< Yeremiya 41 >

1 Pa mwezi wachisanu ndi chiwiri Ismaeli mwana wa Netaniya, mdzukulu wa Elisama amene anali wa banja laufumu ndiponso mmodzi wa atsogoleri a ankhondo a mfumu, anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ndi anthu khumi. Pamene ankadya naye kumeneko,
And it happened that, in the seventh month, Ishmael, the son of Nethaniah, the son of Elishama of royal descent, with the nobles of the king, and accompanied by ten men, went to Gedaliah, the son of Ahikam, at Mizpah. And they ate bread together there, in Mizpah.
2 Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu khumi aja anayimirira ndi kupha ndi lupanga Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani. Choncho anapha munthu amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.
Then Ishmael, the son of Nethaniah, rose up, and the ten men who were with him, and they struck down Gedaliah, the son of Ahikam, the son of Shaphan, with the sword, and they killed him whom the king of Babylon had made governor over the land.
3 Ismaeli anaphanso Ayuda onse amene anali pamodzi ndi Gedaliya ku Mizipa, kuphatikizanso asilikali a Ababuloni amene anali ku Mizipako.
Likewise, Ishmael struck down all the Jews who were with Gedaliah at Mizpah, with the Chaldeans who were found there, and the men of war.
4 Mmawa mwake, anthu asanadziwe kuti Gedaliya waphedwa,
Then, on the second day after he had killed Gedaliah, while no one yet knew of it,
5 kunafika anthu 80 ochekera ku Sekemu, Silo ndi Samariya, amene anali atameta ndevu zawo, atangʼamba zovala zawo ndi kudzichekacheka. Iwowa anatenga chopereka cha ufa ndi lubani kuti adzapereke ku Nyumba ya Yehova.
men arrived from Shechem, and from Shiloh, and from Samaria, eighty men, with their beards shaved, and their garments rent, and unbathed. And they had gifts and frankincense in hand, so that they might make an offering in the house of the Lord.
6 Ismaeli mwana wa Netaniya anachoka ku Mizipa akulira kupita kukakumana nawo. Atakumana nawo, iye anati, “Bwerani mudzaonane ndi Gedaliya mwana wa Ahikamu.”
Therefore, Ishmael, the son of Nethaniah, departing from Mizpah to meet them, went forth weeping as he was walking. And when he had met them, he said to them, “Come to Gedaliah, the son of Ahikam.”
7 Atafika pakati pa mzinda, Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu amene anali naye anawapha anthuwo ndi kuwaponya mʼchitsime.
And when they had arrived at the center of the city, Ishmael, the son of Nethaniah, put them to death around the public cistern, he and the men who were with him.
8 Koma anthu khumi a gululo anawuza Ismaeli kuti, “Musatiphe! Tili ndi tirigu ndi barele, mafuta ndi uchi, zimene tabisa mʼmunda.” Choncho anawasiya ndipo sanawaphere pamodzi ndi anzawo aja.
But ten men were found among them, who said to Ishmael: “Do not kill us! For in the field we have storehouses of grain and barley and oil and honey.” And so he ceased, and he did not put them to death with their brothers.
9 Tsono chitsime chimene anaponyamo mitembo ya anthu amene anawaphawo pamodzi ndi mtembo wa Gedaliya chinali chimene mfumu Asa anachikumba poopsedwa ndi Baasa mfumu ya Israeli. Ismaeli mwana wa Netaliya anachidzaza ndi mitembo.
Now the cistern, into which Ishmael cast all the dead bodies of the men whom he had struck down because of Gedaliah, is the same one that king Asa made out of fear of Baasha, the king of Israel. This same cistern Ishmael, the son of Nethaniah, filled with those who were slain.
10 Pambuyo pake Ismaeli anatenga ukapolo anthu ena onse amene anali ku Mizipa: ana aakazi a mfumu pamodzi ndi ena onse amene anatsalira kumeneko, amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anapatsa Gedaliya mwana wa Ahikamu kuti akhale bwanamkubwa wawo. Ismaeli mwana wa Netaliya anatenga ukapolo anthuwa ndi kuwoloka nawo kumapita ku dziko la Aamoni.
Then Ishmael led away captive all the remnant of the people who were at Mizpah, the king’s daughters as well as all the people who remained at Mizpah, whom Nebuzaradan, the leader of the military, had committed to Gedaliah, the son of Ahikam. And Ishmael, the son of Nethaniah, seized them and went away, so that he might go over to the sons of Ammon.
11 Pamene Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye pamodzi anamva zoyipa zonse zimene Ismaeli mwana wa Netaniya anachita,
But Johanan, the son of Kareah, and all the leaders of the fighters who were with him, heard about all the evil that Ishmael, the son of Nethaniah, had done.
12 anatenga ankhondo awo onse kupita kukamenyana ndi Ismaeli mwana wa Netaniya. Anakamupeza kufupi ndi chidziwe chachikulu cha ku Gibiyoni.
And taking all the men, they set out to make war against Ishmael, the son of Nethaniah. And they found him at the great waters that are in Gibeon.
13 Pamene anthu onse amene Ismaeli anawagwira anaona Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali naye, anasangalala.
And when all the people who were with Ishmael had seen Johanan, the son of Kareah, and all the leaders of the fighters who were with him, they rejoiced.
14 Anthu onse amene Ismaeli anawagwira ukapolo ku Mizipa anabwerera ndi kupita kwa Yohanani mwana wa Kareya.
And all the people whom Ishmael had seized turned back to Mizpah. And they returned and went over to Johanan, the son of Kareah.
15 Koma Ismaeli pamodzi ndi anthu ake asanu ndi atatu, anathawa Yohanani ndi kuthawira kwa Aamoni.
But Ishmael, the son of Nethaniah, fled with eight men from the face of Johanan, and they went over to the sons of Ammon.
16 Kenaka Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye anatsogolera anthu onse otsala a ku Mizipa amene anawapulumutsa kwa Ismaeli mwana wa Netaniya atapha Gedaliya mwana wa Ahikamu. Anthu amenewa anali: asilikali, akazi, ana ndi amuna ofulidwa otumikira mfumu amene anawatenga ku Gibiyoni.
Therefore, Johanan, the son of Kareah, and all the leaders of the fighters who were with him, took from Mizpah the entire remnant of the common people, whom they had led away from Ishmael, the son of Nethaniah, after he had struck down Gedaliah, the son of Ahikam. These were strong men of battle, and women, and children, and eunuchs: those whom he had led away from Gibeon.
17 Ndipo ananyamuka nayima ku Geruti Kimuhamu pafupi ndi Betelehemu pa ulendo wawo wopita ku Igupto
And they went away and settled as sojourners at Chimham, which is near Bethlehem, so that they might continue on and enter into Egypt,
18 kuthawa Ababuloni. Iwo anaopa Ababuloniwo chifukwa Ismaeli mwana wa Netaniya anapha Gedaliya mwana wa Ahikamu, amene mfumu ya ku Babuloni inamuyika kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.
away from the face of the Chaldeans. For they were afraid of them, because Ishmael, the son of Nethaniah, had struck down Gedaliah, the son of Ahikam, whom the king of Babylon had made governor in the land of Judah.

< Yeremiya 41 >