< Yeremiya 38 >

1 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
Potem so Matánov sin Šefatjá, Pašhúrjev sin Gedaljá, Šelemjájev sin Juhál in Malkijájajev sin Pašhúr slišali besede, ki jih je Jeremija govoril vsemu ljudstvu, rekoč:
2 “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
»Tako govori Gospod: ›Kdor preostaja v tem mestu, bo umrl pod mečem, z lakoto in s kužno boleznijo, toda kdor gre naprej h Kaldejcem, bo živel, kajti svoje življenje bo imel za plen in bo živel.‹
3 Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
Tako govori Gospod: ›To mesto bo zagotovo izročeno v roko kralja babilonske vojske, ki ga bo zavzel.‹«
4 Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
Zato so princi rekli kralju: »Rotimo te, naj bo ta človek usmrčen, kajti on tako slabi roke bojevnikov, ki preostajajo v tem mestu in roke vsega ljudstva, ko jim govori takšne besede, kajti ta človek ne išče blaginje tega ljudstva, temveč škodo.«
5 Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
Potem je kralj Sedekíja rekel: »Glejte, v vaši roki je, kajti kralj ni tisti, ki lahko stori kakršnokoli stvar zoper vas.«
6 Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
Potem so prijeli Jeremija in ga vrgli v odprtino jame Malkijája, sina Hameleha, ki je bila na dvorišču ječe in Jeremija so spustili dol z vrvmi. Tam v jami pa ni bilo vode, ampak blato. Tako se je Jeremija pogreznil v blato.
7 Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
Torej ko je Ebed Meleh, Etiopijec, eden izmed evnuhov, ki je bil v kraljevi hiši, slišal, da so Jeremija vtaknili v jamo; kralj je takrat sedel v Benjaminovih velikih vratih;
8 Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
je Ebed Meleh odšel naprej iz kraljeve hiše in kralju spregovoril, rekoč:
9 “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
»Moj gospod kralj, ti možje so storili zlo v vsem, kar so storili preroku Jeremiju, ki so ga vrgli v jamo, in verjetno bo umrl zaradi lakote na kraju, kjer je, kajti v mestu ni več kruha.«
10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
Potem je kralj ukazal Etiopijcu Ebed Melehu, rekoč: »Vzemi od tod trideset mož s seboj in dvigni preroka Jeremija iz jame, preden umre.«
11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
Tako je Ebed Meleh s seboj vzel može in odšel v kraljevo hišo pod zakladnico in od tam vzel stara zakrpana oblačila in stare cunje ter jih z vrvmi spustil dol v jamo k Jeremiju.
12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
Etiopijec Ebed Meleh je rekel Jeremiju: »Deni si ta stara zakrpana oblačila in stare cunje pod svoja ramena pod vrvi.« Jeremija je tako storil.
13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
Tako so Jeremija potegnili gor z vrvmi in ga vzeli iz jame in Jeremija je ostal na dvorišču ječe.
14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
Potem je kralj Sedekíja poslal in vzel preroka Jeremija k sebi v tretji vhod, ki je v Gospodovi hiši. Kralj je rekel Jeremiju: »Vprašal te bom stvar, ničesar ne prikrij pred menoj.«
15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
Potem je Jeremija rekel Sedekíju: »Če ti to razglasim, mar me ne boš zagotovo usmrtil? In če ti dam nasvet, mar mi boš prisluhnil?«
16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
Tako je kralj Sedekíja na skrivnem prisegel Jeremiju, rekoč: » Kakor živi Gospod, ki nam je naredil to dušo, te ne bom usmrtil niti te ne bom dal v roko teh mož, ki ti strežejo po življenju.«
17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
Potem je Jeremija rekel Sedekíju: »Tako govori Gospod, Bog nad bojevniki, Izraelov Bog: ›Če boš zagotovo šel naprej k princem babilonskega kralja, potem bo tvoja duša živela in to mesto ne bo sežgano z ognjem in živel boš ti in tvoja hiša,
18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
toda če ne boš šel naprej k princem babilonskega kralja, potem bo to mesto dano v roke Kaldejcem in požgali ga bodo z ognjem in ne boš pobegnil iz njihove roke.«
19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
Kralj Sedekíja pa je rekel Jeremiju: »Bojim se Judov, ki so prebegnili h Kaldejcem, da me ne bi izročili v njihovo roko in bi se mi posmehovali.«
20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
Toda Jeremija je rekel: »Ne bodo te izročili. Ubogaj, rotim te, glas Gospoda, ki ti ga govorim. Tako bo dobro s teboj in tvoja duša bo živela.
21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
Toda če zavrneš iti naprej, je to beseda, ki mi jo je pokazal Gospod:
22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
›Glej, vse ženske, ki so preostale v hiši Judovega kralja, bodo privedene k princem babilonskega kralja in te ženske bode rekle: ›Tvoji prijatelji so te zavedli in prevladali zoper tebe. Tvoja stopala so pogreznjena v blato in oni so se umaknili nazaj.‹
23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
Tako bodo privedli ven vse tvoje žene in tvoje otroke h Kaldejcem in ne boš ušel iz njihove roke, temveč boš zajet z roko babilonskega kralja in povzročil boš, da bo to mesto sežgano z ognjem.‹«
24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
Potem je Sedekíja rekel Jeremiju: »Naj noben človek ne izve o teh besedah in ne boš umrl.
25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
Toda če princi slišijo, da sem govoril s teboj in pridejo k tebi in ti rečejo: ›Razglasi nam sedaj, kaj si rekel kralju, ne skrivaj tega pred nami in ne bomo te usmrtili; in tudi kaj je kralj rekel tebi.‹
26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
Potem jim boš rekel: ›Svojo ponižno prošnjo sem predstavil pred kraljem, da mi ne bi povzročil, da se vrnem v Jonatanovo hišo, da bi tam umrl.‹
27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
Potem so prišli vsi princi k Jeremiju in ga vprašali in ta jim je povedal glede na vse te besede, ki jih je kralj zapovedal. Tako so prenehali govoriti z njim, kajti zadeva ni bila zaznana.
28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.
Tako je Jeremija prebival na dvorišču ječe do dne, ko je bil Jeruzalem zavzet. Bil je tam, ko je bil Jeruzalem zavzet.

< Yeremiya 38 >