< Yeremiya 43 >

1 Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze,
and to be like/as to end: finish Jeremiah to/for to speak: speak to(wards) all [the] people [obj] all word LORD God their which to send: depart him LORD God their to(wards) them [obj] all [the] word [the] these
2 Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’
and to say Azariah son: child Hoshaiah and Johanan son: child Kareah and all [the] human [the] arrogant to say to(wards) Jeremiah deception you(m. s.) to speak: speak not to send: depart you LORD God our to/for to say not to come (in): come Egypt to/for to sojourn there
3 Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”
for Baruch son: child Neriah to incite [obj] you in/on/with us because to give: give [obj] us in/on/with hand: power [the] Chaldea to/for to die [obj] us and to/for to reveal: remove [obj] us Babylon
4 Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda.
and not to hear: obey Johanan son: child Kareah and all ruler [the] strength: soldiers and all [the] people in/on/with voice LORD to/for to dwell in/on/with land: country/planet Judah
5 Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako.
and to take: take Johanan son: child Kareah and all ruler [the] strength: soldiers [obj] all remnant Judah which to return: return from all [the] nation which to banish there to/for to sojourn in/on/with land: country/planet Judah
6 Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
[obj] [the] great man and [obj] [the] woman and [obj] [the] child and [obj] daughter [the] king and [obj] all [the] soul: person which to rest Nebuzaradan chief guard with Gedaliah son: child Ahikam son: child Shaphan and [obj] Jeremiah [the] prophet and [obj] Baruch son: child Neriah
7 Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.
and to come (in): come land: country/planet Egypt for not to hear: obey in/on/with voice LORD and to come (in): come till Tahpanhes
8 Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti,
and to be word LORD to(wards) Jeremiah in/on/with Tahpanhes to/for to say
9 “Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona.
to take: take in/on/with hand your stone great: large and to hide them in/on/with mortar in/on/with brick which in/on/with entrance house: palace Pharaoh in/on/with Tahpanhes to/for eye: seeing human Jew
10 Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi.
and to say to(wards) them thus to say LORD Hosts God Israel look! I to send: depart and to take: take [obj] Nebuchadnezzar king Babylon servant/slave my and to set: make throne his from above to/for stone [the] these which to hide and to stretch [obj] (pavilion his *Q(K)*) upon them
11 Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
(and to come (in): come *Q(K)*) and to smite [obj] land: country/planet Egypt which to/for death to/for death and which to/for captivity to/for captivity and which to/for sword to/for sword
12 Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere.
and to kindle fire in/on/with house: temple God Egypt and to burn them and to take captive them and to enwrap [obj] land: country/planet Egypt like/as as which to enwrap [the] to pasture [obj] garment his and to come out: come from there in/on/with peace
13 Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’”
and to break [obj] pillar Heliopolis Heliopolis which in/on/with land: country/planet Egypt and [obj] house: temple God Egypt to burn in/on/with fire

< Yeremiya 43 >