< Yeremiya 42 >

1 Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
Zonke izikhulu zebutho, kanye loJohanani indodana kaKhareya loJezaniya indodana kaHoshayiya, labantu bonke kusukela komncane kusiya komkhulu baya
2 kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
kuJeremiya umphrofethi bathi kuye, “Ake uzwe isicelo sethu ubakhulekele bonke laba abaseleyo kuThixo uNkulunkulu wakho. Ngoba njengoba lawe uzibonela khathesi, lanxa sake saba banengi khathesi kusele abalutshwana kuphela.
3 Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
Khuleka ukuba uThixo uNkulunkulu wakho asitshele lapho okumele siye khona lalokho okumele sikwenze.”
4 Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
UJeremiya umphrofethi waphendula wathi, “Ngizwile. Ngizakhuleka impela kuThixo uNkulunkulu wenu njengoba licelile; ngizalitshela konke uThixo akutshoyo ngingalifihleli lutho.”
5 Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
Basebesithi kuJeremiya, “UThixo kabe ngufakazi wethu oqotho lothembekileyo nxa singenzi okuvumelana lakho konke uThixo uNkulunkulu wakho akuthuma ukuba usitshele khona.
6 Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
Lanxa kukuhle kumbe kukubi sizamlalela uThixo uNkulunkulu wethu esikuthuma kuye, ukuze kusilungele, ngoba sizamlalela uThixo uNkulunkulu wethu.”
7 Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
Emva kwensuku ezilitshumi ilizwi likaThixo lafika kuJeremiya.
8 Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
Ngakho wabiza uJohanani indodana kaKhareya lezikhulu zonke zebutho ezazilaye kanye labantu bonke kusukela komncane kusiya komkhulu.
9 Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
Wathi kubo, “UThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, elingithume ukuba ngiyekwethula isicelo senu kuye, uthi:
10 “Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
‘Lingahlala kulelilizwe ngizalakha, ngingalibhidlizi, ngizalihlanyela ngingalisiphuni, ngoba ngilusizi ngomonakalo engawenza kini.
11 Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
Lingayesabi inkosi yaseBhabhiloni, eliyesabayo khathesi. Lingayesabi, kutsho uThixo, ngoba ngilani njalo ngizalihlenga ngilikhulule ezandleni zayo.
12 Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
Ngizakuba lesihawu kini ukuze layo ibe lesihawu kini ilibuyisele elizweni lakini.’
13 “Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
Kodwa lina lingathi, ‘Kasiyikuhlala kulelizwe,’ ngalokho lingalaleli uThixo uNkulunkulu wenu,
14 ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
njalo nxa lisithi, ‘Hatshi, thina sizakuyahlala eGibhithe lapho esingayikubona khona impi loba sizwe icilongo kumbe silambele ukudla,
15 Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
zwanini-ke ilizwi likaThixo, lina abasele koJuda.’ UThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli uthi: ‘Nxa liphitshekela ukuya eGibhithe njalo lihambe ukuyahlala khona,
16 ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
lapho-ke inkemba eliyesabayo izalifica khona, lendlala eliyesabayo izalilandela eGibhithe, njalo lizafela khonale.
17 Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
Ngempela bonke abaphitshekela ukuya eGibhithe ukuba bahlale khona bazakufa ngenkemba, indlala lesifo; kakho lamunye wabo ozasinda loba aphephe kumonakalo engizabehlisela wona.’
18 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
UThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli, uthi, ‘Njengalokhu ukuthukuthela kwami lolaka lwami kwehliselwa phezu kwabantu abahlala eJerusalema, ngokunjalo ulaka lwami luzakwehliselwa phezu kwenu lapho lisiya eGibhithe. Lizakuba yinto yokuthukwa lokwesatshwa, ukulahlwa lokuhlekwa; indawo le kaliyikuyibona futhi.’
19 “Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
Lina abasele koJuda, uThixo ulitshelile wathi, ‘Lingayi eGibhithe.’ Wobani leqiniso lalokhu ukuthi: Ngiyalixwayisa lamuhla
20 kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
ukuthi lenza iphutha elikhulu kakhulu ngokungithuma kuThixo uNkulunkulu wenu lisithi, ‘Sikhulekele kuThixo uNkulunkulu wethu; usitshele konke akutshoyo sizakwenza.’
21 Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
Sengilitshelile lamuhla, kodwa lilokhu lingalaleli lokho uThixo uNkulunkulu wenu angithume ukuthi ngilitshele khona.
22 Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”
Ngakho khathesi wobani leqiniso ukuthi lizakufa ngenkemba, indlala lesifo endaweni elifuna ukuyahlala kuyo.”

< Yeremiya 42 >