< Yeremiya 35 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti:
Parole adressée à Jérémie par l’Eternel au temps de Joïakim, fils de Josias, roi de Juda, en ces termes:
2 “Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”
Va trouver la famille des Rêkhabites, adresse-leur la parole, et amène-les au temple du Seigneur, dans une des salles; et là tu leur offriras du vin à boire.
3 Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu.
J’Allai donc chercher Yazania, fils de Jérémie, fils de Habacinia, avec ses frères, tous ses fils et toute la famille des Rêkhabites,
4 Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo.
et je les amenai au temple du Seigneur, dans la salle des fils de Hanan, fils de Ygdalia, l’homme de Dieu, salle qui était proche de la salle des grands et au-dessus de la salle de Masséya, fils de Challoum, le gardien du seuil.
5 Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”
Je plaçai devant les membres de la famille des Rêkhabites des calices remplis de vin et des coupes, et je leur dis: Buvez du vin.
6 Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale.
Mais ils répondirent: "Nous ne buvons pas de vin! car notre père Jonadab, fils de Rêkhab, nous l’a défendu en disant: Vous ne boirez jamais de vin, ni vous ni vos enfants.
7 Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’
Vous ne bâtirez pas non plus de maison, vous ne sèmerez pas de graines, vous ne planterez pas de vignes et ne posséderez rien de tout cela; mais vous habiterez sous des tentes pendant toute votre existence, afin que vous viviez de longs jours sur le sol où vous séjournerez.
8 Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo
Or, nous avons écouté la voix de notre père Jonadab, fils de Rêkhab, suivi toutes ses prescriptions, en nous abstenant de boire du vin notre vie durant, nous, nos femmes, nos fils et nos filles;
9 kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu.
de construire des maisons pour y demeurer, de posséder des vignes, des champs et des graines pour ensemencer.
10 Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula.
Nous avons habité sous des tentes; nous avons exécuté docilement tout ce que nous avait prescrit Jonadab, notre père.
11 Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”
Seulement, quand Nabuchodonosor, roi de Babylone, a envahi ce pays, nous nous sommes dit: Allons, retirons-nous à Jérusalem devant l’armée des Chaldéens et devant l’armée des Araméens. C’Est ainsi que nous nous sommes établis à Jérusalem."
12 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti,
Alors la parole de l’Eternel fut adressée à Jérémie en ces termes:
13 “Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova.
"Ainsi parle l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël: Va et dis aux gens de Juda et aux habitants de Jérusalem: Ne profiterez-vous pas de la leçon, en obéissant à mes commandements? dit l’Eternel.
14 ‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine.
On a exécuté les ordres de Jonadab, fils de Rêkhab, qui prescrivait à ses enfants de ne pas boire de vin: ils n’en ont pas bu jusqu’à ce jour, dociles aux recommandations de leur père, et moi, je vous ai adressé la parole chaque matin, sans relâche, sans que vous m’ayez écouté!
15 Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine.
Je vous ai envoyé tous mes serviteurs, les prophètes, sans fin ni trêve, pour vous dire: Que chacun de vous revienne de sa voie pernicieuse, amendez vos actes, ne suivez pas le culte des dieux étrangers; de la sorte, vous demeurerez sur le sol que je vous ai donné, à vous et à vos ancêtres. Mais vous n’avez point prêté l’oreille, vous ne m’avez pas écouté.
16 Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.
Les enfants de Jonadab, fils de Rêkhab, ont exécuté, eux, l’ordre que leur avait donné leur père, tandis que ce peuple ne m’a point obéi.
17 “Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’”
C’Est pourquoi l’Eternel, Dieu-Cebaot, Dieu d’Israël, parle ainsi: Voici, je vais faire fondre sur Juda et sur tous les habitants de Jérusalem tous les maux que j’ai décrétés contre eux, puisque je leur ai parlé et qu’ils n’ont point écouté, puisque je les ai appelés et qu’ils n’ont pas répondu!"
18 Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.”
Mais à la famille des Rêkhabites Jérémie dit: "Ainsi parle l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël: Puisque vous avez obéi à l’ordre de Jonadab, votre père, observé toutes ses prescriptions et exécuté tout ce qu’il vous a recommandé,
19 Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”
c’est pourquoi, dit l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël, en aucun temps, il ne manquera à Jonadab, fils de Rêkhab, des hommes pour se tenir en ma présence."

< Yeremiya 35 >