< Yeremiya 38 >

1 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
And Shephatiah the son of Mattan, and Gedaliah the son of Pashur, and Jucal the son of Shelemiah, and Pashur the son of Malchijah, heard the words that Jeremiah had spoken unto all the people, saying,
2 “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
Thus saith Jehovah: He that remaineth in this city shall die by the sword, by the famine, and by the pestilence; but he that goeth forth to the Chaldeans shall live; and he shall have his life for a prey, and shall live.
3 Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
Thus saith Jehovah: This city shall certainly be given into the hand of the king of Babylon's army, and he shall take it.
4 Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
And the princes said unto the king, Let this man, we pray thee, be put to death; for why should he weaken the hands of the men of war that remain in this city, and the hands of all the people, in speaking to them according to these words? for this man seeketh not the welfare of this people, but the hurt.
5 Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
And king Zedekiah said, Behold, he is in your hand; for the king is not he that can do a thing against you.
6 Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
Then they took Jeremiah, and cast him into the dungeon of Malchijah the son of Hammelech, which was in the court of the guard, and they let down Jeremiah with cords. And in the dungeon there was no water, but mire; and Jeremiah sank in the mire.
7 Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
And Ebed-melech the Ethiopian, a eunuch who was in the king's house, heard that they had put Jeremiah in the dungeon — now the king was sitting in the gate of Benjamin,
8 Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
— and Ebed-melech went forth out of the king's house, and spoke to the king, saying,
9 “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
My lord, O king, these men have done evil in all that they have done to the prophet Jeremiah, whom they have cast into the dungeon; and he will die by reason of the famine in the place where he is; for there is no more bread in the city.
10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
And the king commanded Ebed-melech the Ethiopian, saying, Take from hence thirty men with thee, and take up Jeremiah the prophet out of the dungeon, before he die.
11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
And Ebed-melech took the men under his order, and went into the house of the king under the treasury, and took thence old shreds and worn-out clothes, and let them down by cords into the dungeon to Jeremiah.
12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
And Ebed-melech the Ethiopian said to Jeremiah, Put, I pray, [these] old shreds and rags under thine armholes under the cords. And Jeremiah did so.
13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
And they drew up Jeremiah with cords, and brought him up out of the dungeon; and Jeremiah remained in the court of the guard.
14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
And king Zedekiah sent and took the prophet Jeremiah unto him, into the third entry that is in the house of Jehovah; and the king said unto Jeremiah, I will ask thee a thing: hide nothing from me.
15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
And Jeremiah said unto Zedekiah, If I declare [it] unto thee, wilt thou not certainly put me to death? and if I give thee counsel, thou wilt not hearken unto me.
16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
And king Zedekiah swore secretly unto Jeremiah, saying, [As] Jehovah liveth, that made us this soul, I will not put thee to death, neither will I give thee into the hand of these men that seek thy life.
17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
And Jeremiah said unto Zedekiah, Thus saith Jehovah the God of hosts, the God of Israel: If thou wilt freely go forth to the king of Babylon's princes, then thy soul shall live, and this city shall not be burned with fire; and thou shalt live, and thy house.
18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
But if thou wilt not go forth to the king of Babylon's princes, then shall this city be given into the hand of the Chaldeans, and they shall burn it with fire, and thou shalt not escape out of their hand.
19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
And king Zedekiah said unto Jeremiah, I am afraid of the Jews that have deserted to the Chaldeans, lest they give me over into their hand, and they mock me.
20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
And Jeremiah said, They shall not give [thee] over. Hearken, I beseech thee, unto the voice of Jehovah, in that which I speak unto thee; so shall it be well unto thee, and thy soul shall live.
21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
But if thou refuse to go forth, this is the word which Jehovah hath shewn me:
22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
Behold, all the women that are left in the king of Judah's house shall be brought forth to the king of Babylon's princes; and they shall say, Thy familiar friends have set thee on, and have prevailed over thee; thy feet are sunk in the mire, they are turned away back.
23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
And they shall bring out all thy wives and thy children to the Chaldeans, and thou shalt not escape out of their hand; for thou shalt be taken by the hand of the king of Babylon, and thou shalt cause this city to be burned with fire.
24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
And Zedekiah said unto Jeremiah, Let no man know of these words, and thou shalt not die.
25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
And if the princes hear that I have talked with thee, and they come unto thee, and say unto thee, Declare unto us now what thou hast said unto the king, hide it not from us, and we will not put thee to death; and what hath the king said unto thee?
26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
then thou shalt say unto them, I presented my supplication before the king, that he would not cause me to return to Jonathan's house, to die there.
27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
— And all the princes came to Jeremiah, and asked him; and he told them according to all these words that the king had commanded. And they withdrew quietly from him; for the matter was not reported.
28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.
And Jeremiah remained in the court of the guard until the day that Jerusalem was taken.

< Yeremiya 38 >