< Yeremiya 48 >

1 Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
A Moab. Ainsi parle Yahweh des armées, Dieu d'Israël: Malheur à Nabo, car elle est ravagée; Cariathaïm est couverte de honte, elle est prise; la forteresse est couverte de honte, elle est abattue;
2 Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
elle n'est plus, la gloire de Moab! A Hésebon on médite contre lui le mal: Allons et exterminons-le d'entre les nations! Toi aussi, Madmen, tu seras réduite au silence, l'épée marche derrière toi.
3 Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
Des cris partent de Horonaïm; dévastation et grande ruine!
4 Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
Moab est brisé; ses petits enfants font entendre des cris.
5 Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
Oui! à la montée de Luith il y a des pleurs, on la gravit en pleurant; oui! à la descente de Horonaïm, on entend les cris de détresse.
6 Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
Fuyez, sauvez vos vies! Qu’elles soient comme une bruyère dans la lande!
7 Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
Car, puisque tu as mis ta confiance en tes ouvrages et en tes trésors, toi aussi tu seras conquis; et Chamos ira en exil, avec ses prêtres et ses princes, tous ensemble.
8 Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
Le dévastateur viendra contre toutes les villes, et pas une ville n'échappera; la vallées sera ruinée, et le plateau saccagé, comme l'a dit Yahweh.
9 Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
Donnez des ailes à Moab, car il faut qu'il s'envole; ses villes seront dévastées, sans qu'il y ait d'habitant.
10 “Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
Maudit soit celui qui fait mollement l'œuvre du Seigneur! Maudit celui qui refuse le sang à son épée!
11 “Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
Moab a été tranquille depuis sa jeunesse; il a reposé sur sa lie; il n'a pas été vidé d'un vase dans un autre, et il n'est pas allé en captivité. Aussi son goût lui est-il resté, et son parfum ne s'est pas altéré.
12 Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
C’est pourquoi voici que des jours viennent, — oracle Yahweh, où je lui enverrai des transvaseurs qui le transvaseront; ils videront ses vases, et ils briseront ses cruches.
13 Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
Et Moab aura honte de Chamos, comme la maison d'Israël a eu honte de Béthel, en qui était sa confiance.
14 “Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
Comment pouvez-vous dire: " Nous sommes des guerriers, des hommes vaillants au combat? "
15 Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Moab est ravagé, ses villes montent en fumée, l'élite de ses jeunes gens descend pour la boucherie; — oracle du roi, dont le nom est Yahweh des armées.
16 Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
La ruine de Moab approche, son malheur vient en grande hâte.
17 Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
Consolez-le, vous tous, ses voisins, et vous tous qui connaissez son nom, dites: " Comment a été brisé un bâton si fort, un sceptre si magnifique? "
18 “Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
Descends de ta gloire et assieds-toi sur la terre aride, habitante, fille de Dibon; car le dévastateur de Moab est monté contre toi, il a renversé tes remparts.
19 Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
Tiens-toi sur le chemin, et observe, habitante d'Aroër; interroge celui qui fuit et celle qui s'échappe; dis: " Qu'est-il arrivé? —
20 Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
" Moab est confus, car il est renversé. Poussez des gémissements et des cris! Annoncez sur l'Arnon que Moab est ravagé! "
21 Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
Un jugement est venu sur le pays de la plaine, sur Hélon, sur Jasa, sur Méphaath,
22 Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
sur Dibon, sur Nabo, sur Beth-Deblathaïm,
23 Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
sur Cariathaïm, sur Beth-Gamul, sur Beth-Maon,
24 Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
sur Carioth, sur Bosra et sur toutes les villes du pays de Moab, éloignées et proches.
25 Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
La corne de Moab est abattue, et son bras est brisé, — oracle de Yahweh.
26 “Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
Enivrez-le; car il s'est élevé contre Yahweh! que Moab se vautre dans son vomissement, et qu'il devienne un objet de risée, lui aussi!
27 Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
Israël n'a-t-il pas été pour toi un objet de risée? L'a-t-on surpris avec des voleurs, pour que, chaque fois que tu parlés de lui, tu hoches la tête?
28 Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
Abandonnez les villes; demeurez dans les rochers, habitants de Moab, et soyez comme la colombe qui fait son nid au-dessus du précipice béant.
29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
Nous avons entendu l'orgueil de Moab, le très orgueilleux, sa hauteur, son orgueil, sa fierté, et la fierté de son cœur.
30 Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
Moi aussi je connais, — oracle de Yahweh, sa jactance, et ses vains discours, et ses œuvres vaines.
31 Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
C'est pourquoi je me lamente sur Moab; sur tout Moab je pousse des cris; on gémit sur les gens de Qir-Hérès.
32 Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
Plus encore que sur Jazer, je pleure sur toi, vigne de Sabama. Tes sarments dépassaient la mer, ils touchaient à la mer de Jazer. Sur ta récolte et sur ta vendange le dévastateur s'est jeté.
33 Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
La joie et l'allégresse ont disparu des vergers et de la terre de Moab; j'ai fait tarir le vin des cuves; on ne le foule plus au bruit des hourrahs; le hourrah n'est plus le hourrah.
34 “A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
A cause du cri de Hésébon jusqu'à Eléalé; jusqu'à Jasa, ils font entendre leur cri; de Segor jusqu'à Horonaïm, jusqu'à Eglath-Sélisia; Car même les eaux de Nemrim seront taries.
35 Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
Je veux, en finir avec Moab, — oracle de Yahweh, avec celui qui monte à son haut-lieu et offre de l’encens à son dieu.
36 “Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
C'est pourquoi mon cœur au sujet de Moab, gémit comme une flûte, oui, mon cœur au sujet des gens de Qir-Hérès, gémit comme une flûte. C'est pourquoi le gain qu'ils avaient fait est perdu.
37 Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
Car toute tête est rasée, et toute barbe coupée; sur toutes les mains il y a des incisions; et sur les reins des sacs.
38 Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
Sur tous les toits de Moab et sur ses places, ce ne sont que lamentations; car j'ai brisé Moab comme un vase dont on ne veut plus, — oracle de Yahweh.
39 “Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
Comme il est brisé! Gémissez! Comme Moab a honteusement tourné le dos! Moab est devenu un objet de risée, et d'épouvante pour tous ses voisins.
40 Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
Car ainsi parle Yahweh: Voici qu'il prend son vol comme l'aigle, il étend ses ailes sur Moab.
41 Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Carioth est prise, les forteresses sont emportées, et le cœur des guerriers de Moab est, en ce jour, comme le cœur d'une femme en travail.
42 Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
Moab est exterminé du rang des peuples, parce qu'il s'est élevé contre Yahweh.
43 Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
Epouvante, fosse et filet, sont sur toi, habitant de Moab! — oracle de Yahweh.
44 “Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
Celui qui fuit devant l'objet d'épouvante tombera dans la fosse, et celui qui remontera de la fosse sera pris au filet; car je vais faire venir sur lui, sur Moab, l'année de sa visitation, — oracle de Yahweh.
45 “Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
A l'ombre de Hésébon ils s'arrêtent, les fuyards à bout de forces; mais il est sorti un feu de Hésébon, et une flamme du milieu de Séhon; elle a dévoré les flancs de Moab et le crâne des fils du tumulte.
46 Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
Malheur à toi, Moab! Il est perdu, le peuple de Chamos; car tes fils sont emmenés en exil, et tes filles en captivité.
47 “Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.
Mais je ramènerai les captifs de Moab; à la fin des jours, — oracle de Yahweh. Jusqu'ici le jugement de Moab.

< Yeremiya 48 >