelik pe Infacl Arnon Lah Moab sikiyukla!’
21 Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
“Nununku tuku tari nu fin siti inge su oan yen tupasrpasr: Holon, Jahzah, Mephaath,
22 Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
Dibon, Nebo, Beth Diblathaim,
23 Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
Kiriathaim, Bethgamul, Bethmeon,
24 Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
Kerioth, ac Bozrah. Nununku tuku nu fin siti nukewa in acn Moab, loes ac apkuran.
25 Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
Ku lun Moab itungyuki; kufwen mwe mweun lal kipatpatu. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.”
26 “Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
LEUM GOD El fahk, “Oru acn Moab in sruhila, mweyen el utuk nunak lainyu. Moab el fah ipippip in woht lal sifacna, ac mwet uh ac isrunul.
27 Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
Moab, kom esam ke kom aksruksruki mwet Israel? Kom lumahlos oana un mwet ingunyar.
28 Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
“Kowos su muta in Moab, tuyak som liki siti suwos ac muta fin fulu uh, oana wuleoa ma oru ahng lalos sisken acn oatu in eot uh.
29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
Moab el arulana inse fulat! Nga lohng luman filang, enum ac ekak lun mwet we, ac lah elos arulana nunku kaclos sifacna.
30 Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
Nga, LEUM GOD, etu ke tungak lalos. Konkin lalos uh wanginna sripa, ac ma elos oru ac tiana oan paht.
31 Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
Ke ma inge nga fah tungi mwet nukewa in acn Moab, oayapa ke mwet Kir Heres.
32 Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
Nga fah tungi mwet Jazer, ac nga ac tungi mwet Sibmah yohk liki. Siti Sibmah, kom oana oa in grape soko ma lah kac tupalla sun Meoa Misa, ac som pacna nwe Jazer. Tusruktu inge grape sunom ac fokinsak lom ke pacl fol uh sikiyukla.
33 Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
Wanginla pusren engan ac insewowo in facl Moab, sie acn ma wo fohk we. Nga tulokinya wain in tia soror liki nien orek wain. Wanginna mwet in fut grape uh, oru wangin sasa ke engan.
34 “A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
“Mwet Heshbon ac Elealeh wowoyak tung, ac pusralos ku in lohngyuk oe Jahaz. Ku in lohngyuk pac sin mwet Zoar, ac lohngyuk pac e Horonaim ac Eglath Shelishiyah. Finne infacl srisrik Nimrim, paola pac.
35 Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
Nga fah tulokinya mwet Moab liki orek mwe kisa firir ke acn in alu lalos, ac liki orek kisa nu sin god lalos. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.
36 “Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
“Ouinge insiuk eoksra kacl Moab ac ke mwet Kir Heres, oana sie mwet su oru on in pukmas ke mwe ukuk natul, mweyen ma nukewa lalos wanginla.
37 Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
Ke sripen asor lalos, elos nukewa mangsrasrala ac kalla altalos. Elos nukewa sipik paolos, ac nukum nuknuk yohk eoa.
38 Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
Fin lohm nukewa Moab ac ke nien toeni nukewa, wangin ma orek sayen eoksra, mweyen nga fukulya acn Moab oana soko sufa fukulyuki ma wangin mwet enenu.
39 “Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
Kowos in wowoyak ke tung, mweyen acn Moab fukulyuki ac akmwekinyeyuk. El kunanula ac mutunfacl nukewa raunelak israsrinkusrael. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.”
40 Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
LEUM GOD El wulela mu sie mutunfacl ac fah tuhwi nu fin Moab, oana sie eagle ma asroelik posohksok lal,
41 Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
na siti ac pot ku nukewa ac fah sruoh. In len sac mwet mweun lun Moab ac fah arulana sangeng, oana sie mutan ke pacl in isus lal.
42 Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
Moab ac sikiyuk tuh in tia sifilpa sie mutunfacl, mweyen el likkeke lainyu.
43 Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
Sangeng, ac luf, ac sruhf oan soano mwet Moab. LEUM GOD pa fahk ma inge.
44 “Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
Kutena mwet su srike in kaingla liki mwe aksangeng inge fah putatyang nu in luf uh, ac kutena mwet su fanyak liki luf uh, ac fah sremla ke sruhf, mweyen LEUM GOD El oakiya tari pacl in kalyei nu sin Moab.
45 “Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
Mwet uh kaing in suk molela in acn Heshbon, siti se ma Tokosra Sihon el tuh leumi meet, tusruktu firiryak acn we. E uh esukak mangon eol ac masrol lun acn sin mwet Moab su lungsena orek mweun.
46 Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
Pakomuta mwet Moab! Kunausyukla mwet ma alu nu sel Chemosh, ac utukla wen ac acn natulos nu in sruoh.
47 “Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.
Tusruktu sie len, LEUM GOD El ac fah sifil akwoyeak acn Moab. LEUM GOD El fahk lah ma inge nukewa ac sikyak nu ke acn Moab.

< Yeremiya 48 >