< Yeremiya 35 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti:
Słowo, które doszło do Jeremiasza od PANA za dni Joakima, syna Jozjasza, króla Judy, mówiące:
2 “Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”
Idź do domu Rekabitów, porozmawiaj z nimi i wprowadź ich do domu PANA, do jednej z komnat, i daj im wino do picia.
3 Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu.
Zabrałem więc ze sobą Jaazaniasza, syna Jeremiasza, syna Chabasiniasza, jego braci, wszystkich jego synów i cały dom Rekabitów;
4 Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo.
I wprowadziłem ich do domu PANA, do komnaty synów Chanana, syna Jigdaliasza, męża Bożego, która [była] obok komnaty książęcej nad komnatą Maasejasza, syna Szalluma, stróża progu.
5 Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”
Potem postawiłem przed synami domu Rekabitów czasze pełne wina i kubki i powiedziałem do nich: Pijcie wino.
6 Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale.
Lecz oni odpowiedzieli: Nie pijemy wina, bo Jonadab, syn Rekaba, nasz ojciec, nakazał nam, mówiąc: Nie pijcie wina, ani wy, ani wasi synowie, aż na wieki.
7 Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’
Nie budujcie też domów ani nie obsiewajcie nasieniem, nie sadźcie winnic ani nie posiadajcie [żadnej], ale mieszkajcie w namiotach przez wszystkie wasze dni, abyście żyli przez wiele dni na powierzchni ziemi, w której jesteście przybyszami.
8 Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo
Byliśmy więc posłuszni głosowi Jonadaba, syna Rekaba, naszego ojca, we wszystkim, co nam nakazał: nie piliśmy wina przez wszystkie nasze dni, my, nasze żony, nasi synowie i nasze córki;
9 kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu.
I nie budowaliśmy sobie domów do zamieszkania ani nie mieliśmy winnicy ani pola, ani siewu.
10 Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula.
Ale mieszkamy w namiotach; byliśmy posłuszni i postępujemy zgodnie ze wszystkim, co nam nakazał Jonadab, nasz ojciec.
11 Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”
A gdy Nabuchodonozor, król Babilonu, nadciągnął do [naszej] ziemi, powiedzieliśmy: Chodźcie, wejdźmy do Jerozolimy przed wojskiem Chaldejczyków i przed wojskiem Syryjczyków. Zostaliśmy więc w Jerozolimie.
12 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti,
Wówczas doszło słowo PANA do Jeremiasza mówiące:
13 “Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova.
Tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Idź i powiedz Judejczykom i mieszkańcom Jerozolimy: Czy nie przyjmiecie pouczenia, by słuchać moich słów? – mówi PAN.
14 ‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine.
Wypełniane są słowa Jonadaba, syna Rekaba, które przykazał swoim synom, aby nie pili wina. Nie piją go bowiem aż do dziś, bo są posłuszni przykazaniu swego ojca. Ja jednak mówiłem do was, z wczesnym wstawaniem i mówieniem, lecz nie słuchaliście mnie.
15 Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine.
Posłałem też do was wszystkie swe sługi, proroków, z wczesnym wstawaniem i przesłaniem, mówiąc: Niech każdy zawróci już ze swej złej drogi i poprawi swoje uczynki, nie chodźcie za innymi bogami ani im nie służcie, a będziecie mieszkać w tej ziemi, którą dałem wam i waszym ojcom. Ale nie nakłoniliście swego ucha ani mnie nie usłuchaliście.
16 Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.
I chociaż synowie Jonadaba, syna Rekaba, wypełnili nakaz swego ojca, który im przekazał, to jednak ten lud nie był mi posłuszny.
17 “Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’”
Dlatego tak mówi PAN, Bóg zastępów, Bóg Izraela: Oto sprowadzę na Judę i na wszystkich mieszkańców Jerozolimy całe nieszczęście, które wypowiedziałem przeciwko nim, gdyż mówiłem do nich, a nie słuchali, wołałem ich, a nie odpowiedzieli.
18 Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.”
Domowi Rekabitów Jeremiasz zaś powiedział: Tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Ponieważ byliście posłuszni nakazowi Jonadaba, waszego ojca, i przestrzegaliście wszystkich jego przykazań, i postępowaliście zgodnie ze wszystkim, co wam nakazał;
19 Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”
Dlatego tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Nie zabraknie Jonadabowi, synowi Rekaba, potomka, który by stał przede mną po wszystkie dni.

< Yeremiya 35 >