< Yeremiya 36 >
1 Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Ie amy faha-efa-tao’ Iehoiakime ana’ Iosia, mpanjaka’ Iehodày, le niheo am’ Iirmeà ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe:
2 “Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
Mangalà boke-peleke le sokiro ao ze hene tsara nivolañako ty am’ Israele naho Iehodà vaho o hene fifeheañeo sikal’ amy andro nivolañeko ama’o faha’ Iosiay pake henanekeo.
3 Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
Kera ho janjiñe’ ty anjomba’ Iehodà ze hene hankàñe nisafirieko hanoañe; ke sindre hibalintoa amo sata’ rati’eo ondatio, vaho hapoko ty hakeo’ iareo naho o tahi’ iareoo.
4 Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
Aa le kinoi’ Iirmeà t’i Baroke ana’ i Nerià; vaho sinoki’ i Baroke am-boke-pelek’ ao boak’ am-palie’ Iirmeà ze hene tsara nitsara’ Iehovà ama’e.
5 Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
Le hoe t’Iirmeà amy Baroke: sinebañe iraho tsy himoak’ añ’anjomba’ Iehovà ao;
6 Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
akia arè, mamakia amy boke-peleke nanokira’o o tsara’ Iehovà boak’am-bavakooy, an-dravembia’ ondaty añ’anjomba’ Iehovà ao ami’ty androm-pililirañe; mbore vakio an-dravembia’ Iehoda miakatse o rova’eo iaby.
7 Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
Hera hibanabana soloho am’ Iehovà, naho songa hibalik’ amo sata-rati’eo; amy te miforoforo ty haviñera’ Iehovà naho ty fifomboa’e nitaroñeñe am’ ondaty retoa.
8 Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
Aa le nanoe’ i Baroke ana’ i Neria i hene nandilia’ Iirmeà mpitoky ama’ey, le vinaki’e amy bokey ty tsara’ Iehovà añ’anjomba’ Iehovà ao.
9 Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
Aa ie ami’ty volam-paha-sive’ i taom-paha-lime’ Iehoiakime ana’ Iosia mpanjaka’ Iehoday, le nambarañe fililirañe añatrefa’ Iehovà: naho nimb’ e Ierosalaime mb’eo ondati’ Ierosalaimeo naho ze hene boak’ amo rova’ Iehodao.
10 Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
Le vinaki’ i Baroke amy bokey o saontsi’ Iirmeào, añ’anjomba’ Iehovà, añ’efe’ i Gemaria ana’ i Safane mpanokitse, an-kiririsa ambone, amy fimoahan-Dalam-bey Vao’ i anjomba’ Iehovàiy, an-dravembia’ ze fonga ondaty.
11 Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
Aa ie jinanji’ i Mikaieho ana’ i Gemaria, ana’ i Safane ze hene tsara’ Iehovà boak’ amy bokey,
12 anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
le nizotso mb’ añ’ anjomba’ i mpanjakay mb’eo, añ’ efe’ o mpanokitseo; le heheke te hene niambesatse ao o roandriañeo— i Elisama, mpanokitse, naho Delaia ana’ i Semaià, naho i Elnatane ana i Akbore, naho i Gemaria, ana’ i Safane, naho i Tsidkia ana’ i Kananià, naho o roandriañe iabio.
13 Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
Le tinaro’ i Mikaieho ze hene tsara jinanji’e amy Baroke, ie namaky i bokey an-dravembia’ ondatio.
14 Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
Aa le nampihitrife’ o roandriañe iabio t’Iehodý ana’ i Netanià ana’ i Selemia, ana’ i Kosy, mb’ amy Baroke hanoa’e ty hoe: Endeso am-pità’o i peleke vinaki’o an-dravembia’ ondatioy, vaho mb’etoy. Aa le rinambe’ i Baroke ana’ i Neria am-pità’e amy zao i pelekey vaho nimb’ am’ iereo ao.
15 Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
Le hoe iereo ama’e: Miambesara vaho ivakio an-dravembia’ay. Aa le vinaki’ i Baroke an-dravembia’ iareo.
16 Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
Ie amy zao, naho hene jinanji’ iereo i tsaray, le nifampitolik’ an-kahembañañe vaho nanao ty hoe amy Baroke: Tsy mete tsy hene taroñe’ay amy mpanjakay o tsara zao.
17 Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
Le nañontane i Baroke iereo, ty hoe, Ehe, isaontsio, akore ty nanokira’o o tsara iaby zao? boak’am-palie’e hao?
18 Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
Le hoe ty natoi’ i Baroke: Hene sinaontsi’e amako am-palie o tsara retoañe, vaho sinokiko an-drano-mainte amo bokeo.
19 Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
Le hoe o roandriañeo amy Baroke, Akia, mietaha, ihe naho Iirmeà, vaho ko apo’o ho fohi’ ondaty te aia.
20 Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
Aa le nimoak’ amy mpanjakay an-kiririsa’e ao iereo; fa nado’ iareo añ’efe’ i Elisama mpanokitse ao i pelekey; vaho tinaro’ iareo an-dravembia’ i mpanjakay i tsara iabiy.
21 Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
Aa le nampihitrife’ i mpanjakay t’Iehody hangalake i pelekey; le nalae’e añ’efe’ i Elisame mpanokitse ao naho vinaki’ Iehody an-dravembia’ i mpanjakay vaho an-dravembia’ o roandriañe iaby nijohañe marine i mpanjakaio.
22 Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
Niambesatse añ’anjomban’ asotry ao i mpanjakay amy volam-pahasivey, ie nisodotse añ’atrefa’e eo ty toko-pamindroañe.
23 Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
Aa naho nivakia’ Iehody ty fange’e efatse ndra telo, le tinori’e amy kelelahi’ey vaho nahifi’e amy afo amy tokoiy, ampara’ te fonga niforototoe’ ty afo amy toko-pamindroañey i pelekey.
24 Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
F’ie tsy nahahembañe iareo, leo raike tsy nandriatse sikiñe, ndra i mpanjakay ndra o mpitoro’e nahajanjiñe i tsaraio.
25 Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
Mbore nihalaly amy mpanjakay t’i Elnatane naho i Delaia vaho i Gemaria tsy hampiforehete’e i pelekey; fe tsy hinao’e;
26 Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
vaho linili’ i mpanjakay t’Ierakmeele, ana’ i mpanjakay, naho i Seraià, ana’ i Azriele, naho i Selemià, ana’ i Abdile ty hitsepake i Baroke mpanokitse naho Iirmeà mpitoky; f’ie naeta’ Iehovà.
27 Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Ie finorototo’ i mpanjakay i pelekey, naho o tsara’ sinoki’ i Baroke am-palie’ Iirmeào le niheo am’ Iirmeà ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe:
28 “Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
Mangalà peleke indraike, le hene isokiro i tsara tamy peleke valoha’e nisodore’ i mpanjaka’ Iehodaiiy.
29 Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
Le hoe ty ho saontsie’o am’ Iehoiakime mpanjaka’ Iehodà: Hoe t’Iehovà: Fa noroa’o i pelekey, amy ty hoe, Ino ty nanokira’o ao ty hoe te tsy mete tsy hivotrak’ atoy ty mpanjaka’ i Bavele handrotsake o tane atoio, vaho ho mongore’e ze fonga ondaty naho hare ama’e?
30 Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
Aa le hoe t’Iehovà ty am’ Iehoiakime mpanjaka’ Iehodà, t’ie tsy hanan-kiambesatse amy fiambesa’ i Davidey; vaho havokovoko an-tariñandroke ey ty lolo’e te handro, vaho amy fanalay te haleñe.
31 Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
Le ho liloveko, ie naho o tiri’eo naho o mpitoro’eo ty amo hakeo’ iareoo, vaho hafetsako am’ iereo naho amo mpimone’ Ierosalaimeo, naho am’ondati’ Iehodao, ze hene hankàñe nivolañako; o tsy hinao’ iereoo.
32 Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.
Aa le nandrambe peleke ila’e t’Iirmeà, le natolo’e amy Baroke, mpanokitse, ana’ i Nerià; vaho hene sinoki’e ao boak’am-palie’ Iirmeà o tsara’ i peleke noroa’ Iehoiakime mpanjaka’ Iehodaio; mbore tinovo’e tsara maro manahak’ izay.