< Yeremiya 42 >

1 Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
Alors tous les chefs des troupes, Jochanan, fils de Karéach, Jézania, fils d'Hoshaïa, et tout le peuple, depuis le plus petit jusqu'au plus grand, s'approchèrent,
2 kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
et dirent à Jérémie, le prophète: « Laisse, je te prie, notre supplication être présentée devant toi, et prie pour nous Yahvé ton Dieu, même pour tout ce reste, car nous ne sommes plus qu'un petit nombre parmi beaucoup, comme tes yeux le voient,
3 Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
afin que Yahvé ton Dieu nous montre le chemin que nous devons suivre et les choses que nous devons faire. »
4 Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
Alors Jérémie, le prophète, leur dit: « Je vous ai entendus. Voici, je vais prier Yahvé votre Dieu selon vos paroles, et il arrivera que tout ce que Yahvé vous répondra, je vous l'annoncerai. Je ne vous cacherai rien. »
5 Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
Et ils dirent à Jérémie: « Que Yahvé soit au milieu de nous un témoin vrai et fidèle, si nous n'agissons pas selon toute la parole que Yahvé, ton Dieu, t'envoie nous dire.
6 Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
Qu'elle soit bonne ou qu'elle soit mauvaise, nous obéirons à la voix de l'Éternel, notre Dieu, vers qui nous t'envoyons, afin que tout aille bien pour nous, quand nous obéissons à la voix de l'Éternel, notre Dieu. »
7 Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
Dix jours après, la parole de Yahvé fut adressée à Jérémie.
8 Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
Il appela Johanan, fils de Karéa, tous les chefs de troupes qui étaient avec lui, et tout le peuple, depuis le plus petit jusqu'au plus grand,
9 Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
et leur dit: « Yahvé, le Dieu d'Israël, à qui tu m'as envoyé présenter tes supplications devant lui, dit:
10 “Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
Si vous vivez encore dans ce pays, je vous bâtirai et ne vous abattrai pas, je vous planterai et ne vous arracherai pas, car je m'afflige de la détresse que je vous ai causée.
11 Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
Ne craignez pas le roi de Babylone, dont vous avez peur. N'aie pas peur de lui, dit Yahvé, car je suis avec toi pour te sauver et te délivrer de sa main.
12 Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
Je te ferai grâce, afin qu'il ait pitié de toi et que tu retournes dans ton pays.
13 “Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
« Mais si vous dites: Nous n'habiterons pas dans ce pays, et que vous n'obéissez pas à la voix de Yahvé votre Dieu,
14 ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
en disant: Non, mais nous irons au pays d'Égypte, où nous ne verrons pas la guerre, où nous n'entendrons pas le son de la trompette, où nous n'aurons pas faim de pain, et c'est là que nous habiterons »
15 Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
écoutez donc la parole de Yahvé, reste de Juda! Yahvé des armées, le Dieu d'Israël, dit: « Si vous vous décidez à entrer en Égypte et à y vivre,
16 ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
l'épée que vous craignez vous atteindra dans le pays d'Égypte, et la famine que vous redoutez vous suivra de près dans ce pays, et vous y mourrez.
17 Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
Il en sera de même pour tous les hommes qui auront pris le parti d'entrer en Égypte pour y vivre. Ils mourront par l'épée, par la famine et par la peste. Aucun d'eux ne restera ou n'échappera au malheur que je ferai venir sur eux'.
18 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
Car Yahvé des armées, le Dieu d'Israël, dit: « De même que ma colère et ma fureur se sont déversées sur les habitants de Jérusalem, de même ma fureur se déversera sur vous, quand vous entrerez en Égypte; vous serez un objet d'horreur, d'étonnement, de malédiction et d'opprobre, et vous ne verrez plus ce lieu.
19 “Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
« Yahvé a parlé à votre sujet, reste de Juda: « N'allez pas en Égypte! ». Sachez bien que je vous ai rendu aujourd'hui ce témoignage.
20 kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
Car vous avez agi de façon trompeuse contre vos propres âmes; vous m'avez envoyé vers l'Éternel, votre Dieu, en disant: Priez pour nous l'Éternel, notre Dieu; et, selon tout ce que dit l'Éternel, notre Dieu, déclarez-le-nous, et nous le ferons.
21 Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
Je vous l'ai annoncé aujourd'hui, mais vous n'avez pas écouté la voix de l'Éternel, votre Dieu, dans tout ce pour quoi il m'a envoyé vers vous.
22 Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”
Maintenant, sachez donc avec certitude que vous mourrez par l'épée, par la famine et par la peste dans le lieu où vous voulez aller vivre. »

< Yeremiya 42 >