< Yeremiya 44 >

1 Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
The word that came to Jeremiah concerning all the Jews who dwelt in the land of Egypt, who dwelt at Migdol, and at Tahpanhes, and at Memphis, and in the country of Pathros, saying,
2 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Ye have seen all the evil that I have brought upon Jerusalem, and upon all the cities of Judah. And, behold, this day they are a desolation. And no man dwells therein
3 Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
because of their wickedness which they have committed to provoke me to anger, in that they went to burn incense, and to serve other gods, that they knew not, neither they, nor ye, nor your fathers.
4 Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
However I sent all my servants the prophets to you, rising up early and sending them, saying, Oh, do not do this abominable thing that I hate.
5 Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
But they hearkened not, nor inclined their ear to turn from their wickedness, to burn no incense to other gods.
6 Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
Therefore my wrath and my anger was poured forth, and was kindled in the cities of Judah and in the streets of Jerusalem, and they are wasted and desolate, as it is this day.
7 “Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
Therefore now thus says Jehovah, the God of hosts, the God of Israel: Why do ye commit this great evil against your own souls, to cut off from you man and woman, infant and suckling, out of the midst of Judah, to leave you none remaining,
8 Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
in that ye provoke me to anger with the works of your hands, burning incense to other gods in the land of Egypt, where ye have gone to sojourn, that ye may be cut off, and that ye may be a curse and a reproach among all the nations of the earth?
9 Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
Have ye forgotten the wickedness of your fathers, and the wickedness of the kings of Judah, and the wickedness of their wives, and your own wickedness, and the wickedness of your wives which they committed in the land of Judah, and in the streets of Jerusalem?
10 Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
They are not humbled even to this day. Neither have they feared, nor walked in my law, nor in my statutes, that I set before you and before your fathers.
11 “Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
Therefore thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Behold, I will set my face against you for evil, even to cut off all Judah.
12 Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
And I will take the remnant of Judah, who have set their faces to go into the land of Egypt to sojourn there, and they shall all be consumed. In the land of Egypt they shall fall. They shall be consumed by the sword and by the famine. They shall die, from the least even to the greatest, by the sword and by the famine, and they shall be an execration, and an astonishment, and a curse, and a reproach.
13 Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
For I will punish those who dwell in the land of Egypt, as I have punished Jerusalem, by the sword, by the famine, and by the pestilence,
14 Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
so that none of the remnant of Judah who have gone into the land of Egypt to sojourn there, shall escape or be left to return into the land of Judah, to which they have a desire to return to dwell there. For none shall return except such as shall escape.
15 Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
Then all the men who knew that their wives burned incense to other gods, and all the women who stood by, a great assembly, even all the people who dwelt in the land of Egypt, in Pathros, answered Jeremiah, saying,
16 “Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
As for the word that thou have spoken to us in the name of Jehovah, we will not hearken to thee.
17 Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
But we will certainly perform every word that has gone forth out of our mouth, to burn incense to the queen of heaven, and to pour out drink offerings to her, as we have done, we and our fathers, our kings and our rulers, in the cities of Judah, and in the streets of Jerusalem. For then we had plenty of food, and were well, and saw no evil.
18 Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
But since we left off burning incense to the queen of heaven, and pouring out drink offerings to her, we have lacked all things, and have been consumed by the sword and by the famine.
19 Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
And when we burned incense to the queen of heaven, and poured out drink offerings to her, did we make her cakes to worship her, and pour out drink offerings to her, without our husbands?
20 Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
Then Jeremiah said to all the people, to the men, and to the women, even to all the people who had given him that answer, saying,
21 “Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
The incense that ye burned in the cities of Judah, and in the streets of Jerusalem, ye and your fathers, your kings and your rulers, and the people of the land, did Jehovah not remember them, and did it not come into his mind?
22 Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
So that Jehovah could no longer bear, because of the evil of your doings, and because of the abominations which ye have committed. Therefore your land has become a desolation, and an astonishment, and a curse, without inhabitant, as it is this day.
23 Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
Because ye have burned incense, and because ye have sinned against Jehovah, and have not obeyed the voice of Jehovah, nor walked in his law, nor in his statutes, nor in his testimonies, therefore this evil has happened to you, as it is this day.
24 Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
Moreover Jeremiah said to all the people, and to all the women, Hear the word of Jehovah, all Judah who are in the land of Egypt:
25 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel, saying, Ye and your wives have both spoken with your mouths, and with your hands have fulfilled it, saying, We will surely perform our vows that we have vowed, to burn incense to the queen of heaven, and to pour out drink offerings to her. Establish then your vows, and perform your vows.
26 Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
Therefore hear ye the word of Jehovah, all Judah who dwell in the land of Egypt: Behold, I have sworn by my great name, says Jehovah, that my name shall no more be named in the mouth of any man of Judah in all the land of Egypt, saying, As the lord Jehovah lives.
27 Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
Behold, I watch over them for evil, and not for good. And all the men of Judah who are in the land of Egypt shall be consumed by the sword and by the famine, until there is an end of them.
28 Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
And those who escape the sword shall return out of the land of Egypt into the land of Judah, few in number. And all the remnant of Judah, who have gone into the land of Egypt to sojourn there, shall know whose word shall stand, mine, or theirs.
29 “Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
And this shall be the sign to you, says Jehovah, that I will punish you in this place, that ye may know that my words shall surely stand against you for evil:
30 Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”
Thus says Jehovah: Behold, I will give Pharaoh Hophra king of Egypt into the hand of his enemies, and into the hand of those who seek his life, as I gave Zedekiah king of Judah into the hand of Nebuchadrezzar king of Babylon, who was his enemy, and sought his life.

< Yeremiya 44 >