< Yeremiya 44 >

1 Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
Beseda, ki je prišla Jeremiju glede vseh Judov, ki prebivajo v egiptovski deželi, ki prebivajo v Migdólu, v Tahpanhésu, v Nofu in v deželi Patrós, rekoč:
2 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
»Tako govori Gospod nad bojevniki, Izraelov Bog: ›Videli ste vse zlo, ki sem ga privedel nad Jeruzalem in nad vsa Judova mesta, in glejte, ta dan so ta opustošenje in noben človek ne prebiva tam
3 Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
zaradi njihove zlobnosti, ki so jo zagrešili, da me dražijo do jeze v tem, da so odšli zažigat kadilo in da služijo drugim bogovom, ki jih niso poznali niti oni, da, niti vaši očetje.
4 Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
Vendar sem vam pošiljal vse svoje služabnike preroke, vzdigujoče zgodaj in jih pošiljal, rekoč: ›O ne storite te gnusne stvari, ki jo sovražim.‹
5 Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
Toda niso prisluhnili niti nagnili svojega ušesa, da se odvrnejo od svoje zlobnosti, da ne bi zažigali kadila drugim bogovom.
6 Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
Zato sta bila moj bes in moja jeza izlita naprej in vžgana v Judovih mestih in na ulicah Jeruzalema; in ta so opustošena in zapuščena kakor ta dan.‹
7 “Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
Zaradi tega sedaj tako govori Gospod, Bog nad bojevniki, Izraelov Bog: ›Zakaj ste zagrešili to veliko zlo zoper svoje duše, da izmed sebe iztrebite moškega in žensko, otroka in dojenčka, ven iz Juda, da nikogar ne pustite, da preostane.
8 Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
V čem ste me dražili do besa z deli svojih rok, zažigajoč kadilo drugim bogovom v egiptovski deželi, kamor ste odšli, da prebivate, da se lahko sami odrežete in da ste lahko prekletstvo in graja med vsemi narodi zemlje?‹
9 Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
Mar ste pozabili zlobnost svojih očetov, zlobnost Judovih kraljev, zlobnost njihovih žena, svojo lastno zlobnost in zlobnost svojih žena, ki so jo zagrešili v Judovi deželi in na ulicah Jeruzalema?
10 Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
Niso se ponižali celó do tega dne, niti se niso bali, niti hodili po moji postavi, niti po mojih zakonih, ki sem jih postavil pred vas in vaše očete.
11 “Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
Zato tako govori Gospod nad bojevniki, Izraelov Bog: ›Glejte, svoj obraz bom naravnal zoper vas za zlo in da iztrebim vsega Juda.
12 Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
Vzel bom preostanek Juda, ki so svoje obraze naravnali, da gredo v egiptovsko deželo, da začasno prebivajo tam in vsi bodo použiti in padli v egiptovski deželi; torej použiti bodo z mečem in z lakoto. Umrli bodo, od najmanjših celo do največjih, z mečem in z lakoto, in bodo preziranje in osuplost, prekletstvo in graja.
13 Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
Kajti kaznoval bom tiste, ki prebivajo v egiptovski deželi, kakor sem kaznoval Jeruzalem, z mečem, z lakoto in s kužno boleznijo,
14 Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
tako da ne bo nihče izmed Judovega preostanka, ki so odšli v egiptovsko deželo, da začasno prebivajo tam, ušel ali preostal, da bi se vrnil v Judovo deželo, h kateri so imeli željo, da se vrnejo, da prebivajo tam. Kajti nihče se ne bo vrnil, razen tistih, ki bodo pobegnili.‹«
15 Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
Potem so vsi možje, ki so vedeli, da so njihove žene zažigale kadilo drugim bogovom in vse ženske, ki so stale poleg, velika množica, celo vse ljudstvo, ki prebiva v egiptovski deželi, v Patrósu, odgovorili Jeremiju, rekoč:
16 “Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
» Glede na besedo, ki si nam jo govoril v imenu Gospoda, ti ne bomo prisluhnili,
17 Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
temveč bomo zagotovo počeli katerokoli stvar, izhajajočo iz naših lastnih ust, da zažigamo kadilo kraljici neba in da ji izlivamo pitne daritve, kakor smo počeli mi in naši očetje, naši kralji in naši princi v Judovih mestih in na ulicah Jeruzalema, kajti tedaj smo imeli obilico živeža in smo bili dobro in nismo videli zla.
18 Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
Toda odkar smo prenehali zažigati kadilo kraljici neba in ji izlivati pitne daritve, smo bili v potrebi vseh stvari in smo použiti z mečem in z lakoto.«
19 Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
»In ko smo zažigale kadilo kraljici neba in ji izlivale pitne daritve, mar smo ji naredile kolačke, da jo obožujemo in ji izlivale pitne daritve, brez naših moških?«
20 Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
Potem je Jeremija rekel vsemu ljudstvu, moškim in ženskam in vsemu ljudstvu, ki mu je dalo ta odgovor, rekoč:
21 “Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
»Kadilo, ki ste ga zažigali po Judovih mestih in po ulicah Jeruzalema, vi in vaši očetje, vaši kralji, vaši princi in ljudstvo dežele, ali se jih ni Gospod spomnil in ali to ni prišlo v njegov um?
22 Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
Tako da Gospod ni mogel več trpeti zaradi zla vaših početij in zaradi ogabnosti, ki ste jih zagrešili; zato je vaša dežela opustošenje, osuplost in prekletstvo, brez prebivalca, kakor na ta dan.
23 Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
Ker ste zažigali kadilo in ker ste grešili zoper Gospoda in niste ubogali Gospodovega glasu, niti hodili po njegovi postavi, niti po njegovih zakonih, niti po njegovih pričevanjih, zato se vam je zgodilo to zlo, kakor na ta dan.«
24 Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
Poleg tega je Jeremija rekel vsemu ljudstvu in vsem ženskam: »Poslušajte besedo od Gospoda, ves Juda, ki ste v egiptovski deželi:
25 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
›Tako govori Gospod nad bojevniki, Izraelov Bog, rekoč: ›Vi in vaše žene ste tako govorili s svojimi usti in s svojo roko izpolnili, rekoč: ›Zagotovo bomo izvajali svoje zaobljube, ki smo se jih zaobljubili, da zažigamo kadilo kraljici neba in da ji izlivamo pitne daritve.‹ Zagotovo boste dokončali svoje zaobljube in zagotovo boste izvedli svoje zaobljube.
26 Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
Zato poslušajte besedo od Gospoda, ves Juda, ki prebiva v egiptovski deželi: ›Glejte, prisegel sem pri svojem velikem imenu, ‹ govori Gospod, ›da moje ime ne bo več imenovano v ustih kateregakoli moškega iz Juda in po vsej egiptovski deželi, rekoč: ›Gospod Bog živi.‹
27 Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
Glej, bedel bom nad njimi za zlo in ne za dobro; in vsi Judovi možje, ki so v egiptovski deželi, bodo použiti z mečem in z lakoto, dokler jih ne bo konec.
28 Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
Vendar se bo malo število, ki pobegne meču, vrnilo iz egiptovske dežele v Judovo deželo in ves preostanek Juda, ki so odšli v egiptovsko deželo, da tam začasno prebiva, bo vedel čigave besede bodo obstale, moje ali njihove.
29 “Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
To vam bo znamenje, ‹ govori Gospod, ›da vas bom kaznoval na tem kraju, da boste lahko vedeli, da bodo moje besede zagotovo obstale zoper vas v zlo.‹
30 Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”
Tako govori Gospod: ›Glejte, izročil bom faraona Hofrája, egiptovskega kralja, v roko njegovih sovražnikov in v roko tistih, ki strežejo po njegovem življenju, kakor sem Judovega kralja Sedekíja izročil v roko babilonskega kralja Nebukadnezarja, njegovega sovražnika in ki je stregel po njegovem življenju.‹«

< Yeremiya 44 >