< Yeremiya 36 >

1 Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Stalo se pak léta čtvrtého Joakima syna Joziášova, krále Judského, stalo se slovo toto k Jeremiášovi od Hospodina, řkoucí:
2 “Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
Vezmi sobě knihu, a zapiš do ní všecka slova, kteráž jsem mluvil tobě proti Izraelovi, a proti Judovi, i všechněm národům od toho dne, jakž jsem mluvíval s tebou, ode dnů Joziášových, až do dne tohoto,
3 Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
Zdali aspoň uslyšíce dům Judský o všem tom zlém, kteréž já myslím učiniti jim, navrátí se jeden každý z cesty své zlé, abych odpustil nepravost jejich a hřích jejich.
4 Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
Protož zavolal Jeremiáš Bárucha syna Neriášova, i sepsal Báruch do knihy z úst Jeremiášových všecka slova Hospodinova, kteráž mluvil jemu.
5 Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
Potom přikázal Jeremiáš Báruchovi, řka: Já zápověd maje, nemohu jíti do domu Hospodinova.
6 Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
Protož jdi ty, a čti v knize této, což jsi napsal z úst mých, slova Hospodinova, při přítomnosti lidu v domě Hospodinově, v den postu, též také při přítomnosti všech Judských, kteříž by se z měst svých sešli, čti je,
7 Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
Zda by snad poníženě a pokorně modléce se před Hospodinem, i navrátili by se jeden každý z cesty své zlé; neboť jest veliký hněv a prchlivost, v níž mluvil Hospodin proti lidu tomuto.
8 Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
I učinil Báruch syn Neriášův všecko, jakž přikázal jemu Jeremiáš prorok, čta v knize té slova Hospodinova v domě Hospodinově.
9 Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
Stalo se pak léta pátého za Joakima syna Joziášova, krále Judského, měsíce devátého, že vyhlásili půst před Hospodinem všemu lidu v Jeruzalémě, a všemu lidu, kteříž se byli sešli z měst Judských do Jeruzaléma.
10 Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
I četl Báruch z knihy slova Jeremiášova v domě Hospodinově, v pokoji Gemariáše syna Safanova, písaře, na síni hořejší, u dveří brány domu Hospodinova nové, při přítomnosti všeho lidu.
11 Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
Když pak vyslyšel Micheáš syn Gemariášův, syna Safanova, všecka slova Hospodinova z té knihy,
12 anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
Hned šel do domu královského, do pokoje kancléřova, a aj, tam všecka knížata seděla: Elisama ten kancléř, a Delaiáš syn Semaiášův, a Elnatan syn Achborův, a Gemariáš syn Safanův, a Sedechiáš syn Chananiášův, i všecka knížata.
13 Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
A oznámil jim Micheáš všecka slova, kteráž slyšel, když četl Báruch v knize při přítomnosti lidu.
14 Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
Protož poslala všecka knížata k Báruchovi Judu syna Netaniášova, syna Selemiášova, syna Chuzova, aby řekl: Tu knihu, v níž jsi četl při přítomnosti lidu, vezmi do ruky své a poď. I vzal Báruch syn Neriášův tu knihu do ruky své, a přišel k nim.
15 Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
Kteříž řekli jemu: Seď medle a čti ji před námi. I četl Báruch před nimi.
16 Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
Stalo se pak, když uslyšeli všecka slova ta, že předěšeni byli všickni, a řekli Báruchovi: Jistotně oznámíme králi všecka slova tato.
17 Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
Potom otázali se Bárucha, řkouce: Oznam již nám, jak jsi všecka slova ta sepsal z úst jeho?
18 Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
Jimž řekl Báruch: Z úst svých pravil mi všecka slova tato, a já psal jsem na knihách černidlem.
19 Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
Tedy řekla ta knížata Báruchovi: Jdi schovej se ty i Jeremiáš, ať žádný neví, kde jste.
20 Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
Potom vešli k králi na síň, když tu knihu schovati dali v pokoji Elisama kancléře, a oznámili králi všecka slova ta.
21 Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
I poslal král Judu, aby vzal tu knihu. Kterýžto vzal ji z pokoje Elisama kancléře, a četl ji Juda při přítomnosti krále, a při přítomnosti všech knížat stojících před králem.
22 Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
Král pak seděl v domě, v němž v zimě býval, měsíce devátého, a na ohništi před ním hořelo.
23 Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
Tedy stalo se, jakž jen přečtl Juda tři listy neb čtyři, že pořezal ji škriptorálem, a házel na oheň, kterýž byl na ohništi, až shořela všecka kniha ta ohněm tím, kterýž byl na ohništi.
24 Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
Ale neulekli se, aniž roztrhl roucha svá král a všickni služebníci jeho, kteříž slyšeli všecka slova ta.
25 Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
Nýbrž ještě když Elnatan a Delaiáš a Gemariáš přimlouvali se k králi, aby nepálil té knihy, tedy neuposlechl jich.
26 Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
Ale přikázal král Jerachmeelovi synu královu, a Saraiášovi synu Azrielovu, a Selemiášovi synu Abdeelovu, aby jali Bárucha písaře a Jeremiáše proroka. Ale skryl je Hospodin.
27 Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Stalo se pak slovo Hospodinovo k Jeremiášovi, když spálil král tu knihu a slova, kteráž byl sepsal Báruch z úst Jeremiášových, řkoucí:
28 “Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
Vezmi sobě zase knihu jinou, a napiš na ní všecka slova první, kteráž byla v té knize prvnější, kterouž spálil Joakim král Judský.
29 Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
O Joakimovi pak králi Judském rci: Takto praví Hospodin: Ty jsi spálil knihu tuto, pravě: Proč jsi psal v ní, řka: Jistotně přitáhne král Babylonský, a zkazí zemi tuto, a vyhladí z ní lidi i hovada?
30 Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
Protož takto praví Hospodin o Joakimovi králi Judském: Nebude míti, kdo by seděl na stolici Davidově, a tělo jeho mrtvé bude vyvrženo na horko ve dne a na mráz v noci.
31 Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
Nebo trestati budu na něm, a na semeni jeho, i na služebnících jeho nepravost jejich, a uvedu na ně, a na obyvatele Jeruzalémské, i na muže Judské všecko to zlé, o kterémž jsem mluvíval jim, a neposlouchali.
32 Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.
I vzal Jeremiáš knihu jinou, a dal ji Báruchovi synu Neriášovu, písaři, kterýž sepsal do ní z úst Jeremiášových všecka slova té knihy, kterouž byl spálil Joakim král Judský ohněm. A ještě přidáno jest k těm slovům mnoho těm podobných.

< Yeremiya 36 >