< Yeremiya 44 >
1 Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
La parole qui vint à Jérémie pour tous les Juifs qui habitaient dans le pays d’Égypte, qui habitaient à Migdol, et à Takhpanès, et à Noph, et dans le pays de Pathros, disant:
2 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
Ainsi dit l’Éternel des armées, le Dieu d’Israël: Vous avez vu tout le mal que j’ai fait venir sur Jérusalem et sur toutes les villes de Juda; et voici, elles sont aujourd’hui un désert, et personne n’y habite,
3 Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
à cause de l’iniquité qu’ils ont commise pour me provoquer à colère, en allant brûler de l’encens pour servir d’autres dieux, qu’ils n’ont pas connus, eux, ni vous, ni vos pères.
4 Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
Et je vous ai envoyé tous mes serviteurs les prophètes, me levant de bonne heure et [les] envoyant, disant: Ne faites point cette chose abominable que je hais.
5 Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
Et ils n’ont pas écouté, et n’ont pas incliné leur oreille pour se détourner de leur iniquité, afin de ne pas brûler de l’encens à d’autres dieux;
6 Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
alors ma fureur et ma colère ont été versées [sur eux], et ont brûlé dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem; et elles sont devenues un désert, une désolation, comme [il paraît] aujourd’hui.
7 “Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
Et maintenant, ainsi dit l’Éternel, le Dieu des armées, le Dieu d’Israël: Pourquoi faites-vous un grand mal contre vos âmes, pour vous faire retrancher du milieu de Juda, homme et femme, enfant et celui qui tète, en sorte qu’il ne vous demeure aucun reste;
8 Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
en me provoquant par les œuvres de vos mains, en brûlant de l’encens à d’autres dieux dans le pays d’Égypte où vous êtes venus pour y séjourner, en sorte que vous soyez retranchés, et que vous deveniez une malédiction et un opprobre parmi toutes les nations de la terre?
9 Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
Avez-vous oublié les iniquités de vos pères, et les iniquités des rois de Juda, et les iniquités de leurs femmes, et vos iniquités, et les iniquités de vos femmes, commises dans le pays de Juda et dans les rues de Jérusalem?
10 Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
Ils ne se sont pas humiliés jusqu’à ce jour, et ils n’ont pas eu de crainte, et ils n’ont pas marché dans ma loi et dans mes statuts, que j’ai mis devant vous et devant vos pères.
11 “Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
C’est pourquoi, ainsi dit l’Éternel des armées, le Dieu d’Israël: Voici, je mets ma face contre vous pour le mal, et pour retrancher tout Juda!
12 Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
Et je prendrai le reste de Juda qui a tourné sa face pour aller dans le pays d’Égypte pour y séjourner; et ils seront tous consumés; ils tomberont dans le pays d’Égypte; ils seront consumés par l’épée [et] par la famine, depuis le petit jusqu’au grand; ils mourront par l’épée et par la famine, et ils seront une exécration, une désolation, et une malédiction, et un opprobre.
13 Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
Et je punirai ceux qui habitent dans le pays d’Égypte, comme j’ai puni Jérusalem par l’épée, par la famine, et par la peste;
14 Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
et, du reste de Juda qui est venu dans le pays d’Égypte pour y séjourner, il n’y aura ni réchappé ni résidu pour retourner dans le pays de Juda, où ils avaient le désir de retourner pour y habiter; car ils ne retourneront pas, sauf [quelques] réchappés.
15 Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
Et tous les hommes qui savaient que leurs femmes brûlaient de l’encens à d’autres dieux, et toutes les femmes qui se tenaient là, un grand rassemblement, et tout le peuple qui demeurait dans le pays d’Égypte, à Pathros, répondirent à Jérémie, disant:
16 “Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
Quant à la parole que tu nous as dite au nom de l’Éternel, nous ne t’écouterons pas;
17 Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
mais nous ferons certainement toute parole qui est sortie de notre bouche, en brûlant de l’encens à la reine des cieux, et en lui faisant des libations, comme nous avons fait, nous et nos pères, nos rois et nos princes, dans les villes de Juda, et dans les rues de Jérusalem; et nous étions rassasiés de pain, et nous étions à notre aise, et nous ne voyions pas de malheur.
18 Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
Mais depuis que nous avons cessé de brûler de l’encens à la reine des cieux et de lui faire des libations, nous manquons de tout, et nous sommes consumés par l’épée et par la famine.
19 Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
Et si nous avons brûlé de l’encens à la reine des cieux, et si nous lui avons fait des libations, est-ce sans nos maris que nous lui avons fait des gâteaux à son image, ou que nous lui avons fait des libations?
20 Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
Et Jérémie parla à tout le peuple, aux hommes et aux femmes, et à tout le peuple qui lui avait répondu [cette] parole, disant:
21 “Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
Ne sont-ce pas ces encensements que vous avez faits dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem, vous et vos pères, vos rois et vos princes et le peuple du pays, que l’Éternel s’est rappelés, et qui lui sont montés au cœur?
22 Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
Et l’Éternel ne put plus le supporter, à cause de l’iniquité de vos actions, [et] à cause des choses abominables que vous avez faites, et votre pays est devenu un désert, et une désolation, et une malédiction, de sorte qu’il n’y a pas d’habitant, comme [il paraît] aujourd’hui.
23 Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
Parce que vous avez brûlé de l’encens, et que vous avez péché contre l’Éternel, et que vous n’avez pas écouté la voix de l’Éternel, et n’avez point marché dans sa loi, ni dans ses statuts, ni dans ses témoignages, à cause de cela ce mal vous est arrivé, comme [il paraît ] aujourd’hui.
24 Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
Et Jérémie dit à tout le peuple et à toutes les femmes: Écoutez la parole de l’Éternel, vous, tout Juda, qui êtes dans le pays d’Égypte:
25 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
Ainsi parle l’Éternel des armées, le Dieu d’Israël, disant: Vous et vos femmes, vous avez parlé de votre bouche, et vous avez accompli de vos mains, disant: Certainement nous accomplirons nos vœux que nous avons voués, pour brûler de l’encens à la reine des cieux et lui faire des libations. Vous ferez certainement selon vos vœux, et vous accomplirez certainement vos vœux.
26 Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
C’est pourquoi, écoutez la parole de l’Éternel, vous, tout Juda, qui habitez dans le pays d’Égypte: Voici, j’ai juré par mon grand nom, dit l’Éternel, que mon nom ne sera plus réclamé par la bouche d’aucun homme de Juda, dans tout le pays d’Égypte, disant: Le Seigneur, l’Éternel, est vivant!
27 Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
Voici, je veille sur eux pour le mal, et non pour le bien; et ils seront consumés, chaque homme de Juda qui est dans le pays d’Égypte, par l’épée et par la famine, jusqu’à ce qu’il n’y en ait plus.
28 Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
Et ceux qui échapperont à l’épée retourneront du pays d’Égypte dans le pays de Juda, un fort petit nombre; et ils sauront, tout ce reste de Juda, ceux qui sont venus dans le pays d’Égypte pour y séjourner, de qui, de moi ou d’eux, la parole s’accomplira.
29 “Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
Et ceci sera pour vous le signe, dit l’Éternel, que je vous punirai dans ce lieu, afin que vous sachiez que mes paroles s’effectueront certainement contre vous en mal.
30 Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”
Ainsi dit l’Éternel: Voici, je livre le Pharaon Hophra, roi d’Égypte, en la main de ses ennemis et en la main de ceux qui cherchent sa vie, comme j’ai livré Sédécias, roi de Juda, en la main de Nebucadretsar, roi de Babylone, son ennemi, celui qui cherchait sa vie.