< Yeremiya 35 >
1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti:
C'est ici la parole qui fut [adressée] par l'Eternel à Jérémie, aux jours de Jéhojakim, fils de Josias Roi de Juda, en disant:
2 “Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”
Va à la maison des Récabites, et leur parle, et les fais venir en la maison de l'Eternel, dans l'une des chambres, et présente-leur du vin à boire.
3 Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu.
Je pris donc Jaazanja fils de Jérémie, fils de Habatsinja, et ses frères, et tous ses fils, et toute la maison des Récabites;
4 Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo.
Et je les fis venir dans la maison de l'Eternel, en la chambre des fils de Hanan, fils de Jigdalia, homme de Dieu, laquelle était près de la chambre des principaux; qui était sur la chambre de Mahaséja, fils de Sallum, garde des vaisseaux.
5 Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”
Et je mis devant les enfants de la maison des Récabites, des gobelets pleins de vin, et des tasses, et je leur dis: buvez du vin.
6 Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale.
Et ils répondirent: nous ne boirons point de vin; car Jéhonadab, fils de Récab notre père nous a donné un commandement, en disant: vous ne boirez point de vin, ni vous, ni vos enfants, à jamais;
7 Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’
Vous ne bâtirez aucune maison, vous ne sèmerez aucune semence, vous ne planterez aucune vigne, et vous n'en aurez point; mais vous habiterez en des tentes tous les jours de votre vie, afin que vous viviez longtemps sur la terre dans laquelle vous séjournez comme étrangers.
8 Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo
Nous avons donc obéi à la voix de Jéhonadab, fils de Récab notre père, dans toutes les choses qu'il nous a commandées, de sorte que nous n'avons point bu de vin tous les jours de notre vie, ni nous, [ni] nos femmes, ni nos fils, ni nos filles.
9 kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu.
Nous n'avons bâti aucune maison pour notre demeure, et nous n'avons eu ni vigne, ni champ, ni semence.
10 Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula.
Mais nous avons demeuré dans des tentes, et nous avons obéi, et avons fait selon toutes les choses que Jéhonadab notre père nous a commandées.
11 Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”
Mais il est arrivé que quand Nébucadnetsar Roi de Babylone est monté au pays, nous avons dit: venez, et entrons dans Jérusalem pour fuir de devant l'armée des Caldéens, et de devant l'armée de Syrie; et nous sommes demeurés dans Jérusalem.
12 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti,
Alors la parole de l'Eternel fut [adressée] à Jérémie, en disant:
13 “Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova.
Ainsi a dit l'Eternel des armées, le Dieu d'Israël: va, et dis aux hommes de Juda, et aux habitants de Jérusalem: ne recevrez-vous point d'instruction pour obéir à mes paroles? dit l'Eternel.
14 ‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine.
Toutes les paroles de Jéhonadab, fils de Récab, qu'il a commandées à ses enfants de ne boire point de vin, ont été observées, et ils n'[en] ont point bu jusques à ce jour; mais ils ont obéi au commandement de leur père; mais moi je vous ai parlé, me levant dès le matin, et parlant, et vous ne m'avez point obéi.
15 Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine.
Car je vous ai envoyé tous les Prophètes, mes serviteurs, me levant dès le matin, et les envoyant, pour vous dire: détournez-vous maintenant chacun de son mauvais train, et corrigez vos actions, et ne suivez point d'autres dieux pour les servir, afin que vous demeuriez en la terre que j'ai donnée à vous et à vos pères; mais vous n'avez point incliné vos oreilles, et ne m'avez point écouté.
16 Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.
Parce que les enfants de Jéhonadab fils de Récab ont observé le commandement de leur père, lequel il leur avait fait, et que ce peuple ne m'a point écouté;
17 “Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’”
A cause de cela l'Eternel le Dieu des armées, le Dieu d'Israël, dit ainsi: voici, je m'en vais faire venir sur Juda et sur tous les habitants de Jérusalem tout le mal que j'ai prononcé contre eux; parce que je leur ai parlé, et ils n'ont point écouté; et que je les ai appelés, et ils n'ont point répondu.
18 Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.”
Et Jérémie dit à la maison des Récabites: ainsi a dit l'Eternel des armées, le Dieu d'Israël: parce que vous avez obéi au commandement de Jéhonadab votre père, et que vous avez gardé tous ses commandements, et avez fait selon tout ce qu'il vous a commandé;
19 Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”
C'est pourquoi ainsi a dit l'Eternel des armées, le Dieu d'Israël: il n'arrivera jamais qu'il n'y ait quelqu'un appartenant à Jéhonadab fils de Récab, qui assiste devant moi tous les jours.