< Yeremiya 35 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti:
The word which it came to Jeremiah from with Yahweh in [the] days of Jehoiakim [the] son of Josiah [the] king of Judah saying.
2 “Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”
Go to [the] house of the Rechabites and you will speak them and you will bring them [the] house of Yahweh to one of the rooms and you will give to drink them wine.
3 Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu.
And I took Jaazaniah [the] son of Jeremiah [the] son Habazziniah and brothers his and all children his and all [the] house of the Rechabites.
4 Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo.
And I brought them [the] house of Yahweh to [the] room of [the] sons of Hanan [the] son Igdaliah [the] man of God which [was] beside [the] room of the officials which [was] from above [the] room of Maaseiah [the] son of Shallum [the] keeper of the threshold.
5 Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”
And I put before - [the] sons of [the] house of the Rechabites bowls full wine and cups and I said to them drink wine.
6 Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale.
And they said not we drink wine for Jonadab [the] son of Rechab ancestor our he commanded to us saying not you must drink wine you and children your until perpetuity.
7 Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’
And a house not you must build and seed not you must sow and a vineyard not you must plant and not it will belong to you for in tents you will dwell all days your so that you may live days many on [the] surface of the ground where you [are] sojourning there.
8 Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo
And we have listened to [the] voice of Jonadab [the] son of Rechab ancestor our to all that he commanded us to not to drink wine all days our we wives our sons our and daughters our.
9 kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu.
And to not to build houses to dwell in we and vineyard and field and seed not it belongs to us.
10 Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula.
And we have dwelt in tents and we have obeyed and we have done according to all that he commanded us Jonadab ancestor our.
11 Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”
And it was when came up Nebuchadnezzar [the] king of Babylon against the land and we said come so we may go Jerusalem because of [the] army of the Chaldeans and from before [the] army of Aram and we have dwelt in Jerusalem.
12 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti,
And it came [the] word of Yahweh to Jeremiah saying.
13 “Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova.
Thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel go and you will say to [the] man of Judah and to [the] inhabitants of Jerusalem ¿ not will you accept correction to listen to words my [the] utterance of Yahweh.
14 ‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine.
It was carried out [the] words of Jonadab [the] son of Rechab which he commanded children his to not to drink wine and not they have drunk until the day this for they have obeyed [the] commandment of ancestor their and I I have spoken to you rising early and speaking and not you have listened to me.
15 Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine.
And I sent to you all servants my the prophets - rising early and sending - saying turn back please everyone from way his evil and make good deeds your and may not you walk after gods other to serve them and dwell to the land which I gave to you and to ancestors your and not you inclined ear your and not you listened to me.
16 Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.
For they have carried out [the] sons of Jonadab [the] son of Rechab [the] commandment of ancestor their which he commanded them and the people this not they have listened to me.
17 “Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’”
Therefore thus he says Yahweh [the] God of hosts [the] God of Israel here I [am] about to bring to Judah and to all [the] inhabitants of Jerusalem all the calamity which I spoke on them because I spoke to them and not they listened and I called to them and not they answered.
18 Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.”
And to [the] house of the Rechabites he said Jeremiah thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel because that you have listened to [the] commandment of Jonadab ancestor your and you have kept all commandments his and you have done according to all that he commanded you.
19 Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”
Therefore thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel not it will be cut off a man to Jonadab [the] son of Rechab [who] will stand before me all the days.

< Yeremiya 35 >