< Yeremiya 36 >

1 Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
I Judas konge Jojakims, Josias' sønns fjerde år kom dette ord til Jeremias fra Herren:
2 “Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
Ta dig en bokrull og skriv i den alle de ord jeg har talt til dig om Israel og Juda og alle hedningefolkene fra den dag da jeg først talte til dig, fra Josias' dager og like til denne dag!
3 Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
Kanskje Judas hus vil merke sig all den ulykke jeg tenker å gjøre dem, så de kan vende om, hver fra sin onde vei, og jeg kan forlate dem deres misgjerning og deres synd.
4 Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
Da kalte Jeremias til sig Baruk, Nerijas sønn, og Baruk skrev efter Jeremias' munn alle de ord som Herren hadde talt til ham, i en bokrull.
5 Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
Og Jeremias talte til Baruk og sa: Jeg er forhindret, jeg kan ikke komme til Herrens hus.
6 Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
Men gå du dit og les av rullen som du har skrevet efter min munn, Herrens ord op for folket i Herrens hus på en fastedag! Også for hele Juda, som kommer fra sine byer, skal du lese den.
7 Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
Kanskje de vil legge sin ydmyke bønn frem for Herrens åsyn og vende om, hver fra sin onde vei; for stor er den vrede og harme som Herren har uttalt over dette folk.
8 Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
Og Baruk, Nerijas sønn, gjorde alt som profeten Jeremias hadde pålagt ham, og leste Herrens ord op av boken i Herrens hus.
9 Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
For i Judas konge Jojakims, Josias' sønns femte år, i den niende måned, blev det ropt ut at alt folket i Jerusalem og alt folket som var kommet fra Judas byer til Jerusalem, skulde faste for Herrens åsyn.
10 Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
Da leste Baruk op av boken Jeremias' ord i Herrens hus, i statsskriveren Gemarjas, Safans sønns kammer i den øvre forgård, ved inngangen til den nye port i Herrens hus, mens alt folket hørte på.
11 Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
Da Mikaja, sønn av Gemarja, sønn av Safan, hørte alle Herrens ord bli lest op av boken,
12 anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
gikk han ned til kongens hus, til statsskriverens kammer, og der fant han alle høvdingene sittende: statsskriveren Elisama og Delaja, Sjemajas sønn, og Elnatan, Akbors sønn, og Gemarja, Safans sønn, og Sedekias, Hananjas sønn, og alle de andre høvdinger.
13 Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
Og Mikaja fortalte dem om alle de ord han hadde hørt da Baruk leste op av boken for folket.
14 Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
Da sendte alle høvdingene Jehudi, sønn av Netanja, sønn av Selemja, sønn av Kusi, til Baruk og sa: Ta med dig rullen som du leste op av for folket, og kom hit! Og Baruk, Nerijas sønn, tok rullen med sig og kom til dem.
15 Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
De sa til ham: Sett dig ned og les den for oss! Og Baruk leste den for dem.
16 Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
Og da de hørte alle ordene, vendte de sig forferdet til hverandre, og de sa til Baruk: Vi må melde kongen alt dette.
17 Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
Så spurte de Baruk: Fortell oss hvorledes du skrev alle disse ord efter hans munn!
18 Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
Baruk svarte: Med sin munn foresa han mig alle disse ord, og jeg skrev dem i boken med blekk.
19 Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
Da sa høvdingene til Baruk: Gå og skjul dig, du og Jeremias, og la ingen vite hvor I er!
20 Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
Så gikk de inn til kongen i forgården, men rullen la de ned i statsskriveren Elisamas kammer; og de fortalte alt dette til kongen.
21 Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
Da sendte kongen Jehudi avsted for å hente rullen, og han hentet den fra statsskriveren Elisamas kammer, og Jehudi leste den op for kongen og alle høvdingene som stod hos kongen.
22 Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
Kongen satt i vinterhuset, for det var den niende måned, og det brente ild i et fyrfat foran ham,
23 Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
og da Jehudi hadde lest op tre eller fire blad, skar kongen rullen i stykker med en pennekniv og kastet den på ilden i fyrfatet, inntil hele rullen var fortært av ilden der i fyrfatet.
24 Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
Og de forferdedes ikke og sønderrev ikke sine klær, hverken kongen eller nogen av hans tjenere som hørte alle disse ord,
25 Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
og skjønt Elnatan og Delaja og Gemarja inntrengende bad kongen at han ikke skulde brenne rullen, hørte han ikke på dem.
26 Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
Så bød kongen Jerahme'el, kongesønnen, og Seraja, Asriels sønn, og Selemja, Abde'els sønn, å gripe skriveren Baruk og profeten Jeremias; men Herren skjulte dem.
27 Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Da kom Herrens ord til Jeremias, efterat kongen hadde brent op rullen med de ord Baruk hadde skrevet efter Jeremias' munn:
28 “Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
Ta dig en annen rull og skriv i den alle de forrige ord, de som stod i den forrige rull, som Judas konge Jojakim brente op!
29 Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
Og om Judas konge Jojakim skal du si: Så sier Herren: Du brente denne rull og sa: Hvorfor skrev du i den således: Babels konge skal komme og ødelegge dette land og utrydde mennesker og dyr av det?
30 Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
Derfor sier Herren så om Judas konge Jojakim: Han skal ikke ha nogen ætling som skal sitte på Davids trone, og hans døde kropp skal ligge slengt bort, utsatt for heten om dagen og for kulden om natten.
31 Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
Og jeg vil hjemsøke ham og hans ætt og hans tjenere for deres misgjerning, og jeg vil la komme over dem og over Jerusalems innbyggere og over Judas menn all den ulykke jeg har forkynt dem uten at de vilde høre.
32 Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.
Da tok Jeremias en annen rull og gav den til skriveren Baruk, Nerijas sønn, og han skrev i den efter Jeremias' munn alle ordene i den bok som Judas konge Jojakim hadde brent i ilden, og det blev til dem ennu lagt mange lignende ord.

< Yeremiya 36 >