< Yeremiya 46 >

1 Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
Słowo Pańskie, które się stało do Jeremijasza proroka przeciwko tym narodom.
2 Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
Przeciwko Egiptowi. Przeciwko wojsku Faraona Necha, króla Egipskiego, (które było nad rzeką Eufrates u Karchemis, które poraził Nabuchodonozor, król Babiloński) roku czwartego Joakima, syna Jozyjaszowego, króla Judzkiego;
3 anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
Gotujcie tarcz i pawężę, a wychodźcie na wojnę;
4 Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
Zaprzęgajcie konie, a wsiadajcie jezdni, stańcie w hełmach, wycierajcie oszczepy, obleczcie się w pancerze.
5 Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
Czemuż tych widzę zatrwożonych, tył podawających, a mocarzy ich startych i prędko uciekających, tak, że się ani oglądają? Strach jest zewsząd, mówi Pan,
6 Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
Aby nie uciekł prędki, a nie uszedł mocarz; aby się na północy o brzeg rzeki Eufrates otrącili i upadli.
7 “Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
Któż to jest, który jako rzeka wzbiera? Którego się wody wzruszają jako rzeki?
8 Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
Egipt jako rzeka wzbiera, a jego wody wzruszają się jako rzeki, i mówi: Pociągnę, okryję ziemię, wygubię miasto, i tych, co w niem mieszkają.
9 Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
Poskoczcie konie, a zagrzmijcie wozy, a niech się ruszą i mocarze, Murzynowie, i Putejczycy noszący tarcz, i Ludymczycy, którzy noszą i ciągną łuk,
10 Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
Bo ten dzień panującego Pana zastępów będzie dzień pomsty, aby się pomścił nad nieprzyjaciołmi swymi, których miecz pożre, a nasyci się, i opije się krwią ich; bo ofiara panującego Pana zastępów będzie w ziemi północnej u rzeki Eufrates.
11 “Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
Wstąp do Galaad, a nabierz soku balsamowego, panno, córko Egipska! Aleć próżno używasz wiele lekarstw; bo nie będziesz uleczona.
12 Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
Narody usłyszą o sromocie twojej, a narzekanie twoje napełniło ziemię; bo mocarz na mocarza natarł, tak, że społem oba upadają.
13 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
Słowo, które mówił Pan do Jeremijasza, proroka, o tem, że ma przyjść Nabuchodonozor, król Babiloński, a porazić ziemię Egipską.
14 “Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
Oznajmijcie w Egipcie, a rozgłoście w Migdolu; opowiadajcie także w Nof, i w Tachpanches; rzeczcie: Postuj a nagotuj się; wszakże miecz pożre to, co jest około ciebie.
15 Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
Przecz porażony jest każdy z mocarzów twoich? Nie może się ostać, przeto, że Pan natarł nań.
16 Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
Wieleć będzie tych, którzy poszwankują a padną jeden na drugiego, i rzeką: Wstań, a wróćmy się do ludu naszego, i do ziemi urodzenia naszego przed ostrzem miecza pustoszącego.
17 Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
Tam będą wołać: Farao, król Egipski, jest tylko próżny trzask, już mu pominął czas postanowiony,
18 “Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
Jakom żywy Ja, mówi król, Pan zastępów imię jego; że jako Tabor między górami, i jako Karmel przy morzu, tak to przyjdzie.
19 Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
Spraw sobie naczynie przeprowadzenia, obywatelko, córko Egipska! bo Nof pustynią będzie i spustoszeje, i będzie bez obywatela.
20 “Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
Egipt jest jako piękna jałowica; ale zabicie jej od północy idzie, idzie.
21 Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
Więc i najemnicy jego w pośrodku niego są jako ciele utuczone, ale i oni także obróciwszy się uciekną społem, nie ostoją się; bo dzień porażki ich przyszedł na nich, czas nawiedzenia ich.
22 Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
Głos jego wynijdzie jako wężowy; bo z wojskiem idą, a z siekierami przyjdą nań, jako ci, co wyrąbują drzewo.
23 Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
Wyrąbią las jego, mówi Pan, choć policzony być nie może; bo się nad szarańczę rozmnożyli, i niemasz im liczby.
24 Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
Zawstydzi się córka Egipska; podana będzie w rękę ludu północnego.
25 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
Pan zastępów, Bóg Izraelski, mówi: Oto Ja nawiedzę ludne miasto No, także Faraona i Egipt, i bogów jego, i królów jego, Faraona mówię, i tych, którzy w nim ufają:
26 Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
I podam ich w rękę tych, którzy szukają duszy ich, to jest w rękę Nabuchodonozora, króla Babilońskiego, i ręką sług jego; lecz potem mieszkać w nim będą, jako za dawnych dni, mówi Pan.
27 “Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
Ale się ty nie bój, sługo mój Jakóbie! a nie lękaj się, o Izraelu! Bo oto Ja ciebie wybawię z daleka, i nasienie twoje z ziemi pojmania ich; i wróci się Jakób, aby odpoczywał i aby miał pokój, a nie będzie, ktoby go postraszył;
28 Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”
Ty, mówię, Jakóbie, sługo mój! nie bój się, mówi Pan; bom Ja z tobą. Uczynię zaiste koniec wszystkim narodom, do których cię wypędzę; lecz tobie nie uczynię końca, ale cię miernie karać będę, a cale cię bez karania nie zostawię.

< Yeremiya 46 >