< Yeremiya 38 >

1 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
Forsothe Safacie, sone of Nathan, and Jedelie, sone of Fassur, and Jothal, sone of Selemye, and Fassour, sone of Melchie, herden the wordis whiche Jeremye spak to al the puple,
2 “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
`and seide, The Lord seith these thingis, Who euer dwellith in this citee, schal die bi swerd, and hungur, and pestilence; but he that flieth to Caldeis, shal lyue, and his soule schal be hool and lyuynge.
3 Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
The Lord seith these thingis, This citee to be bitakun schal be bitakun in to the hond of the oost of the kyng of Babiloyne, and he schal take it.
4 Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
And the princes seiden to the kyng, We preien, that this man be slayn; for of bifore castyng he discoumfortith the hondis of men werriours, that dwelliden in this citee, and the hondis of al the puple, and spekith to hem bi alle these wordis. For whi this man sekith not pees to this puple, but yuel.
5 Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
And kyng Sedechie seide, Lo! he is in youre hondis, for it is not leueful that the kyng denye ony thing to you.
6 Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
Therfor thei token Jeremye, and castiden hym doun in to the lake of Elchie, sone of Amalech, which was in the porche of the prisoun; and thei senten doun Jeremye bi cordis in to the lake, wherynne was no watir, but fen; therfor Jeremye yede doun in to the filthe.
7 Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
Forsothe Abdemalech Ethiopien, a chast man and oneste, herde, that was in the kyngis hous, that thei hadden sent Jeremye in to the lake; sotheli the king sat in the yate of Beniamyn.
8 Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
And Abdemalech yede out of the kyngis hous, and spak to the kyng,
9 “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
and seide, My lord the kyng, these men diden yuele alle thingis, what euer thingis thei diden ayens Jeremye, the profete, sendynge hym in to the lake, that he die there for hungur; for whi looues ben no more in the citee.
10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
Therfor the kyng comaundide to Abdemelech Ethiopien, and seide, Take with thee thretti men fro hennus, and reise thou Jeremye, the profete, fro the lake, bifor that he die.
11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
Therfor whanne Abdemelech hadde take men with hym, he entride in to the hous of the kyng, that was vndur the celer; and he took fro thennus elde clothis, and elde ragges, that weren rotun; and he sente tho doun to Jeremye, in to the lake, bi cordis.
12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
And Abdemelech Ethiopien seide to Jeremye, Putte thou elde clothis, and these to-rent and rotun thingis vndur the cubit of thin hondis, and on the cordis. Therfor Jeremye dide so.
13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
And thei drowen out Jeremye with cordis, and ledden hym out of the lake. Forsothe Jeremye dwellide in the porche of the prisoun.
14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
And kyng Sedechie sente, and took hym Jeremye, the profete, at the thridde dore that was in the hous of the Lord. And the kyng seide to Jeremye, Y axe of thee a word; hide thou not ony thing fro me.
15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
Forsothe Jeremye seide to Sedechie, If Y telle to thee, whether thou schalt not sle me? And if Y yyue councel to thee, thou schalt not here me.
16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
Therfor Sedechie the king swoor to Jeremye priueli, and seide, The Lord lyueth, that maad to vs this soule, Y schal not sle thee, and Y schal not bitake thee in to the hondis of these men, that seken thi lijf.
17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
And Jeremye seide to Sedechie, The Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, If thou goest forth, and goest out to the princes of the kyng of Babiloyne, thi soule schal lyue, and this citee schal not be brent with fier, and thou schalt be saaf, thou and thin hous.
18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
Forsothe if thou goest not out to the princes of the kyng of Babiloyne, this citee schal be bitakun in to the hondis of Caldeis; and thei schulen brenne it with fier, and thou schalt not ascape fro the hond of hem.
19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
And kyng Sedechie seide to Jeremye, Y am angwischid for the Jewis that fledden ouer to Caldeis, lest perauenture Y be bitakun in to the hondis of hem, and thei scorne me.
20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
Forsothe Jeremye answeride, and seide to hym, Thei schulen not bitake thee; Y biseche, here thou the vois of the Lord, which Y schal speke to thee, and it schal be wel to thee, and thi soule schal lyue.
21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
That if thou wolt not go out, this is the word which the Lord schewide to me, Lo!
22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
alle the wymmen, that weren left in the hous of the kyng of Juda, schulen be led out to the princes of the kyng of Babiloyne; and tho wymmen schulen seie, Thi pesible men disseyueden thee, and hadden the maistrye ayens thee; thei drenchiden thee in filthe, and thi feet in slidirnesse, and yeden awei fro thee.
23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
And alle thi wyues and thi sones schulen be led out to Caldeis, and thou schalt not ascape the hondis of hem; but thou schalt be bitakun in to the hondis of the kyng of Babiloyne, and he schal brenne this citee bi fier.
24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
Therfore Sedechie seide to Jeremye, No man wite these wordis, and thou schalt not die.
25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
Sotheli if the princes heren, that Y spak with thee, and comen to thee, and seien to thee, Schewe thou to vs what thou spakest with the kyng, hide thou not fro vs, and we schulen not sle thee; and what the kyng spak with thee,
26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
thou schalt seie to hem, Knelyngli Y puttide forth my preiris bifore the kyng, that he schulde not comaunde me to be led ayen in to the hous of Jonathan, and Y schulde die there.
27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
Therfor alle the princes camen to Jeremye, and axiden hym; and he spak to hem bi alle the wordis whiche the kyng hadde comaundid to hym, and thei ceessiden fro hym; for whi no thing was herd.
28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.
Therfor Jeremye dwellide in the porche of the prisoun, til to the dai wherynne Jerusalem was takun; and it was don, that Jerusalem schulde be takun.

< Yeremiya 38 >