< Yeremiya 45 >
1 Uwu ndi uthenga umene mneneri Yeremiya anawuza Baruki mwana wa Neriya mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa mwana ya Yosiya kuti alembe mʼbuku.
La parole que Jérémie, le prophète, adressa à Baruc, fils de Nérija, lorsqu’il écrivit dans un livre ces paroles, sous la dictée de Jérémie, la quatrième année de Jojakim, fils de Josias, roi de Juda. Il dit:
2 “Yehova Mulungu wa Israeli, akunena kwa iwe Baruki kuti:
Ainsi parle l’Éternel, le Dieu d’Israël, sur toi, Baruc:
3 Iwe unati, ‘Kalanga ine! Yehova wawonjezera chisoni pa mavuto anga. Ine ndatopa ndi kubuwula ndipo sindikupeza mpumulo.’”
Tu dis: Malheur à moi! Car l’Éternel ajoute le chagrin à ma douleur; je m’épuise en soupirant, et je ne trouve point de repos.
4 Koma Yehova akukuwuza kuti, “Ndidzagwetsa chimene ndinamanga ndipo ndidzazula chimene ndinadzala. Ndidzachita zimenezi mʼdziko lonse.
Dis-lui: Ainsi parle l’Éternel: Voici, ce que j’ai bâti, je le détruirai; ce que j’ai planté, je l’arracherai, savoir tout ce pays.
5 Kodi tsono ukudzifunira wekha zinthu zazikulu? Usadzifunire. Pakuti ndidzagwetsa mavuto pa anthu onse, koma ndidzasunga moyo wako kulikonse kumene ungadzapite.”
Et toi, rechercherais-tu de grandes choses? Ne les recherche pas! Car voici, je vais faire venir le malheur sur toute chair, dit l’Éternel; et je te donnerai ta vie pour butin, dans tous les lieux où tu iras.