< Yeremiya 4 >

1 “Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli, bwererani kwa Ine,” akutero Yehova. “Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga ndipo musasocherenso.
“Sɛ wo, Israel, wobɛsan wʼakyi a, san bra me nkyɛn,” sɛɛ na Awurade se. “Sɛ wuyi wʼahoni a ɛyɛ akyiwade fi mʼani so na sɛ woamman bio,
2 Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’ Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse ndipo adzanditamanda.”
na sɛ wufi nokware, pɛpɛyɛ ne trenee mu ka ntam se, ‘Sɛ Awurade te ase yi,’ a afei wobehyira aman no na ne mu na wobenya anuonyam.”
3 Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi: “Limani masala anu musadzale pakati pa minga.
Eyi ne asɛm a, Awurade ka kyerɛ Yuda mmarima ne Yerusalem: “Munsiesie mo asase a womfuntum da, na munnnua wɔ nsɔe mu.
4 Dziperekeni nokha kwa Ine kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse, inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu. Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani, chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo popanda wina wowuzimitsa.
Muntwitwa mo ho twetia mma Awurade muntwitwa mo koma twetia, mo Yuda mmarima ne Yerusalemfo, anyɛ saa a mʼabufuwhyew bɛsɔre na adɛw sɛ ogya mo bɔne a moayɛ nti, ɛbɛhyew a obiara rennum.”
5 “Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti, ‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’ Ndipo fuwulani kuti, ‘Sonkhanani! Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’
“Bɔ nkae wɔ Yuda na pae mu ka wɔ Yerusalem se ‘Hyɛn torobɛnto no wɔ asase no nyinaa so!’ Teɛ mu dennen se: ‘Mommoaboa mo ho ano! Momma yenguan nkɔ nkuropɔn a wɔabɔ ho ban no mu!’
6 Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni! Musachedwe, thawani kuti mupulumuke! Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto, kudzakhala chiwonongeko choopsa.”
Momma frankaa so na monkɔ Sion munguan nkɔbɔ mo ho aguaa! Efisɛ mede amanehunu fi atifi fam reba, ɔsɛe a ɛyɛ hu.”
7 Monga mkango umatulukira mʼngaka yake momwemonso wowononga mayiko wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake. Watero kuti awononge dziko lanu. Mizinda yanu idzakhala mabwinja popanda wokhalamo.
Gyata bi afi ne tu mu; ɔbɔɔaman bi asi mu. Wafi ne tenabea sɛ ɔrebɛsɛe wʼasase. Wo nkurow bebubu na ada mpan.
8 Choncho valani ziguduli, lirani ndi kubuwula, pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova sunatichokere.
Enti fura atweaatam, di awerɛhow na twa adwo, efisɛ Awurade abufuwhyew no nnan mfii yɛn so.
9 “Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima, ansembe adzachita mantha kwambiri, ndipo aneneri adzathedwa nzeru,” akutero Yehova.
“Saa da no,” Awurade na ose, “ɔhene no ne adwumayɛfo no bɛbɔ hu, asɔfo no bo betu, na adiyifo no ho bedwiriw wɔn.”
10 Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”
Afei, mekae se, “Aa, Otumfo Awurade, woadaadaa nnipa yi ne Yerusalem, wokae se, ‘Mubenya asomdwoe,’ wɔ bere a afoa da yɛn mene mu.”
11 Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa;
Saa bere no wɔbɛka akyerɛ nnipa yi ne Yerusalem se, “Mframa a emu yɛ hyew bɛbɔ afi nkoko wosee a ɛwɔ nweatam so aba me nkurɔfo so, ɛnyɛ nea ɛpo ho anaa ehuhuw so;
12 koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”
mframa a ano yɛ den boro saa no fi me nkyɛn. Afei mepae mu ka mʼatemmu a etia wɔn.”
13 Taonani, adani akubwera ngati mitambo, magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu, akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga. Tsoka ilo! Tawonongeka!
Hwɛ! ɔreba sɛ omununkum, ne nteaseɛnam reba sɛ mfɛtɛ, nʼapɔnkɔ ho yɛ hare sen akɔre. Yennue! Yɛawu!
14 Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke. Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?
Yerusalem, yi bɔne fi wo koma mu na woanya nkwa. Wode adwemmɔne bɛhyɛ wo mu akosi da bɛn?
15 Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani; akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.
Nne bi rebɔ amanneɛ fi Dan, ɛrebɔ amanehunu ho dawuru fi Efraim nkoko so.
16 Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina, lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti, ‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali, akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.
“Monka eyi nkyerɛ aman no, mommɔ no dawuru nkyerɛ Yerusalem se, ‘Atuafo dɔm fi akyirikyiri asase bi so reba, wɔma ɔko nteɛmu so de tia Yuda nkuropɔn.
17 Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda, chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’” akutero Yehova.
Wotwa ne ho hyia sɛ mmarima a wɔrewɛn afuw, efisɛ watew me so atua,’” sɛɛ na Awurade se.
18 “Makhalidwe anu ndi zochita zanu zakubweretserani zimenezi. Chimenechi ndiye chilango chanu. Nʼchowawa kwambiri! Nʼcholasa mpaka mu mtima!”
“Wo ankasa abrabɔ ne nneyɛe, na ɛde eyi aba wo so. Eyi yɛ wʼasotwe. Ɛyɛ nwen! Ɛwowɔ koma!”
19 Mayo, mayo, ndikumva kupweteka! Aa, mtima wanga ukupweteka, ukugunda kuti thi, thi, thi. Sindingathe kukhala chete. Pakuti ndamva kulira kwa lipenga; ndamva mfuwu wankhondo.
Ao, mʼahoyeraw, mʼahoyeraw! midi me mu yaw. Me koma mu yawdi! Me koma bɔ kitirikitiri wɔ me mu, mintumi nyɛ komm. Efisɛ, mate torobɛnto no nnyigye; mate ɔko frɛ no.
20 Tsoka limatsata tsoka linzake; dziko lonse lasanduka bwinja. Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa, mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.
Amanehunu di amanehunu akyi; asase no nyinaa asɛe. Wɔasɛe me ntamadan prɛko pɛ, ne me hintabea mpofirim.
21 Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo, ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?
Ɛsɛ sɛ mehwɛ ɔko frankaa no na mitie torobɛnto no nnyigye kosi da bɛn?
22 Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru; iwo sandidziwa. Iwo ndi ana opanda nzeru; samvetsa chilichonse. Ali ndi luso lochita zoyipa, koma sadziwa kuchita zabwino.”
“Me nkurɔfo yɛ nkwaseafo; wonnim me. Wɔyɛ mma a wonni adwene; wɔnte hwee ase. Wɔwɔ bɔneyɛ ho nyansa; na wonnim sɛnea wɔyɛ papa.”
23 Ndinayangʼana dziko lapansi, ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu; ndinayangʼana thambo, koma linalibe kuwala kulikonse.
Mehwɛɛ asase no, na enni bɔbea, na ɛda mpan; mehwɛɛ ɔsorosoro, na wɔn hann no nni hɔ.
24 Ndinayangʼana mapiri, ndipo ankagwedezeka; magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.
Mehwɛɛ mmepɔw no, na wɔrewosowosow, na nkoko no nyinaa rehinhim.
25 Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu; mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.
Mehwɛe, na nnipa nni hɔ; wim anomaa biara atu kɔ.
26 Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu; mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.
Mehwɛe, na nsasebere no adan nweatam na ne nkurow nyinaa asɛe wɔ Awurade anim, wɔ nʼabufuwhyew ano.
27 Yehova akuti, “Dziko lonse lidzasanduka chipululu komabe sindidzaliwononga kotheratu.
Sɛnea Awurade se: “Wɔbɛsɛe asase no nyinaa; mmom, merensɛe no korakora.
28 Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira ndipo thambo lidzachita mdima, pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima, ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”
Enti asase bedi awerɛhow na ɔsorosoro beduru sum, efisɛ makasa na merentwe nsan; masi gyinae na merennan no.”
29 Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi, anthu a mʼmizinda adzathawa. Ena adzabisala ku nkhalango; ena adzakwera mʼmatanthwe mizinda yonse nʼkuyisiya; popanda munthu wokhalamo.
Apɔnkɔsotefo ne agyantowfo nnyigyei ma kurow biara sofo guan. Ebinom kɔhyɛ nkyɛkyerɛ mu, ebinom foro kɔ abotan mu. Nkurow no nyinaa so adeda mpan; na obiara nte so.
30 Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja! Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira ndi kuvalanso zokometsera zagolide? Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera, ukungodzivuta chabe. Zibwenzi zako zikukunyoza; zikufuna kuchotsa moyo wako.
Dɛn na woreyɛ, wo a wɔasɛe wo? Adɛn na wufura ɔkɔben de sikakɔkɔɔ agude asiesie wo ho? Adɛn na wode nnuru keka wʼani? Wohyehyɛ wo ho kwa. Wʼadɔfo bu wo animtiaa; wɔrehwehwɛ wo akum wo.
31 Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka, kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba. Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu. Atambalitsa manja awo nʼkumati, “Kalanga ife! Tikukomoka. Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”
Mete osu bi te sɛ ɔbea a ɔwɔ awoko mu, apinisi te sɛ ɔbea a ɔrewo nʼabakan, Ɔbabea Sion resu te sɛ nea osi apini, ɔtrɛw ne nsa mu na ɔreka se, “Afei de meretɔ piti; wɔde me nkwa ama awudifo.”

< Yeremiya 4 >