< Yeremiya 36 >

1 Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
La quatrième année de Jojakim, fils de Josias, roi de Juda, cette parole fut adressée à Jérémie de la part de Yahvé, en ces termes:
2 “Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
« Prends un rouleau de livre, et écris-y toutes les paroles que je t'ai dites contre Israël, contre Juda et contre toutes les nations, depuis le jour où je t'ai parlé, depuis l'époque de Josias jusqu'à ce jour.
3 Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
Peut-être la maison de Juda entendra-t-elle tout le mal que j'ai l'intention de lui faire, afin que chacun revienne de sa mauvaise voie, et que je pardonne son iniquité et son péché. »
4 Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
Jérémie appela Baruc, fils de Neriah, et Baruc écrivit de la bouche de Jérémie toutes les paroles de l'Éternel, qu'il lui avait dites, sur un rouleau de livre.
5 Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
Jérémie donna un ordre à Baruc, en disant: « Je suis limité. Je ne peux pas entrer dans la maison de Yahvé.
6 Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
Va donc, et lis dans le rouleau que tu as écrit de ma bouche, les paroles de l'Éternel, aux oreilles du peuple dans la maison de l'Éternel, le jour du jeûne. Tu les liras aussi aux oreilles de tous les Judéens qui sortiront de leurs villes.
7 Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
Il se peut qu'ils présentent leurs supplications à l'Éternel et que chacun revienne de sa mauvaise voie, car l'Éternel a annoncé une grande colère et une grande fureur contre ce peuple. »
8 Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
Baruc, fils de Nérija, fit tout ce que lui avait ordonné Jérémie, le prophète, en lisant dans le livre les paroles de l'Éternel, dans la maison de l'Éternel.
9 Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
Or, la cinquième année de Jojakim, fils de Josias, roi de Juda, au neuvième mois, tout le peuple de Jérusalem et tout le peuple venu des villes de Juda à Jérusalem, proclamèrent un jeûne devant Yahvé.
10 Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
Et Baruch lut les paroles de Jérémie tirées du livre dans la maison de l'Éternel, dans la chambre de Gemaria, fils de Shaphan, le scribe, dans le parvis supérieur, à l'entrée de la nouvelle porte de la maison de l'Éternel, aux oreilles de tout le peuple.
11 Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
Lorsque Michée, fils de Guemaria, fils de Shaphan, eut entendu du livre toutes les paroles de l'Éternel,
12 anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
il descendit dans la maison du roi, dans la chambre du secrétaire; et voici, tous les princes étaient assis là, Élischama, le secrétaire, Delaja, fils de Schemaeja, Elnathan, fils d'Acbor, Guemaria, fils de Shaphan, Sédécias, fils de Hanania, et tous les princes.
13 Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
Et Michée leur rapporta toutes les paroles qu'il avait entendues, lorsque Baruch lisait le livre aux oreilles du peuple.
14 Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
Alors tous les chefs envoyèrent Jehudi, fils de Nethania, fils de Shelemia, fils de Cushi, vers Baruch, en disant: « Prends en main le rouleau que tu as lu aux oreilles du peuple, et viens. » Baruch, fils de Neriah, prit le rouleau dans sa main et vint vers eux.
15 Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
Ils lui dirent: « Assieds-toi maintenant, et lis-le à notre intention. » Alors Baruch l'a lu à leur oreille.
16 Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
Or, lorsqu'ils eurent entendu toutes ces paroles, ils se tournèrent avec crainte les uns vers les autres, et dirent à Baruc:
17 Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
« Ils demandèrent à Baruc: « Dis-nous maintenant comment tu as écrit toutes ces paroles à sa bouche? ».
18 Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
Baruch leur répondit: « Il m'a dicté toutes ces paroles de sa bouche, et je les ai écrites avec de l'encre dans le livre. »
19 Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
Alors les princes dirent à Baruch: « Toi et Jérémie, allez vous cacher. Que personne ne sache où vous êtes. »
20 Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
Ils se rendirent auprès du roi dans la cour, mais ils avaient déposé le rouleau dans la chambre d'Elishama, le scribe. Ils racontèrent alors toutes ces paroles à l'oreille du roi.
21 Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
Le roi envoya Jehudi chercher le rouleau, et il le sortit de la chambre d'Elishama, le scribe. Jehudi le lut en présence du roi et de tous les princes qui se tenaient près du roi.
22 Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
Le roi était assis dans la maison d'hiver, au neuvième mois, et le feu brûlait devant lui dans le brasero.
23 Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
Lorsque Jehudi eut lu trois ou quatre colonnes, le roi les coupa avec le canif et les jeta dans le feu qui était dans le brasier, jusqu'à ce que tout le rouleau fût consumé dans le feu qui était dans le brasier.
24 Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
Le roi et ses serviteurs, qui entendirent toutes ces paroles, n'eurent pas peur et ne déchirèrent pas leurs vêtements.
25 Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
Elnathan, Delaja et Gemaria avaient fait des instances auprès du roi pour qu'il ne brûle pas le rouleau, mais il ne voulut pas les écouter.
26 Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
Le roi ordonna à Jerahmeel, fils du roi, à Seraja, fils d'Azriel, et à Shelemiah, fils d'Abdeel, d'arrêter Baruch, le scribe, et Jérémie, le prophète; mais Yahvé les cacha.
27 Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
La parole de Yahvé fut adressée à Jérémie, après que le roi eut brûlé le rouleau et les paroles que Baruc écrivit à la bouche de Jérémie, en ces termes:
28 “Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
« Prends encore un autre rouleau, et écris-y toutes les paroles antérieures qui étaient dans le premier rouleau, que Jojakim, roi de Juda, a brûlé.
29 Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
Tu diras à propos de Jojakim, roi de Juda: « Yahvé dit: Tu as brûlé ce rouleau, en disant: Pourquoi as-tu écrit: Le roi de Babylone viendra certainement détruire ce pays, et il en fera disparaître les hommes et les bêtes?
30 Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
C'est pourquoi Yahvé dit à propos de Jehoïakim, roi de Juda: « Il n'y aura personne pour s'asseoir sur le trône de David. Son cadavre sera jeté dehors, le jour à la chaleur, la nuit au gel.
31 Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
Je le punirai, lui, sa progéniture et ses serviteurs, pour leur iniquité. Je ferai venir sur eux, sur les habitants de Jérusalem et sur les hommes de Juda, tous les malheurs que j'ai prononcés contre eux, mais ils n'ont pas écouté. »'"
32 Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.
Jérémie prit un autre rouleau, et le donna à Baruc, le scribe, fils de Neriah, qui y écrivit de la bouche de Jérémie toutes les paroles du livre que Jojakim, roi de Juda, avait brûlé au feu, et beaucoup de paroles semblables y furent ajoutées.

< Yeremiya 36 >