< Yeremiya 38 >

1 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
And he heard Shephatiah [the] son of Mattan and Gedaliah [the] son of Pashhur and Jucal [the] son of Shelemiah and Pashhur [the] son of Malkijah the words which Jeremiah [was] speaking to all the people saying.
2 “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
Thus he says Yahweh the [one who] remains in the city this he will die by the sword by famine and by pestilence and the [one who] goes out to the Chaldeans (and he will live *Q(K)*) and it will belong to him life his to plunder and he will live.
3 Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
Thus he says Yahweh certainly it will be given the city this in [the] hand of [the] army of [the] king of Babylon and he will capture it.
4 Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
And they said the officials to the king let him be put to death please the man this for since he [is] making drop [the] hands of [the] men of war who remain - in the city this and [the] hands of all the people by speaking to them according to the words these that - the man this not he [is] seeking for welfare for the people this that except for harm.
5 Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
And he said the king Zedekiah there! he [is] in hand your for not the king he is able you anything.
6 Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
And they took Jeremiah and they threw him into the cistern of - Malkijah [the] son of the king which [was] in [the] courtyard of the guard and they let down Jeremiah with ropes and in the cistern there not [was] water that except mud and he sank Jeremiah in the mud.
7 Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
And he heard Ebed Melech the Cushite a man a court-official and he [was] in [the] house of the king that they had put Jeremiah into the cistern and the king [was] sitting in [the] gate of Benjamin.
8 Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
And he went out Ebed Melech from [the] house of the king and he spoke to the king saying.
9 “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
O lord my the king they have done evil the men these all that they have done to Jeremiah the prophet whom they have thrown into the cistern and he died in it because of famine for there not [is] the food yet in the city.
10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
And he commanded the king Ebed Melech the Cushite saying take in hand your from here thirty men and you will bring up Jeremiah the prophet from the cistern before he will die.
11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
And he took - Ebed Melech the men in hand his and he went [the] house of the king to under the storehouse and he took from there worn out things of (clothes *Q(K)*) and worn out things of rags and he let down them to Jeremiah into the cistern with ropes.
12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
And he said Ebed Melech the Cushite to Jeremiah put please [the] worn out things of the clothes and the rags under [the] joints of hands your from under to [the] ropes and he did Jeremiah thus.
13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
And they drew out Jeremiah with ropes and they brought up him from the cistern and he remained Jeremiah in [the] courtyard of the guard.
14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
And he sent the king Zedekiah and he brought Jeremiah the prophet to him to an entrance third which [was] in [the] house of Yahweh and he said the king to Jeremiah [am] about to ask I you a matter may not you hide from me anything.
15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
And he said Jeremiah to Zedekiah if I will tell to you ¿ not certainly will you put to death me and if I will counsel you not you will listen to me.
16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
And he swore the king Zedekiah to Jeremiah in secrecy saying [by] [the] life of Yahweh (*Q(K)*) who he has made for us the life this if I will put to death you and if I will give you in [the] hand of the men these who [are] seeking life your.
17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
And he said Jeremiah to Zedekiah thus he says Yahweh [the] God of hosts [the] God of Israel certainly [if] you will go out to [the] commanders of [the] king of Babylon and you will live self your and the city this not it will be burned with fire and you will live you and household your.
18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
And if not you will go out to [the] commanders of [the] king of Babylon and it will be given the city this in [the] hand of the Chaldeans and they will burn it with fire and you not you will escape from hand their.
19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
And he said the king Zedekiah to Jeremiah I [am] dreading the Jews who they have fallen to the Chaldeans lest they should give me in hand their and they will deal wantonly with me.
20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
And he said Jeremiah not they will give listen please - to [the] voice of Yahweh to [that] which I [am] speaking to you so it may go well for you so it may live self your.
21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
And if [are] refusing you to go out this [is] the thing which he has shown me Yahweh.
22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
And there! all the women who they are left in [the] house of [the] king of Judah [are] about to be brought out to [the] commanders of [the] king of Babylon and they [will be] saying they misled you and they prevailed to you [the] people of peace your they are sunk in the mire feet your they have turned backwards.
23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
And all wives your and children your [people will] bring out to the Chaldeans and you not you will escape from hand their for by [the] hand of [the] king of Babylon you will be captured and the city this it will burn with fire.
24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
And he said Zedekiah to Jeremiah anyone may not he know in the words these and not you will die.
25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
And if they will hear the officials that I have spoken with you and they will come to you and they will say to you tell! please to us what? did you say to the king may not you hide [it] from us and not we will put to death you and what? did he say to you the king.
26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
And you will say to them [was] making fall I supplication my before the king to not to send back me [the] house of Jonathan to die there.
27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
And they came all the officials to Jeremiah and they asked him and he told to them according to all the words these which he had commanded the king and they kept silent from him for not it had been heard the matter.
28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.
And he remained Jeremiah in [the] courtyard of the guard until [the] day when it was captured Jerusalem. And it was just when it was captured Jerusalem.

< Yeremiya 38 >