< Yeremiya 36 >

1 Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Et il arriva dans la quatrième année de Joakim, fils de Josias, roi de Juda, que cette parole fut adressée à Jérémie par le Seigneur, disant:
2 “Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
Prends un rouleau de livre et tu y écriras toutes les paroles que je t’ai dites contre Israël, et contre Juda, et contre tous les peuples, depuis le jour où je t’ai parlé, depuis les jours de Josias, jusqu’à ce jour;
3 Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
Pour voir si par hasard, la maison de Juda apprenant tous les maux que moi je pense leur faire, chacun reviendra de ses voies très mauvaises; et je lui pardonnerai son iniquité et son péché.
4 Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
Jérémie appela donc Baruch, fils de Nérias, et Baruch écrivit, sorties de la bouche de Jérémie sur un rouleau de livre, toutes les paroles que le Seigneur lui avait dites.
5 Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
Et Jérémie ordonna à Baruch, disant: Moi je suis enfermé, et je ne puis entrer dans la maison du Seigneur.
6 Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
Entre donc, toi, et lis d’après le rouleau dans lequel tu as écrit, sorties de ma bouche, les paroles du Seigneur, le peuple entendant dans la maison du Seigneur, au jour de jeûne; de plus tous ceux de Juda qui viennent de leurs cités entendant, tu les leur liras;
7 Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
Pour voir si par hasard leur prière tombera devant le Seigneur, et s’ils reviendront chacun de sa voie très mauvaise; parce que grande est la fureur et l’indignation avec laquelle a parlé le Seigneur contre son peuple.
8 Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
Et Baruch, fils de Nérias, fit selon tout ce que lui avait ordonné Jérémie, le prophète, lisant dans le rouleau les paroles du Seigneur, dans la maison du Seigneur.
9 Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
Or il arriva en la cinquième année de Joakim, fils de Josias, roi de Juda, dans le neuvième mois, qu’on publia un jeûne en présence du Seigneur, pour tout le peuple dans Jérusalem et pour toute la multitude qui avait afflué des cités de Juda dans Jérusalem.
10 Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
Et Baruch lut dans le rouleau les paroles de Jérémie dans la maison du Seigneur, dans la chambre du trésor de Gamarias, fils de Saphan, le scribe, dans le vestibule supérieur, à l’entrée de la porte neuve de la maison du Seigneur, tout le peuple entendant.
11 Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
Et lorsque Michée, fils de Gamarias, fils de Saphan, eut entendu toutes les paroles du Seigneur écrites dans le livre,
12 anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
Il descendit dans la maison du roi, en la chambre du trésor du scribe; et voilà que là tous les princes étaient assis: Elisama le Scribe, et Dalaïas, fils de Séméias, et Elnathan, fils d’Achobor, et Gamarias, fils de Saphan, et Sédécias, fils d’Hananias, et tous les princes.
13 Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
Et Michée leur rapporta toutes les paroles qu’il avait entendues de Baruch, lisant dans le rouleau aux oreilles du peuple.
14 Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
C’est pourquoi tous les princes envoyèrent à Baruch Judi, fils de Nathanias, fils de Sélémias, fils de Chusi, disant: Prends en ta main le rouleau que tu as lu, le peuple entendant, et viens. Baruch, fils de Nérias, prit donc le rouleau en sa main, et vint à eux.
15 Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
Et ils lui dirent: Assieds-toi, et lis ces choses à nos oreilles. Et Baruch lut à leurs oreilles.
16 Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
Ainsi, lorsqu’ils eurent entendu toutes les paroles, ils se regardèrent les uns les autres avec étonnement, et ils dirent à Baruch: Nous devons rapporter au roi toutes ces paroles.
17 Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
Et ils l’interrogèrent, disant: Déclare-nous comment tu as écrit toutes ces paroles sorties de la bouche de Jérémie.
18 Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
Or Baruch leur dit: Il me disait de sa bouche toutes ces paroles comme s’il les avait lues; et moi je les écrivais dans le rouleau avec de l’encre.
19 Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
Et les princes dirent à Baruch: Va, et cache-toi, ainsi que Jérémie, et que personne ne sache où vous serez.
20 Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
Et ils entrèrent chez le roi dans le vestibule; quant au rouleau, ils l’avaient déposé dans la chambre du trésor d’Elisama, le scribe, et ils rapportèrent, le roi entendant, toutes les paroles.
21 Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
Et le roi envoya Judi afin de prendre le rouleau; lequel l’ayant pris de la chambre du trésor d’Elisama, le scribe, le lut, le roi entendant, ainsi que tous les princes qui étaient autour du roi.
22 Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
Or le roi était assis dans sa maison d’hiver au neuvième mois; et un brasier était placé devant lui, plein de charbons ardents.
23 Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
Lorsque Judi eut lu trois ou quatre pages, le roi coupa le rouleau avec le canif du scribe, et le jeta dans le feu qui était sur le brasier, jusqu’à ce que le volume entier fût consumé par le feu qui était dans le brasier.
24 Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
Et le roi et tous ses serviteurs qui entendirent toutes ces paroles, ne craignirent pas, et ne déchirèrent pas leurs vêtements.
25 Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
Mais cependant Elnathan et Dalaïas et Gamarias, s’opposèrent au roi, afin qu’il ne brûlât point le livre; et il ne les écouta point.
26 Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
Et le roi ordonna à Jérémiel, fils d’Amélech, et à Saraïas, fils d’Ezriel, et à Sélémias, fils d’Abdéel, de prendre Baruch, le scribe, et Jérémie, le prophète; mais le Seigneur les cacha.
27 Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Et la parole du Seigneur fut adressée à Jérémie, le prophète, après que le roi eut brûlé le rouleau et les paroles que Baruch avait écrites et qui étaient sorties de la bouche de Jérémie, disant:
28 “Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
Reprends un autre rouleau, et écris-y toutes les paroles qui étaient dans le premier rouleau qu’a brûlé Joakim, roi de Juda.
29 Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
Et à Joakim, roi de Juda, tu diras: Voici ce que dit le Seigneur: Tu as brûlé ce rouleau, disant: Pourquoi as-tu écrit dans ce livre en publiant: Soudain viendra le roi de Babylone, et il dévastera cette terre et il en fera disparaître l’homme et la bête?
30 Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur contre Joakim, roi de Juda: Il n’y aura pas de lui de prince qui s’assiéra sur le trône de David; et son cadavre sera jeté à la chaleur du jour et à la gelée de la nuit.
31 Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
Et je visiterai contre lui, et contre sa race, et contre ses serviteurs, leurs iniquités; et j’amènerai sur eux et sur les habitants de Jérusalem et sur les hommes de Juda tout le mal que je leur ai annoncé, et ils ne m’ont pas entendu.
32 Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.
Or Jérémie prit un autre rouleau et le donna à Baruch, fils de Nérias, le scribe, qui y écrivit, sorties de la bouche de Jérémie, toutes les paroles qui étaient dans le livre qu’avait brûlé Joakim, roi de Juda; et il y ajouta en outre beaucoup plus de paroles qu’il n’y en avait auparavant.

< Yeremiya 36 >