< Yeremiya 36 >

1 Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
And it was don, in the fourthe yeer of Joachym, sone of Josie, kyng of Juda, this word was maad of the Lord to Jeremye, and seide,
2 “Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
Take thou the volym of a book, and thou schalt write therynne alle the wordis, whiche Y spake to thee ayens Israel and Juda, and ayens alle folkis, fro the dai in whiche Y spak to thee, fro the daies of Josie `til to this dai.
3 Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
If perauenture whanne the hous of Juda herith alle the yuels whiche Y thenke to do to hem, ech man turne ayen fro his worste weye, and Y schal be merciful to the wickidnesse and synne of hem.
4 Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
Therfor Jeremye clepide Baruk, the sone of Nerye; and Baruk wroot of the mouth of Jeremye in the volym of a book alle the wordis of the Lord, whiche he spak to hym.
5 Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
And Jeremye comaundide to Baruk, and seide, Y am closid, and Y may not entre in to the hous of the Lord.
6 Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
Therfor entre thou, and rede of the book, in which thou hast write of my mouth the wordis of the Lord, in hering of the puple, in the hous of the Lord, in the dai of fastyng; ferthermore and in heryng of al Juda, that comen fro her citees, thou schalt rede to hem;
7 Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
if perauenture the preier of hem falle in the siyt of the Lord, and eche man turne ayen fro his worste weie; for whi the strong veniaunce and indignacioun is greet, which the Lord spak ayens this puple.
8 Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
And Baruk, the sone of Nerie, dide aftir alle thingis, which Jeremye, the prophete, comaundide to hym; and he redde of the book the wordis of the Lord, in the hous of the Lord.
9 Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
Forsothe it was doon, in the fyueth yeer of Joachym, sone of Josie, kyng of Juda, in the nynthe monethe, thei prechiden fastynge in the siyt of the Lord, to al the puple in Jerusalem, and to al the multitude, that cam togidere fro the citees of Juda in to Jerusalem.
10 Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
And Baruc redde of the volym the wordis of Jeremye, in the hous of the Lord, in the treserie of Gamarie, sone of Saphan, scryuen, in the hiyere porche, in the entring of the newe yate of the hous of the Lord, in audience of al the puple.
11 Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
And whanne Mychie, the sone of Gamarie, sone of Saphan, hadde herd alle the wordis of the Lord,
12 anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
of the book, he yede doun in to the hous of the kyng, to the treserye of the scryuen. And lo! alle the princes saten there, Elisama, the scryuen, and Dalaie, the sone of Semeye, and Elnathan, the sone of Achabor, and Gamarie, the sone of Saphan, and Sedechie, the sone of Ananye, and alle princes.
13 Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
And Mychee telde to hem alle the wordis, whiche he herde Baruc redynge of the book, in the eeris of the puple.
14 Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
Therfor alle the princes senten to Baruc Judi, the sone of Nathathie, sone of Selemye, sone of Chusi, and seiden, Take in thin hond the book, of which thou reddist in audience of the puple, and come thou. Therfor Baruc, the sone of Nereie, took the book in his hoond, and cam to hem.
15 Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
And thei seiden to hym, Sitte thou, and rede these thingis in oure eeris; and Baruc redde in the eeris of hem.
16 Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
Therfor whanne thei hadden herd alle the wordis, thei wondriden ech man to his neiybore, and thei seiden to Baruc, Owen we to telle to the kyng alle these wordis?
17 Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
And thei axiden hym, and seiden, Schewe thou to vs, hou thou hast write alle these wordis of his mouth.
18 Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
Forsothe Baruc seide to hem, Of his mouth he spak, as redynge to me, alle these wordis; and Y wroot in a book with enke.
19 Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
And alle the princes seiden to Baruc, Go, be thou hid, thou and Jeremye; and no man wite where ye ben.
20 Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
And thei entriden to the kyng, in to the halle; forsothe thei bitoken the book to be kept in to the treserie of Elisame, the scryuen. And thei telden alle the wordis, in audience of the kyng.
21 Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
Therfor the kyng sente Judi, that he schulde take the book. Which took the book fro the treserie of Elysame, the scryuen, and redde in audience of the kyng, and of alle the princes, that stoden aboute the kyng.
22 Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
Forsothe the kyng sat in the wyntir hous, in the nynthe monethe; and a panne ful of coolis was set bifore hym.
23 Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
And whanne Judi hadde red thre pagyns, ethir foure, he kittide it with the knyf of a scryueyn, and castide in to the fier, `that was in the panne, til al the book was wastid bi the fier, that was on the panne.
24 Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
And the kyng and alle hise seruauntis, that herden alle these wordis, dredden not, nethir to-renten her clothis.
25 Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
Netheles Elnathan, and Dalaie, and Gamarie ayenseiden the kyng, that he schulde not brenne the book; and he herde not hem.
26 Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
And the kyng comaundide to Jeremyel, sone of Amalech, and to Saraie, sone of Esreel, and to Selemye, sone of Abdehel, that thei schulden take Baruc, the writer, and Jeremye, the profete; forsothe the Lord hidde hem.
27 Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
And the word of the Lord was maad to Jeremye, the profete, aftir that the kyng hadde brent the book and wordis, whiche Baruc hadde write of Jeremyes mouth;
28 “Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
and he seid, Eft take thou another book, and write therynne alle the former wordis, that weren in the firste book, which Joachym, the kyng of Juda, brente.
29 Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
And thou schalt seie to Joachym, kyng of Juda, The Lord seith these thingis, Thou brentist that book, and seidist, What hast thou write therynne, tellynge, The kyng of Babiloyne schal come hastynge, and schal distrie this lond, and schal make man and beeste to ceesse therof?
30 Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
Therfor the Lord seith these thingis ayens Joachym, king of Juda, Noon schal be of hym, that schal sitte on the seete of Dauid; and his careyn schal be cast forth to the heete bi dai, and to the forst bi niyt.
31 Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
And Y schal visite ayens hym, and ayens his seed, and ayens hise seruauntis, her wickidnessis. And Y schal bryng on hem, and on the dwelleris of Jerusalem, and on the men of Juda, al the yuel which Y spak to hem, and thei herden not.
32 Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.
Forsothe Jeremye took an other book, and yaf it to Baruc, the writer, the sone of Nerie, which wroot therynne of Jeremyes mouth alle the wordis of the book, which book Joachym, the kyng of Juda, hadde brent bi fier; and ferthermore many mo wordis weren addid than weren bifore.

< Yeremiya 36 >