< Yeremiya 46 >

1 Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
BOEIPA ol he Namtom ham tonghma Jeremiah taengla ha pawk.
2 Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
Judah manghai Josiah capa Jehoiakim kah a kum li dongah Perath tuiva kaep aha aka om tih, Babylon manghai Nebukhanezar loh a ngawn Karkhemish kah Egypt manghai Pharaoh Neko kah caem sokah Egypt kawng ni.
3 anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
Photlingca neh photlinglen neh rhongpai uh lamtah caemtloek ham thoeih uh laeh.
4 Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
Marhang te khit uh lamtah marhang caem khaw cet laeh saeh. Lumuek neh pai uh lamtah cai te met uh laeh. Caempho te bai uh laeh.
5 Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
Balae tih a paep neh a hnuk la aka balkhong te ka hmuh. Amih kah hlangrhalh rhoek khaw dae uh tih thuhaelhnah khuila rhaelrham uh coeng. Te dongah kaepvai kah rhihnah te mael uh thil pawh. He tah BOEIPA kah olphong ni.
6 Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
Kapyang khaw rhaelrham thai pawt tih hlangrhalh khaw loeih thai pawh. Tlangpuei kah Perath tuiva hmoi ah paloe uh tih cungku uh.
7 “Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
Sokko bangla aka phul tih tuiva tui bangla aka tuen he unim?
8 Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
Egypt tah sokko bangla phul tih tuiva tui bangla tuen. Te dongah, “Ka cet vetih diklai he ka khuk ni. Khopuei neh a khuikah khosa rhoek khaw ka milh sak ni,” a ti.
9 Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
Marhang rhoek te cet lamtah leng rhoek te yan uh laeh. Kusah hlangrhalh rhoek neh photlingca aka pom Put rhoek khaw, lii nuen ham aka tu Ludim rhoek khaw cet uh laeh.
10 Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
Tedae te khohnin tah, ka Boeipa Caempuei Yahovah kah a rhal rhoek taengah phuloh ham tawnlohnah khohnin coeng ni. Te dongah ka Boeipa Caempuei Yahovah taengkah hmueih la tlangpuei khohmuen Perath tuiva ah cunghang loh a cawk vetih amih thii neh a hah la hmilhmal ni.
11 “Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
Egypt nu, oila, Gilead la cet lamtah thingpi te lo laeh. Si tah a poeyoek la na puh na puh sak tih na saibawnnah hae moenih.
12 Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
Na yah te namtom loh a yaak vetih na henah te diklai ah khawk ni. Hlangrhalh soah hlangrhalh khaw paloe uh rhoi vetih a rhenten la cungku rhoi ni.
13 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
Babylon manghai Nebukhanezar loh Egypt khohmuen tloek ham ha pawk vaengah he ol he BOEIPA loh tonghma Jeremiah taengah a thui.
14 “Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
Egypt taengah puen lamtah Migdol ah khaw yaak sak. Noph neh Tahpanhes ah khaw yaak sak. “Pai uh lamtah namah ham rhuengphong laeh, na kaepvai te cunghang loh a cawk coeng,” ti nah.
15 Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
Aka lueng nang te balae tih ng'kawt mai eh? Anih te BOEIPA loh a thaek vetih pai tloel ni.
16 Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
Hlang loh a hui soah a cungku khaw paloe neh a khoep hae. Te dongah, “Thoo lamtah cunghang kah a vuelvaek hman ah mah pilnam taeng neh mah pacaboeina kah khohmuen la mael sih,” a ti uh ni.
17 Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
“Tingtunnah aka paan tah longlonah Egypt manghai Pharaoh,” tila hnap a hoe uh ni.
18 “Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
Kai hingnah manghai olphong tah a ming khaw caempuei BOEIPA ni. Te dongah tlang ah Tabor bangla, tuitunli ah Karmel bangla ha pawk ni.
19 Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
Egypt nu taengkah khosa loh namah ham vangsawn hnopai te saii laeh. Noph te imsuep la om vetih khosa a om pawt hil a hnueih ni.
20 “Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
Egypt bawnthen vaito aw tlangpuei lamkah pilyang ha pawk rhoe ha pawk coeng.
21 Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
A kutloh rhoek khaw a kotak ah vaitoca bangla toitup. Amih te oeih, hoilae uh vetih rhenten rhaelrham uh ni. Amih kah rhainah khohnin ah a cawhnah tue loh amih a thoeng thil coeng dongah pai uh mahpawh.
22 Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
A ol te rhul a colh vaengkah bangla, caem rhoek a khong vaengkah bangla, om tih hai neh thing top bangla anih taengah thoeih uh ni.
23 Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
He tah BOEIPA kah olphong ni. A duup te a hum pah ni. Kaisih lakah khaw a puh dongah hoem lek pawt tih amih te tae lek pawh.
24 Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
Tlangpuei pilnam kut ah a paek vaengah Egypt nu te yak bitni.
25 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
Israel Pathen caempuei BOEIPA loh, “No kah Amon neh Pharaoh, Egypt khaw, a pathen neh a manghai khaw, Pharaoh neh anih soah aka pangtung boeih te ka cawh coeng.
26 Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
Amih te a hinglu aka toem kut ah, Babylon manghai Nebukhanezar kut ah, anih kah sal kut ah ka tloeng ni. Tedae he phoeiah ni hlamat kum kah bangla kho a sak eh. He tah BOEIPA kah olphong ni.
27 “Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
Ka sal Jakob nang rhih boel lamtah Israel nang khaw rhihyawp boel saeh. Nang te khohla lamloh, na tiingan te a tamna khohmuen lamloh ka khang coeng ne. Te dongah Jakob ha mael vetih mong vetih rhalthal pawn ni. Te vaengah lakueng voel mahpawh.
28 Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”
Ka sal Jakob nang rhih boeh. He tah BOEIPA kah olphong ni. Nang taengah ka om tih namtom boeih kah a boeihnah te ka khueh coeng. Te ah te nang kang heh cakhaw nang kah a bawtnah te ka saii moenih. Nang te tiktamnah neh kan thuituen vetih nang te kam hmil rhoe kam hmil mahpawh.

< Yeremiya 46 >