< Yeremiya 4 >

1 “Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli, bwererani kwa Ine,” akutero Yehova. “Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga ndipo musasocherenso.
Jeźlibyś się chciał nawrócić, Izraelu! mówi Pan, do mnie się nawróć. Bo jeźli odejmiesz obrzydłości twoje od oblicza mego, a nie będziesz się tułał,
2 Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’ Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse ndipo adzanditamanda.”
I przysiężeszli w prawdzie, w sądzie i w sprawiedliwości, mówiąc: Jako żyje Pan; tedy błogosławić sobie w nim będą narody, i w nim się przechwalać.
3 Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi: “Limani masala anu musadzale pakati pa minga.
Albowiem tak mówi Pan mężom Judzkim i Jeruzalemskim: Poorzcie sobie nowinę, a nie siejcie na cierniu;
4 Dziperekeni nokha kwa Ine kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse, inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu. Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani, chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo popanda wina wowuzimitsa.
Obrzeżcie się Panu, a odejmijcie nieobrzezki serca waszego, mężowie Judzcy, a obywatele Jeruzalemscy! by snać nie wyszła jako ogień popędliwość moja, a nie zapaliła się, a nie byłby, ktoby ugasił dla złości przedsięwzięcia waszego.
5 “Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti, ‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’ Ndipo fuwulani kuti, ‘Sonkhanani! Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’
Opowiadajcie w Judzie, a w Jeruzalemie ogłaszajcie, i mówcie: Zatrąbcie w trąbę w ziemi, zwołajcie, zgromadźcie lud, a mówcie: Zbierzcie się, a wejdźmy do miast obronnych.
6 Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni! Musachedwe, thawani kuti mupulumuke! Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto, kudzakhala chiwonongeko choopsa.”
Podnieście chorągiew na Syonie, bądźcie serca dobrego, nie zastanawiajcie się; bo Ja złe przywiodę od północy, i porażkę wielką.
7 Monga mkango umatulukira mʼngaka yake momwemonso wowononga mayiko wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake. Watero kuti awononge dziko lanu. Mizinda yanu idzakhala mabwinja popanda wokhalamo.
Wychodzi lew z jaskini swojej, a ten, który niszczy narody, wyszedłszy z miejsca swego, ciągnie, aby obrócił ziemię twoję w pustynię, a miasta twoje aby zburzone były, aby nie było żadnego obywatela.
8 Choncho valani ziguduli, lirani ndi kubuwula, pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova sunatichokere.
Przetoż przepaście się worami, narzekajcie a kwilcie, bo nie jest odwrócony gniew zapalczywości Pańskiej od nas.
9 “Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima, ansembe adzachita mantha kwambiri, ndipo aneneri adzathedwa nzeru,” akutero Yehova.
I stanie się dnia onego, mówi Pan, że zginie serce królewskie, i serce książąt, a zdumieją się kapłani, i prorocy dziwować się będą.
10 Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”
I rzekłem: Ach panujący Panie! zaprawdęś bardzo ten lud i Jeruzalem omylił, mówiąc: Pokój mieć będziecie! a wżdy miecz przeniknął aż do duszy.
11 Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa;
Czasu onego rzeką temu ludowi i Jeruzalemowi: Wiatr gwałtowny z miejsc wysokich na puszczy idzie prosto na lud mój, nie żeby przewiewał, ani wyczyszczał.
12 koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”
Wiatr gwałtowniejszy niż oni przyjdzie mi; teraz Ja też opowiem im sądy.
13 Taonani, adani akubwera ngati mitambo, magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu, akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga. Tsoka ilo! Tawonongeka!
Oto występuje jako obłoki, a wozy jego jako wicher, prędsze są niż orły konie jego. Biada nam! bośmy spustoszeni.
14 Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke. Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?
Omyj od złości serce twoje, Jeruzalem! abyś wybawione było. Dokądże trwać będą w pośrodku ciebie myśli nieprawości twojej.
15 Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani; akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.
Bo głos opowiadającego idzie od Danu, a tego, który ogłasza nieprawość, z góry Efraim.
16 Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina, lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti, ‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali, akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.
Przypominajcież tym narodom: Oto ogłaszajcie Jeruzalemczykom, że stróżowie przychodzą z ziemi dalekiej, a wydawają przeciwko miastom Judzkim głos swój.
17 Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda, chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’” akutero Yehova.
Jako stróżowie pól położą się przeciwko niemu w około; bo mię do gniewu wzruszyło, mówi Pan.
18 “Makhalidwe anu ndi zochita zanu zakubweretserani zimenezi. Chimenechi ndiye chilango chanu. Nʼchowawa kwambiri! Nʼcholasa mpaka mu mtima!”
Droga twoja i postępki twoje to uczyniły tobie; toć złość twoja przyniosła, że to jest gorzkie, a że przenika aż do serca twego.
19 Mayo, mayo, ndikumva kupweteka! Aa, mtima wanga ukupweteka, ukugunda kuti thi, thi, thi. Sindingathe kukhala chete. Pakuti ndamva kulira kwa lipenga; ndamva mfuwu wankhondo.
O wnętrzności moje, wnętrzności moje! boleść cierpię. O osierdzia moje! trwoży się we mnie serce moje, nie zamilczę; bo głos trąby słyszysz, duszo moja! i okrzyk wojenny.
20 Tsoka limatsata tsoka linzake; dziko lonse lasanduka bwinja. Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa, mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.
Porażka za porażką ogłasza się, spustoszona będzie zaiste wszystka ziemia; nagle spustoszone będą namioty moje, i opony moje w okamgnieniu.
21 Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo, ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?
Dokądże widzieć będę chorągiew, i słyszeć głos trąby?
22 Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru; iwo sandidziwa. Iwo ndi ana opanda nzeru; samvetsa chilichonse. Ali ndi luso lochita zoyipa, koma sadziwa kuchita zabwino.”
Bo głupi lud mój nie zna mię, synowie niemądrzy i nierozumni są; mądrzy są do czynienia złego, ale dobrze czynić nie umieją.
23 Ndinayangʼana dziko lapansi, ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu; ndinayangʼana thambo, koma linalibe kuwala kulikonse.
Spojrzęli na ziemię, a oto jest niepozorna i próżna; jeżeli na niebo, nie masz na niem światłości.
24 Ndinayangʼana mapiri, ndipo ankagwedezeka; magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.
Spojrzęli na góry, a oto się trzęsą, i wszystkie pagórki chwieją się.
25 Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu; mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.
Spojrzęli, a oto niemasz człowieka, i wszelkie ptastwo niebieskie odleciało.
26 Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu; mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.
Spojrzęli, a oto pole urodzajne jest pustynią, a wszystkie miasta jego zburzone są od oblicza Pańskiego, i od oblicza gniewu zapalczywości jego.
27 Yehova akuti, “Dziko lonse lidzasanduka chipululu komabe sindidzaliwononga kotheratu.
Bo tak mówi Pan: Spustoszona będzie wszystka ziemia, wszakże końca jeszcze nie uczynię.
28 Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira ndipo thambo lidzachita mdima, pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima, ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”
Nad tem ziemia kwilić będzie, a niebiosa w górze zaćmią się, przeto, żem mówił, com umyślił, a nie żałuję, ani się odwrócę od tego.
29 Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi, anthu a mʼmizinda adzathawa. Ena adzabisala ku nkhalango; ena adzakwera mʼmatanthwe mizinda yonse nʼkuyisiya; popanda munthu wokhalamo.
Przed grzmotem jeźdźców i strzelających z łuku uciecze wszystko miasto; wejdą do gęstych obłoków, i na skały wstąpią. Wszystkie miasta opuszczone będą, a nie będzie, ktoby w nich mieszkał.
30 Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja! Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira ndi kuvalanso zokometsera zagolide? Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera, ukungodzivuta chabe. Zibwenzi zako zikukunyoza; zikufuna kuchotsa moyo wako.
A ty zburzona będąc cóż uczynisz? Choćbyś się ubrała w szarłat, choćbyś się ozdobiła ozdobą złotą, choćbyś też oblicze twe przyprawiła barwiczką, próżno się stroisz; wzgardzą tobą zalotnicy twoi, a duszy twojej szukać będą.
31 Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka, kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba. Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu. Atambalitsa manja awo nʼkumati, “Kalanga ife! Tikukomoka. Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”
Bom słyszał głos jako rodzącej, uciski jako pierworodzącej, głos córki Syońskiej narzekającej, a załamującej ręce swe, mówiąc: Biada mnie teraz! bo ustała dusza moja dla morderców.

< Yeremiya 4 >