< Yeremiya 38 >

1 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
Now it came to the ears of Shephatiah, the son of Mattan, and Gedaliah, the son of Pashhur, and Jucal, the son of Shelemiah, and Pashhur, the son of Malchiah, that Jeremiah had said to all the people,
2 “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
These are the words of the Lord: Whoever goes on living in this town will come to his death by the sword or through need of food or by disease: but whoever goes out to the Chaldaeans will keep his life out of the power of the attackers and be safe.
3 Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
The Lord has said, This town will certainly be given into the hands of the army of the king of Babylon, and he will take it.
4 Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
Then the rulers said to the king, Let this man be put to death, because he is putting fear into the hearts of the men of war who are still in the town, and into the hearts of the people, by saying such things to them: this man is not working for the well-being of the people, but for their damage.
5 Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
Then Zedekiah the king said, See, he is in your hands: for the king was not able to do anything against them.
6 Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
So they took Jeremiah and put him into the water-hole of Malchiah, the king's son, in the place of the armed watchmen: and they let Jeremiah down with cords. And in the hole there was no water, but wet earth: and Jeremiah went down into the wet earth.
7 Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
Now it came to the ears of Ebed-melech the Ethiopian, an unsexed servant in the king's house, that they had put Jeremiah into the water-hole; the king at that time being seated in the doorway of Benjamin:
8 Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
And Ebed-melech went out from the king's house and said to the king,
9 “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
My lord the king, these men have done evil in all they have done to Jeremiah the prophet, whom they have put into the water-hole; and he will come to his death in the place where he is through need of food: for there is no more bread in the town.
10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
Then the king gave orders to Ebed-melech the Ethiopian, saying, Take with you three men from here and get Jeremiah out of the water-hole before death overtakes him.
11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
So Ebed-melech took the men with him and went into the house of the king, to the place where the clothing was kept, and got from there old clothing and bits of old cloth, and let them down by cords into the water-hole where Jeremiah was.
12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
And Ebed-melech the Ethiopian said to Jeremiah, Put these bits of old cloth under your arms under the cords. And Jeremiah did so.
13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
So pulling Jeremiah up with the cords they got him out of the water-hole: and Jeremiah was kept in the place of the armed watchmen.
14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
Then King Zedekiah sent for Jeremiah the prophet and took him into the rulers' doorway in the house of the Lord: and the king said to Jeremiah, I have a question to put to you; keep nothing back from me.
15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
Then Jeremiah said to Zedekiah, If I give you the answer to your question, will you not certainly put me to death? and if I make a suggestion to you, you will not give it a hearing.
16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
So King Zedekiah gave his oath to Jeremiah secretly, saying, By the living Lord, who gave us our life, I will not put you to death, or give you up to these men who are desiring to take your life.
17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
Then Jeremiah said to Zedekiah, These are the words of the Lord, the God of armies, the God of Israel: If you go out to the king of Babylon's captains, then you will have life, and the town will not be burned with fire, and you and your family will be kept from death:
18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
But if you do not go out to the king of Babylon's captains, then this town will be given into the hands of the Chaldaeans and they will put it on fire, and you will not get away from them.
19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
And King Zedekiah said to Jeremiah, I am troubled on account of the Jews who have gone over to the Chaldaeans, for fear that they may give me up to them and they will put me to shame.
20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
But Jeremiah said, They will not give you up: be guided now by the word of the Lord as I have given it to you, and it will be well for you, and you will keep your life.
21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
But if you do not go out, this is what the Lord has made clear to me:
22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
See, all the rest of the women in the house of the king of Judah will be taken out to the king of Babylon's captains, and these women will say, Your nearest friends have been false to you and have got the better of you: they have made your feet go deep into the wet earth, and they are turned away back from you.
23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
And they will take all your wives and your children out to the Chaldaeans: and you will not get away out of their hands, but will be taken by the hands of the king of Babylon: and this town will be burned with fire.
24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
Then Zedekiah said to Jeremiah, Let no man have knowledge of these words, and you will not be put to death.
25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
But if it comes to the ears of the rulers that I have been talking with you, and they come and say to you, Give us word now of what you have said to the king and what the king said to you, keeping nothing back and we will not put you to death;
26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
Then you are to say to them, I made my request to the king, that he would not send me back to my death in Jonathan's house.
27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
Then all the rulers came to Jeremiah, questioning him: and he gave them an answer in the words the king had given him orders to say. So they said nothing more to him; for the thing was not made public.
28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.
So Jeremiah was kept in the place of the armed watchmen till the day when Jerusalem was taken.

< Yeremiya 38 >