< Yeremiya 40 >
1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya pamene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anamasula Yeremiyayo ku Rama. Anamupeza Yeremiya ali womangidwa ndi unyolo pamodzi ndi amʼndende ena onse a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene ankapita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Det Ord, som kom fra HERREN til Jeremias, efter at Livvagtsøversten Nebuzar'adan havde løsladt ham i Rama; han lod ham hente, medens han var bundet med Lænker iblandt alle Fangerne fra Jerusalem og Juda, der førtes til Babel.
2 Mtsogoleriyu anamupeza Yeremiya, anamuwuza kuti, “Yehova Mulungu wako analengeza kale zakuti malo ano adzawonongedwa.
Livvagtsøversten lod Jeremias hente og sagde til ham: »HERREN din Gud har udtalt denne Ulykke over dette Sted,
3 Ndipo tsopano Yehova wachitadi zimenezi monga mmene ananenera. Izi zonse zachitika chifukwa anthu inu munachimwira Yehova ndipo simunamumvere.
og HERREN lod det ske og gjorde, hvad han havde sagt, fordi I syndede mod HERREN og ikke adlød hans Røst; derfor timedes dette eder.
4 Koma tsopano taona, lero ndikukumasula unyolo umene unali mʼmanja mwako. Ngati ukufuna kupita nane ku Babuloni, tiye ndipo adzakusamala bwino. Koma ngati sukufuna kupita, ndiye usapite. Dziko ndi limeneli monga ukulioneramo. Uli ndi ufulu kupita kulikonse kumene ukufuna.”
Se, nu tager jeg i Dag Lænkerne af dine Hænder. Hvis det tykkes dig godt at drage med mig til Babel, saa drag med, og jeg vil have Øje med dig; men tykkes det dig ilde, saa lad være! Se, hele Landet staar dig aabent; gaa, hvor det tykkes dig godt og ret!«
5 Yeremiya asanayankhe, Nebuzaradani anamuwuzanso kuti, “Ngati supita ndiye pita, ubwerere kwa Gedaliya, mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kuti akhale bwanamkubwa wa Yuda. Ukakhale naye pakati pa anthu, kapena upite kulikonse ukufuna.” Ndipo mtsogoleri uja anamupatsa Yeremiya chakudya ndi mphatso zina ndi kumulola kuti apite.
Og da han tøvede med at vende tilbage, tilføjede han: »Saa vend tilbage til Gedalja, Sjafans Søn Ahikams Søn, som Babels Konge har sat over Judas Land, og bosæt dig hos ham iblandt Folket, eller gaa, hvor som helst det tykkes dig ret!« Og Livvagtsøversten gav ham Rejsetæring og Gave og lod ham gaa.
6 Motero Yeremiya anapita kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ku Mizipa ndipo anakakhala naye kumeneko pakati pa anthu amene anatsala mʼdzikomo.
Jeremias gik da til Gedalja, Ahikams Søn, i Mizpa og bosatte sig hos ham iblandt Folket, der var levnet i Landet.
7 Panali atsogoleri ena a nkhondo ndi anthu awo amene sanadzipereke nawo. Iwowa anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu kukhala bwanamkubwa wa dzikolo ndipo kuti yamuyika kukhala wolamulira amuna, akazi ndi ana amene anali osauka kwambiri mʼdzikomo, amene sanawagwire ukapolo kupita nawo ku Babuloni.
Da alle Hærførerne, som var ude i aabent Land, og deres Mænd hørte, at Babels Konge havde sat Gedalja, Ahikams Søn, over Landet og over Mænd, Kvinder og Børn og dem af den fattige Befolkning i Landet, som ikke var ført til Babel,
8 Iwowa anapita ku Mizipa kwa Gedaliya. Amene anapitawo ndi awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani ndi Yonatani ana a Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti, ana a Efai a ku Netofa, ndi Yezaniya mwana wa Maaka, iwowo pamodzi ndi anthu awo.
kom de til Gedalja i Mizpa: Jisjmael Netanjas Søn, Johanan Kareas Søn, Seraja Tanhumets Søn, Netofatiten Efajs Sønner og Jezanja Ma'akatitens Søn, med deres Mænd.
9 Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, anawalonjeza iwo pamodzi ndi anthuwo mwalumbiro. Ndipo anati, “Musaope kuwatumikira Ababuloni. Khalani mʼdziko muno, tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
Og Gedalja, Sjafans Søn Ahikams Søn, tilsvor dem og deres Mænd saaledes: »Frygt ikke for at staa under Kaldæerne; bosæt eder i Landet og underkast eder Babels Konge, saa skal det gaa eder vel.
10 Ine ndidzakhala ku Mizipa kuti ndizikuyimirirani kwa Ababuloni amene azidzabwera kwa ife, koma inu muzikolola vinyo wanu, zipatso zanu, mafuta anu ndi kuzisunga mʼmitsuko yanu, nʼkumakhala mʼmizinda imene mwalandayo.”
Se, selv bliver jeg i Mizpa for at tage mod Kaldæerne, naar de kommer til os; men I skal samle Vin, Frugt og Olie i eders Kar og bo i de Byer, I tager i Eje!«
11 Nawonso Ayuda onse a ku Mowabu, ku Amoni, ku Edomu ndi a ku mayiko ena onse anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasiyako anthu ena ku Yuda ndipo kuti inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala bwanamkubwa wawo.
Og da ogsaa alle de Judæere, der var i Moab, hos Ammoniterne, i Edom og alle de andre Lande, hørte, at Babels Konge havde levnet Juda en Rest og sat Gedalja, Sjafans Søn Ahikams Søn, over dem,
12 Tsono Ayuda onsewo anabwerera ku Yuda, ku Mizipa kwa Gedaliya, kuchokera ku mayiko onse kumene anabalalikira. Ndipo anakolola zipatso zochuluka ndi vinyo wambiri.
vendte de alle tilbage fra alle de Steder, som de var fordrevet til, og kom til Judas Land til Gedalja i Mizpa; og de indsamlede Vin og Frugt i store Maader.
13 Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri a ankhondo onse amene sanadzipereke aja anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya
Men Johanan, Kareas Søn, og alle de andre Hærførere, som havde været ude i aabent Land, kom til Gedalja i Mizpa
14 ndipo anamufunsa kuti, “Kodi sukudziwa kuti Baalisi mfumu ya Aamoni watuma Ismaeli mwana wa Netaniya kuti akuphe?” Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu sanawankhulupirire.
og sagde: »Mon du ved, at Ba'alis, Ammoniternes Konge, har sendt Jisjmael, Netanjas Søn, for at myrde dig?« Men Gedalja, Ahikams Søn, troede dem ikke.
15 Tsono Yohanani mwana wa Kareya, mwamseri anawuza Gedaliya ku Mizipa kuti, “Loleni ndipite ndikaphe Ismaeli mwana wa Netaniya, ndipo palibe amene ati adziwe. Akuphereninji ndi kuchititsa Ayuda onse, amene akuzungulirani kuti abalalike ndi kuti otsala a ku Yuda awonongeke?”
Da sagde Johanan, Kareas Søn, i al Hemmelighed til Gedalja I Mizpa: »Lad mig gaa hen og myrde Jisjmael, Netanjas Søn; ingen skal faa det at vide. Hvorfor skal han myrde dig, saa at hele Juda, som har samlet sig om dig, splittes, og Judas Rest gaar til Grunde?«
16 Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu anawuza Yohanani mwana wa Kareya kuti, “Usachite zimenezo! Zimene ukunena za Ismaeli ndi zabodza.”
Men Gedalja, Ahikams Søn, svarede Johanan, Kareas Søn: »Det maa du ikke gøre, thi du lyver om Jisjmael!«