< Yeremiya 48 >

1 Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
Against Moab, thus says the Lord of hosts, the God of Israel: “Woe upon Nebo! For it has been devastated and confounded. Kiriathaim has been seized; the strong one has been confounded and has trembled.
2 Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
There is no longer any rejoicing in Moab over Heshbon. They have devised evil. ‘Come and let us destroy it as a nation.’ Then you will be utterly silenced, and the sword will pursue you.
3 Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
A voice of clamor from Horonaim: devastation and great destruction!
4 Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
Moab has been crushed. Announce an outcry for her little ones.
5 Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
For, along the ascent of Luhith, the mourner will ascend with weeping. For, on the descent of Horonaim, the enemies have heard the wailing of devastation.
6 Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
Flee, save your lives! And you shall be like a saltcedar tree in the desert.
7 Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
For because you have had faith in your fortifications and in your storehouses, you too will be seized. And Chemosh will go into captivity: his priests and his leaders together.
8 Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
And the despoiler will overwhelm every city, and not a single city will be saved. And the valleys will perish, and the fields will be destroyed. For the Lord has spoken.
9 Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
Give a blossom to Moab. For it will depart when it is blossoming. And its cities will become desolate and uninhabited.
10 “Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
Cursed is he who does the work of the Lord deceitfully. And cursed is he who prohibits his sword from blood.
11 “Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
Moab has been fertile from his youth, and he has rested amid his brood. And he has not been transferred from vessel to vessel, nor has he gone into the transmigration. Therefore, his taste has remained with him, and his scent has not changed.
12 Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
Because of this, behold, the days are approaching, says the Lord, when I will send to him those who will line up and knock down his bottles, and they will knock him down and empty his vessels, and they will break their bottles against one another.
13 Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
And Moab will be confounded by Chemosh, just as the house of Israel was shamed by Bethel, in which they had faith.
14 “Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
How can you say: ‘We are strong and robust men of battle?’
15 Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Moab has been devastated, and they have cut down her cities. And her elect young men have descended to slaughter. So says the King, whose name is the Lord of hosts.
16 Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
The passing away of Moab draws near and arrives. Its evil will rush forward with great speed.
17 Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
Console him, all you who surround him and all you who know his name. Say: ‘How has the strong staff become broken, the glorious staff?’
18 “Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
Descend from your glory, and sit in thirst, O habitation of the daughter of Dibon! For the destroyer of Moab has ascended to you; he has dissipated your fortifications.
19 Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
Stand in the way, and gaze out, O habitation of Aroer! Question him who is fleeing, and say to him who has escaped: ‘What has happened?’
20 Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
Moab has been confounded, because he has been conquered. Wail and cry out! Announce it in Arnon: Moab has been devastated,
21 Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
and judgment has arrived upon the land of the plains: upon Holon, and upon Jahzah, and upon Mephaath,
22 Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
and upon Dibon, and upon Nebo, and upon the house of Deblathaim,
23 Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
and upon Kiriathaim, and upon the house of Gamul, and upon the house of Meon,
24 Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
and upon Kerioth, and upon Bozrah, and upon all the cities of the land of Moab, those far away and those nearby.
25 Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
The horn of Moab has been cut away, and his arm has been crushed, says the Lord.
26 “Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
Inebriate him, for he has lifted himself up against the Lord. And Moab will thrust his hand into his own vomit, and also now he himself will become a derision.
27 Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
For Israel had been a derision to them. It was as if you had discovered him among thieves. Because of your own words, then, which you have spoken against him, you will be led away captive.
28 Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
Relinquish the cities, and live upon a rock, O inhabitants of Moab, and be like a dove nesting at the mouth of an opening at the summit.
29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
We have listened to the arrogance of Moab; he is very proud: his exaltation, and arrogance, and pride, and the loftiness of his heart.
30 Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
I myself know, says the Lord, his boasting, and that his ability is not in accord with it, nor is it in accord with what he has been striving to do.
31 Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
For this reason, I will wail over Moab, and I will cry out to all of Moab, to the men on the brick wall who are lamenting.
32 Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
O vineyard of Sibmah, I will weep for you, with the mourning of Jazer. Your offshoots have crossed over the sea. They have reached even to the sea of Jazer. The despoiler has rushed over your harvest and your vintage.
33 Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
Rejoicing and exultation has been taken away from Carmel and from the land of Moab. And I have taken the wine from the winepresses. The treader of grapes will no longer sing the usual rhythmic chant.
34 “A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
From the outcry of Heshbon, even to Elealeh and Jahzah, they have uttered their voice; from Zoar, even to Horonaim, like a three year old calf. So too, the waters of Nimrim will be very bad.
35 Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
And I will take away from Moab, says the Lord, the one who makes offerings in exalted places, and the one who sacrifices to his gods.
36 “Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
Because of this, my heart will resound for Moab, like the pipes, and my heart will make a sound like the pipes for the men on the brick wall. For he has done more than he was able, yet still they have perished.
37 Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
For every head will be bald, and every beard will be shaved. All the hands will be bound together, and there will be haircloth on every back.
38 Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
Over all the rooftops of Moab, and in its streets, everyone will mourn. For I have crushed Moab like a useless vessel, says the Lord.
39 “Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
How was it conquered, so that they would wail? How is it that Moab has cast down his neck and been confounded? And Moab will be a derision and an example to everyone around him.”
40 Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
Thus says the Lord: “Behold, he will fly like the eagle, and he will extend his wings to Moab.
41 Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Kerioth has been captured, and the fortifications have been taken. And in that day, the heart of the strong ones of Moab will be like the heart of a woman giving birth.
42 Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
And Moab will cease to be a people. For he has been glorified against the Lord.
43 Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
Terror and the pit and the snare will overwhelm you, O inhabitant of Moab, says the Lord.
44 “Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
Whoever flees from the terror will fall into the pit. And whoever climbs out of the pit will be seized by the snare. For I will lead over Moab the year of their visitation, says the Lord.
45 “Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
Those fleeing from the snare stood in the shadow of Heshbon. For a fire has gone forth from Heshbon, and a flame from the midst of Sihon, and it will devour the portion of Moab, and the top of the head of the sons of tumult.
46 Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
Woe to you, O Moab! You have been ruined, O people of Chemosh! For your sons and your daughters have been taken into captivity.
47 “Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.
But I will convert the captivity of Moab in the last days, says the Lord.” Such are the judgments of Moab thus far.

< Yeremiya 48 >