< Yeremiya 42 >
1 Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
І підійшли всі військо́ві зверхники та Йоаханан, син Кареахів, і Єзанія, син Гошаїн, та ввесь наро́д від мало́го й аж до великого,
2 kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
та й сказали до пророка Єремії: „Нехай упаде́ наше блага́ння перед обличчя твоє, і молися за нас до Господа, Бога твого, за всю оцю решту, бо залиши́лося нас мало з багатьо́х, як бачать твої очі нас.
3 Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
І нехай виявить нам Господь, Бог твій, ту дорогу, якою ми пі́демо, та те ді́ло, яке ми зро́бимо“.
4 Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
І промовив до них пророк Єремія: „Чую я! Ось я помолюся до Господа, вашого Бога, за вашими словами. І станеться, кожне слово, що Господь відповість вам, звіщу́ вам, — нічого не затаю́ від вас“.
5 Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
А вони сказали до Єремії: „Нехай буде Господь проти нас за свідка правдивого та вірного, якщо ми не зробимо так, як усе те, з чим пошле тебе до нас Господь, Бог твій.
6 Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
Чи добре й чи зле, ми послухаємося голосу Господа, Бога нашого, що до Нього ми посилаємо тебе, щоб було нам добре, коли бу́демо слухатися голосу Господа, Бога нашого“.
7 Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
І сталося з кінце́м десятьох днів, і було Господнє слово до Єремії.
8 Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
І він покликав Йоханана, сина Кареахового, і всіх військо́вих зверхииків, що були з ним, та ввесь наро́д від малого й аж до великого,
9 Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
та й сказав до них: „Так говорить Господь, Бог Ізраїлів, що ви послали мене до Нього скласти ваше блага́ння перед Його лице:
10 “Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
Якщо ви бу́дете сидіти в цьому кра́ї, то збудую вас, а не розіб'ю́, і засаджу́ вас, а не вирву, бо пожалував Я щодо того зла, що зробив був вам.
11 Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
Не бійте́ся вавилонського царя, якого ви боїтеся, не бійтеся його, — говорить Господь, — бо з вами Я, щоб вас спасати, і щоб вас рятувати від його руки!
12 Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
І дам Я вам милість, і змилуюся над вами, і він ве́рне вас до вашої землі.
13 “Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
А якщо ви скажете: „Не бу́демо сидіти в цьому кра́ї“, щоб не слухатися голосу Господа, Бога вашого,
14 ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
кажучи: „Ні, ми пі́демо до єгипетського кра́ю, де не побачимо війни, і не почуємо звуку сурми́, і на хліб не бу́демо голодні, і там бу́демо сидіти“,
15 Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
то тому́ послухайте тепер Господнього слова, решто Юдина! Так говорить Господь Саваот, Бог Ізраїлів: Якщо ви справді скеру́єте своє обличчя, щоб іти до Єгипту, і вві́йдете, щоб чужи́нцями заме́шкати там,
16 ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
то станеться: той меч, що ви боїте́ся його, досягне вас там, ув єгипетськім кра́ї, а голод, якого ви лякаєтесь, пристане до вас в Єгипті, — і там ви повмираєте...
17 Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
І станеться, всі люди, що звернули своє обличчя на мандрівку до Єгипту, щоб чужинцями замешкати там, повмирають від меча, від голоду та від морови́ці, і жоден з них не позоста́неться й не втече через те зло, що Я спрова́джу на них.
18 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
Бо так каже Господь, Саваот, Бог Ізраїлів: Як вилився гнів Мій та лютість Моя на ме́шканців Єрусалиму, так виллється лютість Моя на вас, коли ви при́йдете до Єгипту, і будете там на клятьбу́, і на застра́шення, і на прокля́ття, і на га́ньбу, і ви вже не побачите цього місця.
19 “Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
Господь говорить до вас, Юдина решто: Не ходіть до Єгипту! Добре знайте, що сьогодні Я вас остеріг!
20 kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
Бо ви зблуди́лися в душах своїх, що послали мене до Господа, вашого Бога, говорячи: „Молися за нас до Господа, Бога нашого, і все, що скаже Господь, Бог наш, так перекажи нам, — і ми зробимо“.
21 Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
І переказав я вам сьогодні, та не послухалися ви голосу Господа, Бога вашого, та всього того, з чим послав Він мене до вас.
22 Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”
А тепер знайте напевно, що повмираєте від меча, голоду та від зарази в тому місці, куди хочете йти, щоб жити там чужи́нцями“.