< Yeremiya 38 >

1 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
UShefathiya indodana kaMathani, loGedaliya indodana kaPashuri, loJukali indodana kaShelemiya, loPashuri indodana kaMalikiya, sebezwile amazwi uJeremiya ayewakhuluma kubo bonke abantu esithi:
2 “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
Itsho njalo iNkosi: Osala kulumuzi uzakufa ngenkemba, ngendlala, langomatshayabhuqe wesifo; kodwa ophuma aye kumaKhaladiya uzaphila, ngoba uzakuba lempilo yakhe ibe yimpango, aphile.
3 Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
Itsho njalo iNkosi: Lumuzi uzanikelwa isibili esandleni sebutho lenkosi yeBhabhiloni, elizawuthumba.
4 Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
Iziphathamandla zasezisithi enkosini: Ake abulawe lumuntu, ngoba ngalindlela uyekethisa izandla zamadoda empi asele kulumuzi, lezandla zabo bonke abantu, ngokukhuluma kibo amazwi anje; ngoba lumuntu kadingi ukuthula kwalababantu, kodwa okubi.
5 Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
Inkosi uZedekhiya yasisithi: Khangela, usesandleni senu, ngoba inkosi kayilakho okuphambene lani ngalutho.
6 Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
Basebemthatha uJeremiya, bamphosela emgodini kaMalikiya indodana yenkosi, owawusegumeni lentolongo, bamehlisa uJeremiya ngamagoda; kwakungelamanzi emgodini, kodwa udaka; uJeremiya wasetshona odakeni.
7 Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
Kwathi uEbedimeleki umEthiyophiya indoda umthenwa, owayesendlini yenkosi, esizwa ukuthi uJeremiya bamfake emgodini (lapho inkosi yayihlezi esangweni lakoBhenjamini),
8 Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
uEbedimeleki waphuma endlini yenkosi, wakhuluma lenkosi esithi:
9 “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
Nkosi yami, nkosi, abantu laba benzile okubi ngakho konke abakwenze kuJeremiya umprofethi, abamphosele emgodini, ngoba uzakufa endaweni yakhe ngenxa yendlala, ngoba kakusekho isinkwa emzini.
10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
Inkosi yasimlaya uEbedimeleki umEthiyophiya, isithi: Thatha lapha amadoda angamatshumi amathathu ngaphansi kwesandla sakho, umenyule uJeremiya umprofethi emgodini engakafi.
11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
Ngakho uEbedimeleki wathatha amadoda ngaphansi kwesandla sakhe, wangena endlini yenkosi waze waba ngaphansi kwesiphala, wathatha khona izidwedwe ezidabukileyo lezidwedwe ezigugileyo, wazehlisela kuJeremiya emgodini ngamagoda.
12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
UEbedimeleki umEthiyophiya wasesithi kuJeremiya: Ake ufake izidwedwe ezidabukileyo lezigugileyo ngaphansi kwamakhwapha akho ngaphansi kwamagoda. UJeremiya wasesenza njalo.
13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
Basebemdonsa uJeremiya ngamagoda, bamenyula emgodini. UJeremiya wasehlala egumeni lentolongo.
14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
Inkosi uZedekhiya yasithuma yathatha uJeremiya umprofethi yamusa kuye, ekungeneni kwesithathu okusendlini yeNkosi. Inkosi yasisithi kuJeremiya: Ngizakubuza udaba, ungangifihleli lutho.
15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
UJeremiya wasesithi kuZedekhiya: Uba ngikutshela, kawuyikungibulala lokungibulala yini? Loba ngikweluleka, kawuyikungilalela.
16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
Inkosi uZedekhiya yasifunga kuJeremiya ekusithekeni isithi: Kuphila kukaJehova owasenzela lumphefumulo: Isibili kangiyikukubulala, futhi isibili kangiyikukunikela esandleni salamadoda adinga umphefumulo wakho.
17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
UJeremiya wasesithi kuZedekhiya: Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu wamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Uba uphuma isibili uye kuziphathamandla zenkosi yeBhabhiloni, umphefumulo wakho uzaphila, lalumuzi kawuyikutshiswa ngomlilo; uzaphila wena lendlu yakho.
18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
Kodwa uba ungaphumi uye kuziphathamandla zenkosi yeBhabhiloni, lumuzi uzanikelwa esandleni samaKhaladiya, awutshise ngomlilo; lawe kawuyikuphunyuka esandleni sawo.
19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
Inkosi uZedekhiya yasisithi kuJeremiya: Ngiyawesaba amaJuda ahlubukele kumaKhaladiya, hlezi anginikele esandleni sawo, angiklolodele.
20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
UJeremiya wasesithi: Kawayikukunikela; ake ulalele ilizwi leNkosi njengalelo engilikhuluma kuwe, khona kukulungele, futhi umphefumulo wakho uzaphila.
21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
Kodwa uba usala ukuphuma, yileli ilizwi iNkosi engibonise lona lokuthi:
22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
Khangela-ke, bonke abesifazana abasele endlini yenkosi yakoJuda bazakhitshelwa kuziphathamandla zenkosi yeBhabhiloni, bathi: Abangane bakho bakukhuthazile, bakwehlula; inyawo zakho zitshone odakeni; babuyele emuva.
23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
Njalo azakhuphela abafazi bonke bakho lamadodana akho kumaKhaladiya; lawe kawuyikuphunyuka esandleni sawo, kodwa uzabanjwa ngesandla senkosi yeBhabhiloni, lalumuzi uzawutshisa ngomlilo.
24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
UZedekhiya wasesithi kuJeremiya: Kakungabi khona umuntu owaziyo lamazwi, khona ungayikufa.
25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
Kodwa nxa iziphathamandla zisizwa ukuthi ngikhulume lawe, zize kuwe zithi kuwe: Ake usitshele, ubusithini enkosini, ungakufihli kithi, khona kasiyikukubulala; njalo inkosi ikhulumeni kuwe;
26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
uzakuthi-ke kuzo: Mina ngiwise ukuncenga kwami phambi kwenkosi ukuthi ingangibuyiseli endlini kaJonathani ukuze ngifele khona.
27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
Zasezifika zonke iziphathamandla kuJeremiya, zambuza; yena waziphendula njengawo wonke lamazwi inkosi ewalayileyo. Zasezithula kuye, ngoba udaba lwalungezwakali.
28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.
UJeremiya wasehlala egumeni lentolongo kwaze kwaba lusuku iJerusalema eyathunjwa ngalo; wayekhona lapho iJerusalema ithunjwa.

< Yeremiya 38 >