< Yeremiya 48 >

1 Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
Israel Pathen caempuei BOEIPA loh Moab ham he ni a thui. Anunae Nebo aih te, a rhoelrhak neh yak vetih a tuuk ni. Kiriathaim khaw yak vetih a imsang khaw rhihyawp ni.
2 Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
Moab koehnah te koep om mahpawh. Heshbon ah anih te a moeh tih boethae loh a pongpa thil. Madmen khaw namtom lamloh saii uh sih. Namah hnukah cunghang loh m'paan daengah na kuemsuem bitni.
3 Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
Horonaim lamkah rhoelrhanah, pangngawlnah ol neh pocinah tanglue aih te.
4 Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
Moab te bawt vetih a pang te a canoi loh a yaak ni.
5 Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
Luhith kah Luhith tangkham te a rhah a rhah doeah luei. Horonaim singling ah khaw rhal taengkah pocinah pangngawlnah te a yaak uh.
6 Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
Rhaelrham lamtah na hinglu ham poenghal puei laeh. Khosoek kah koknai bangla na om coeng.
7 Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
Na bibi neh na thakvoh dongah na pangtung dongah namah khaw n'tuuk pawn ni. Khemosh kah a khosoih rhoek neh a mangpa rhoek vangsawn la rhenten a khuen ni.
8 Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
Khopuei tom ah aka rhoelrhak te ha pawk vetih khopuei te loeih mahpawh. BOEIPA loh a thui coeng dongah tuikol loh moelh vetih tlangkol tim ni.
9 Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
Moab te ding sak ham a phae pae lamtah khuen laeh saeh. A khopuei te imsuep la om vetih a khuiah khosa om mahpawh.
10 “Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
Vuelvaeknah neh BOEIPA kah bitat aka saii tah thae a phoei coeng tih thii lamloh a cunghang aka hloh khaw thae a phoei thil.
11 “Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
Moab he a camoe lamloh mong tih a sampa dongah mong te. Am khat lamloh am khat dongla kong noek pawt tih vangsawn la a caeh noek moenih. A khuikah a omih te cak tangloeng tih a bo khaw sap pawh.
12 Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
Te dongah BOEIPA kah olphong khohnin ha pawk tangloeng he. Hlang aka khuum rhoek te a taengla ka tueih vetih anih a khuum uh ni. A am te a khawk pah vetih a khap a thaeh pah ni.
13 Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
A pangtungnah Bethel kah Israel imkhui a yah bangla Khemosh kongah Moab te yak ni.
14 “Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
Balae tih, “Kaimih kah hlangrhalh rhoek neh tatthai hlang caemtloek la om,” na ti uh?
15 Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Moab a rhoelrhak vetih a khopuei rhoek te a khuen ni. A tongpang hlangrhoei rhoek te a maeh la suntla uh ni. A ming dongah caempuei BOEIPA manghai kah olphong ni.
16 Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
Moab rhainah ha pawk ham yoei coeng tih a boethae loh bahoeng loe ni.
17 Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
A kaepvai boeih neh a ming aka ming boeih loh anih te a suem uh tih, “Balae tih sarhi caitueng, boeimang cungkui khaw a paep,” ti uh laeh.
18 “Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
Dibon nu dongkah khosa rhoek aw thangpomnah dongkah khosak lamloh rhum lamtah tuihalh dongla ngol uh laeh. Moab aka rhoelrhak loh nang te m'paan vetih na hmuencak te a phae ni.
19 Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
Longpuei taengah pai lamtah Aroer khosa rhoek ke tawt ne. Aka rhaelrham pa neh aka loeih nu te dawt lamtah, “Balae aka om,” ti na uh.
20 Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
Moab khaw rhihyawp tih yak coeng. Rhung la, rhung lamtah pang khaw pang mai laeh. Moab a rhoelrhak te Arnon ah puen pah.
21 Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
Te dongah laitloeknah he tlangkol khohmuen la, Holon la, Jahzah neh Mephaath la,
22 Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
Dibon la, Nebo la, Bethdiblathaim la,
23 Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
Kiriathaim la, Bethgamul neh Bethmeon la,
24 Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
Kerioth la, Bozrah neh Moab khohmuen khopuei a yoei a hla boeih la pawk coeng.
25 Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
Moab ki ngun coeng tih a ban khaw khaem coeng. He tah BOEIPA kah olphong ni.
26 “Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
BOEIPA te a pantai thil dongah anih te rhuihmil sak. Te daengah ni Moab te a lok dongah kut a paeng vetih amah khaw nueihbu la a om eh.
27 Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
Israel khaw nang ham tah nueihbu la om het pawt nim? Na ol neh anih na hnet dingdoeng bangla hlanghuen lakli ah a hmuh khaw a hmuh a?
28 Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
Moab khosa rhoek aw khopuei te hnoo uh lamtah thaelpang ah khosa uh. Rhalvangan kah rhom rhai ah butuk uh lamtah, vahui bangla om uh.
29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
Moab kah hoemdamnah neh thinthah pangkha la a oeknah neh a hoemdamnah khaw, a hoemnah neh a lungbuei buhuengpomnah khaw ka yaak uh coeng.
30 Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
Kai tah BOEIPA kah a thinpom olphong khaw ka ming dae a olsai tangloeng pawt tih a saii van moenih.
31 Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
Te dongah Moab ham ka rhung tangloeng coeng, Moab ham a pum la ka pang. Kirhareseth hlang ham a thuep.
32 Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
Jazer kah a rhah lakah Sibam misur nang ham ka rhap. Na baek te tuipuei la yam tih Jazer tuipuei duela a pha. Na khohal thaih neh na misurbit te aka rhoelrhak loh a cuhu sak.
33 Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
Kohoenah neh omngaihnah he cangphil cangngol lamkah, Moab khohmuen lamkah ni. Tedae khum coeng tih, va-am dongkah misurtui ka kak sak. Tamlung khaw tamlung pawt ah, tamlung neh neet boel saeh.
34 “A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
Heshbon lamkah a pang te Elealeh duela, Jahaz duela, Zoar lamloh vaito Horonaim duela a ol a huel uh. Nimrim tui khaw rhaerhap la om coeng.
35 Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
He tah BOEIPA kah olphong ni. Moab kah hmuensang ah aka pongpa tih a pathen taengah aka phum rhoek te ka kangkuen sak ni.
36 “Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
Te dongah ka lungbuei he Moab ham tah phitphoet bangla cai tih ka lungbuei he Kirhareseth hlang ham phitphoet bangla cai. Te dongah koeva a tung te paltham coeng.
37 Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
A lu khaw boeih lungawng tih hmuimul khaw boeih a kuet uh. A kut hma khaw cungkuem tih, a cinghen ah tlamhni a yen.
38 Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
Moab imphu tom neh a toltung tom ah a rhaengsae uh. Moab te a ngaih pawh hnopai bangla ka phaek coeng. He tah BOEIPA kah olphong ni.
39 “Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
Rhihyawp tih rhung kanoek a? Moab loh rhawn a maelh te yak kanoek a? Te dongah Moab he nueihbu la, a kaepvai boeih te porhaknah la poeh.
40 Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
He ni BOEIPA loh a thui. atha bangla ding tih Moab soah a phae a khuk.
41 Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Kerioth te a tuuk vetih rhalmahim te a loh pah ni. Te khohnin ah tah Moab hlangrhalh lungbuei ah huta puencak kah lungbuei bangla om ni.
42 Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
BOEIPA te a taloeh thil dongah Moab he pilnam lamloh mitmoeng ni.
43 Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
Moab khosa nang ham birhihnah rhom neh pael om coeng lah ko. He tah BOEIPA kah olphong ni.
44 “Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
Ngaihuet neh birhihnah hmai lamloh aka rhaelrham te rhom ah cungku ni. Rhom lamloh aka yoeng te khaw pael neh a boh ni. Moab loh a sokah a cawhnah kum te amah soah ka thoeng sak ni.
45 “Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
Heshbon hlip ah aka pai te Heshbon lamkah hmai loh a coe thil tih thadueng om kolla rhaelrham coeng. Te vaengah Sihon laklo lamkah hmaisai loh Moab baengki neh longlonah ca rhoek kah luki te a hlawp pah.
46 Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
Anunae Moab nang aih te, Khemosh kah pilnam tah milh coeng. Na ca rhoek te tamna la, na canu rhoek tamna la a khuen uh coeng.
47 “Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.
Hmailong tue ah tah Moab thongtla te ka mael puei ni. BOEIPA kah olphong coeng ni. He hil he Moab ham laitloeknah coeng ni.

< Yeremiya 48 >