< Yeremiya 42 >

1 Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
Zasezisondela zonke induna zamabutho, loJohanani indodana kaKareya, loJezaniya indodana kaHoshaya, labo bonke abantu, kusukela komncinyane kuze kube komkhulu,
2 kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
bathi kuJeremiya umprofethi: Ake kuthi ukuncenga kwethu kuwe phambi kwakho, usikhulekele eNkosini uNkulunkulu wakho, umele le insali yonke, ngoba sisele sibalutshwana kwabanengi, njengalokho amehlo akho esibona;
3 Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
ukuze iNkosi, uNkulunkulu wakho, isazise indlela esizahamba ngayo, lento esizayenza.
4 Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
UJeremiya umprofethi wasesithi kibo: Sengizwile; khangelani, ngizakhuleka eNkosini uNkulunkulu wenu njengokwamazwi enu; kuzakuthi-ke, lonke ilizwi iNkosi ezaliphendula ngizalitshela lona, kangiyikuligodlela lizwi.
5 Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
Bona basebesithi kuJeremiya: INkosi kayibe ngumfakazi oqinisileyo lothembekileyo phakathi kwethu, uba singenzi ngokunjalo njengalo lonke ilizwi iNkosi uNkulunkulu wakho ekuthuma kithi ngalo.
6 Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
Loba kukuhle loba kukubi, sizalalela ilizwi leNkosi uNkulunkulu wethu, esikuthuma kuyo, ukuze kusilungele lapho sililalela ilizwi leNkosi uNkulunkulu wethu.
7 Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
Kwasekusithi ekupheleni kwensuku ezilitshumi, ilizwi leNkosi lafika kuJeremiya.
8 Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
Wasebiza uJohanani indodana kaKareya, lazo zonke induna zamabutho ezazilaye, labantu bonke kusukela komncinyane kusiya komkhulu;
9 Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
wathi kibo: Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, elingithume kiyo ukuthi ngenze ukuncenga kwenu kuwe phambi kwayo:
10 “Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
Uba lihlala lokuhlala kulelilizwe, ngizalakha ngingalidilizi, ngilihlanyele, ngingalisiphuni; ngoba ngiyazisola ngokubi engikwenzileyo kini.
11 Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
Lingayesabi inkosi yeBhabhiloni eliyesabayo, lingayesabi, itsho iNkosi; ngoba mina ngilani ukuze ngilisindise ngilophule esandleni sayo.
12 Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
Ngilinike izihawu, ukuze ibe lomusa kini, ilibuyisele elizweni lakini.
13 “Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
Kodwa uba lisithi: Kasiyikuhlala kulelilizwe; ukuthi lingalaleli ilizwi leNkosi uNkulunkulu wenu;
14 ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
lisithi: Hatshi; kodwa sizangena elizweni leGibhithe, lapho esingayikubona impi khona, singayikuzwa ukukhala kophondo, singalambelanga isinkwa, sihlale khona;
15 Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
khathesi-ke, ngakho zwanini ilizwi leNkosi, nsali yakoJuda: Itsho njalo iNkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Uba lina libeka ubuso benu ngokupheleleyo ukuya eGibhithe, lingene ukuyahlala njengabezizwe khona,
16 ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
kuzakuthi-ke inkemba eliyesabayo izalifica khona elizweni leGibhithe, lendlala elinqineka ngayo izanamathela emva kwenu khona eGibhithe, lifele khona.
17 Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
Bazakuba njalo bonke abantu ababeka ubuso babo ukuya eGibhithe, ukuze bahlale njengabezizwe khona; bazakufa ngenkemba, ngendlala, langomatshayabhuqe wesifo; njalo kabayikuba lensali kumbe ophunyuke phambi kokubi engizabehlisela khona.
18 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
Ngoba itsho njalo iNkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Njengokuthululwa kolaka lwami lentukuthelo yami phezu kwabahlali beJerusalema, ngokunjalo intukuthelo yami izathululelwa phezu kwenu, nxa lingena eGibhithe. Njalo lizakuba yisithuko lokwesabekayo lesiqalekiso lehlazo, lingaphindi liyibone lindawo.
19 “Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
INkosi ithe ngani, nsali yakoJuda: Lingangeni eGibhithe. Yazini isibili ukuthi lamuhla ngifakazile ngimelene lani.
20 kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
Ngoba liyikhohlisile imiphefumulo yenu; ngoba lina lingithume eNkosini, uNkulunkulu wenu, lisithi: Sikhulekele eNkosini uNkulunkulu wethu; lanjengakho konke iNkosi uNkulunkulu wethu ekutshoyo, ngokunjalo sitshele, sikwenze.
21 Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
Sengilitshelile lamuhla, kodwa kalililalelanga ilizwi leNkosi uNkulunkulu wenu, laloba yiyiphi into engithume yona kini.
22 Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”
Khathesi-ke yazini isibili ukuthi lizakufa ngenkemba, ngendlala, langomatshayabhuqe wesifo, endaweni eliloyisa ukuyahlala khona njengabezizwe.

< Yeremiya 42 >