< Yeremiya 45 >

1 Uwu ndi uthenga umene mneneri Yeremiya anawuza Baruki mwana wa Neriya mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa mwana ya Yosiya kuti alembe mʼbuku.
The word that Jeremiah the prophet spoke to Baruch, the son of Neriah, when he had written these words in a book, from the mouth of Jeremiah, in the fourth year of Jehoiakim, the son of Josiah, the king of Judah, saying:
2 “Yehova Mulungu wa Israeli, akunena kwa iwe Baruki kuti:
“Thus says the Lord, the God of Israel, to you, Baruch:
3 Iwe unati, ‘Kalanga ine! Yehova wawonjezera chisoni pa mavuto anga. Ine ndatopa ndi kubuwula ndipo sindikupeza mpumulo.’”
You have said: ‘Woe to me, a wretched man! For the Lord has added sorrow to my sorrow. I have labored in my groaning, and I have not found rest.’
4 Koma Yehova akukuwuza kuti, “Ndidzagwetsa chimene ndinamanga ndipo ndidzazula chimene ndinadzala. Ndidzachita zimenezi mʼdziko lonse.
Thus says the Lord: So shall you say to him: Behold, those whom I have built up, I destroy, and those whom I have planted, I uproot, even this entire land.
5 Kodi tsono ukudzifunira wekha zinthu zazikulu? Usadzifunire. Pakuti ndidzagwetsa mavuto pa anthu onse, koma ndidzasunga moyo wako kulikonse kumene ungadzapite.”
And are you seeking great things for yourself? Do not choose to seek them. For behold, I will lead evil over all that is flesh, says the Lord. But I will give your life to you unto salvation, in every place, wherever you may travel.”

< Yeremiya 45 >